Genesis 44 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 44:1-34

Chikho Chasiliva Mʼthumba la Benjamini

1Pambuyo pake Yosefe analamulira wantchito wa mʼnyumba mwake kuti, “Adzazire chakudya anthuwa mʼmatumba mwawo monga mmene anganyamulire, ndipo uwayikire ndalama zawo pakamwa pa matumba awowo. 2Tsono uyike chikho changa cha siliva chija, pakamwa pa thumba la wamngʼono kwambiriyu pamodzi ndi ndalama zake za chakudya” Ndipo iye anachita monga Yosefe ananenera.

3Mmawa kutacha anthu aja analoledwa kuti apite ndi abulu awo. 4Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino? 5Mwaberanji chikho chimene mbuye wanga amamweramo ndi kugwiritsa ntchito akafuna kuwombeza? Chimene mwachitachi ndi chinthu choyipa.’ ”

6Wantchito uja atawapeza ananena mawu anawuzidwa aja. 7Koma iwo anati kwa iye, “Kodi mbuye wanga mukuneneranji zimenezi? Sizingatheke ndi pangʼono pomwe kuti antchito anufe nʼkuchita zoterozo ayi! 8Paja ife pobwera kuchokera ku Kanaani tinatenga ndalama kubwezera zimene tinazipeza mʼmatumba mwathu. Ndiye pali chifukwa chanji kuti tikabe siliva kapena golide mʼnyumba mwa mbuye wanu? 9Ngati wantchito wanu wina pano atapezeka nacho chikhocho, ameneyo aphedwe ndipo ena tonsefe tidzakhala akapolo anu, mbuye wathu.”

10Iye anati, “Chabwino, tsono zikhale monga mwaneneramu. Komatu aliyense amene angapezeke nacho chikhocho adzakhala kapolo wanga, ndipo ena nonsenu muzipita mwaufulu.”

11Tsono onse anafulumira kutsitsa pansi aliyense thumba lake ndi kulitsekula. 12Kenaka anayamba kufufuza, kuyambira pa wamkulu mpaka pa wamngʼono. Ndipo chikhocho chinapezeka mʼthumba mwa Benjamini. 13Apo onse anangʼamba zovala zawo ndi chisoni. Ndipo anasenzetsa abulu katundu wawo nabwerera ku mzinda konkuja.

14Pamene Yuda ndi abale ake ankafika ku nyumba kwa Yosefe nʼkuti Yosefe akanali komweko. Ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pake. 15Yosefe anafunsa kuti, “Nʼchiyani mwachitachi? Kodi simudziwa kuti munthu ngati ine ndikhoza kuona zinthu mwakuwombeza?”

16Yuda anayankha, “Kodi tinganenenji kwa mbuye wanga? Tinena chiyani? Tingadzilungamitse bwanji? Mulungu waulula kulakwa kwa antchito anu. Ndipo tsopano ndife akapolo a mbuye wanga, ife tonse pamodzi ndi amene wapezeka ndi chikhocho.”

17Koma Yosefe anati, “Sindingachite choncho ayi! Yekhayo amene wapezeka ndi chikhocho ndi amene akhale kapolo wanga. Ena nonsenu, bwererani kwa abambo anu mu mtendere.”

18Ndipo Yuda anamuyandikira iye nati, “Chonde mbuye wanga mulole kapolo wanune ndinene mawu pangʼono kwa mbuye wanga. Musandipsere mtima, kapolo wanune, popeza inu muli ngati Farao yemwe. 19Mbuye wanga munafunsa akapolo anufe kuti, ‘Kodi muli ndi abambo anu kapena mʼbale wanu?’ 20Ndipo ife tinayankha, ‘Inde mbuye wathu, ife tili ndi abambo athu wokalamba, ndipo pali mwana wamwamuna wamngʼono amene anabadwa abambo athu atakalamba kale. Mʼbale wake anafa ndipo ndi yekhayo mʼmimba mwa amayi ake amene watsala ndipo abambo ake amamukonda.’

21“Ndipo inu munatiwuza kuti, ‘Mubwere naye kwa ine kuti ndidzamuone ndekha.’ 22Ife tinati, ‘Mbuye wathu, mnyamatayo sangasiye abambo ake, akawasiya ndiye kuti abambo akewo adzafa.’ 23Koma inu munatichenjeza kuti, ‘Pokhapokha mutabwera naye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri, simudzandionanso.’ 24Ndiye pamene tinafika kwa kapolo wanu, abambo athu tinawawuza zonse zimene munanena.

25“Abambo athu anatiwuza kuti, ‘Pitaninso mukagule kachakudya pangʼono.’ 26Koma tinati, ‘Sitingathe kupitanso. Sitingapite pokhapokha mngʼono wathuyu apite nafe chifukwa munthu uja anati sitingaonane naye ngati mngʼono wathuyu sakhala nafe.’

27“Koma kapolo wanu, abambo athu anatiwuza kuti, ‘Inu mukudziwa kuti mkazi wanga anandiberekera ana aamuna awiri. 28Mmodzi wa iwo anandisiya. Ine ndimati anadyedwa ndi chirombo popeza sindinamuonenso mpaka lero. 29Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’

30“Tsono ngati tizibwerera kwa mtumiki wanu, abambo athu popanda mnyamatayu, amene moyo wa abambo ake uli pa iyeyu, 31ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. 32Ndiponsotu ine ndinadzipereka kwa abambo anga kukhala chikole chotsimikiza kuti mnyamatayu ndidzamuteteza, ndipo ndinati, ‘Ngati sindibwerera naye mnyamatayu kwa inu, ndiye kuti ndidzakhala wochimwira inu abambo anga moyo wanga wonse.’

33“Tsono, chonde mulole kuti ine kapolo wanu nditsalire kuno kukhala kapolo wa mbuye wathu mʼmalo mwa mnyamatayu. Koma iye apite pamodzi ndi abale akewa. 34Ndingabwerere bwanji kwa abambo anga ngati sindingapite ndi mnyamatayu? Ayi! Sindifuna kukaona tsoka limene lingakagwere abambo anga.”

Bibelen på hverdagsdansk

1. Mosebog 44:1-34

Josefs sølvbæger

1Senere gav Josef sin husholder befaling om at fylde brødrenes sække med alt det korn, som æslerne kunne bære. „Sørg for at lægge de penge, de har betalt for kornet, tilbage i hver sæk!” beordrede han. 2„Og i den yngste brors sæk skal du desuden lægge mit sølvbæger.” Husholderen gjorde, som Josef havde sagt. 3Ved daggry næste morgen fik brødrene lov at tage af sted med deres æsler.

4Men de var kun lige kommet ud af byen, da Josef sagde til sin husholder: „Sæt efter dem og stands dem. Sig så til dem: ‚Hvorfor har I gengældt godt med ondt? 5Hvorfor har I taget min herres personlige sølvbæger, som han bruger til at tage varsler af? Hvordan kunne I gøre noget så usselt?’ ” 6Husholderen indhentede hurtigt brødrene og sagde det, Josef havde givet ham besked på.

7„Hvad mener du?” svarede brødrene. „Sådan noget kunne vi da aldrig finde på at gøre! 8Bragte vi måske ikke de penge tilbage, som lå oven i vores sække sidste gang? Hvorfor i alverden skulle vi stjæle guld eller sølv fra din herres hus? 9Hvis du finder bægeret hos en af os, skal vedkommende dø! Og resten af os skal være din herres slaver!”

10„Nej,” svarede husholderen. „Det er kun den, bægeret findes hos, der skal være min herres slave, I andre kan godt rejse hjem.”

11Brødrene løftede hurtigt sækkene af æslerne og åbnede dem. 12Husholderen begyndte at gennemsøge den ældste brors sæk, og sådan fortsatte han hele rækken ned til den yngste. Bægeret blev fundet i Benjamins sæk. 13Da flængede brødrene i fortvivlelse deres tøj, læssede igen deres æsler og vendte tilbage til byen. 14Josef var stadig hjemme i sit hus, da Juda og hans brødre ankom. De faldt på knæ for ham med ansigtet mod jorden.

15„Hvad er I ude på?” spurgte Josef. „Er I ikke klar over, at en mand som jeg har spåmænd, der kunne fortælle mig, hvem der stjal det?”

16Da sagde Juda: „Oh, herre, hvad skal vi sige til vores forsvar? Hvordan kan vi bevise, at vi er uskyldige? Gud har bragt vores skyld for dagens lys. Vi er nu Deres slaver—både vi og vores bror, som bægeret blev fundet hos.”

17„Nej,” svarede Josef. „Kun den, som stjal bægeret, skal være min slave. Resten af jer kan frit rejse hjem til jeres far.”

Juda tilbyder at blive slave for at redde Benjamin

18Da trådte Juda et skridt frem mod Josef og sagde: „Herre, tillad mig at tale til Dem. Hav tålmodighed med mig et øjeblik. Jeg ved, at De har magt til at dræbe mig på stedet, for De er jo som Farao selv. 19De spurgte os, herre, om vi havde en far eller en bror. 20Dertil svarede vi: ‚Ja, vores far er gammel, og han har endnu en søn derhjemme, som han fik i sin alderdom. Denne søns bror er død, så nu er han den eneste, hans mor efterlod sig. Derfor holder hans far så meget af ham.’ 21Så sagde De, herre: ‚Bring ham til mig, så jeg kan se ham!’ 22Men vi svarede: ‚Det er umuligt, herre! Drengen kan ikke forlade sin far, for hans far vil dø af sorg, hvis der sker ham noget.’ 23Men De insisterede: ‚Kom ikke tilbage, medmindre jeres yngste bror er med!’ 24Derefter rejste vi hjem til vores far og fortalte ham, hvad De havde sagt. 25Og da han senere bad os om at tage til Egypten igen og købe mere korn, 26sagde vi til ham: ‚Det kan ikke lade sig gøre, medmindre du lader vores yngste bror rejse med os. Uden ham vil vores rejse være forgæves.’

27Så sagde vores far: ‚I ved jo, at min elskede kone fødte mig to sønner. 28Den ene forsvandt. Han blev nok flået ihjel af et rovdyr, for jeg så ham aldrig igen. 29Hvis der nu også sker noget med den anden søn, dør jeg af sorg.’ 30Derfor kan De nok forstå, herre, at hvis jeg kommer hjem uden den dreng, som min far er så stærkt knyttet til, 31så dør han af sorg, og det er vi skyld i. 32Herre, jeg har personligt lovet min far at tage mig af drengen på denne rejse—ja, jeg sagde ligefrem: ‚Hvis jeg ikke bringer ham tilbage i god behold, tager jeg selv hele skylden!’ 33Herre, tillad mig derfor at blive Deres slave i stedet for drengen. Lad ham få lov at tage hjem sammen med sine brødre. 34Hvordan kan jeg tage hjem til min far uden drengen? Jeg vil ikke kunne holde ud at se min fars sorg.”