Genesis 43 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 43:1-34

Ulendo Wachiwiri wa ku Igupto

1Njala inakula kwambiri mʼdzikomo. 2Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”

3Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’ 4Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya. 5Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’ ”

6Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”

7Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”

8Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo. 9Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse. 10Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”

11Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni. 12Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa. 13Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga. 14Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”

15Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe. 16Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”

17Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe. 18Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”

19Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti, 20“Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya 21koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo. 22Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”

23Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.

24Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo. 25Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.

26Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi. 27Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”

28Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.

29Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.” 30Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.

31Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.

32Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri. 33Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa. 34Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.

La Bible du Semeur

Genèse 43:1-34

Benjamin part avec ses frères en Egypte

1La famine sévissait de plus en plus durement dans le pays. 2Quand la famille de Jacob eut mangé tout le blé rapporté d’Egypte43.2 Sans doute après une année (voir 45.6)., Jacob dit à ses fils : Retournez là-bas nous acheter un peu de vivres.

3Juda lui répondit : Cet homme nous a solennellement avertis que nous ne pourrons plus nous présenter devant lui si notre frère ne nous accompagne pas. 4Si tu laisses notre frère partir avec nous, nous irons en Egypte et nous t’achèterons des vivres. 5Mais si tu ne le laisses pas venir, nous ne partirons pas ; car cet homme nous a bien dit : « Vous ne serez pas admis en ma présence si votre frère n’est pas avec vous. »

6Israël reprit : Pourquoi m’avez-vous causé ce tort ? Aviez-vous besoin de raconter à cet homme que vous avez encore un frère ?

7Ils lui répondirent : Cet homme nous a questionnés en détail sur nous et sur notre parenté. Il nous a demandé : « Votre père vit-il encore ? Avez-vous un autre frère ? » Et nous avons répondu à ces questions. Pouvions-nous savoir qu’il nous ordonnerait de lui amener notre frère ?

8Alors Juda dit à Israël, son père : Laisse partir le jeune homme avec moi. Nous nous mettrons en route et nous irons là-bas pour pouvoir survivre. Sinon, nous mourrons tous, et nous, et toi et nos jeunes enfants. 9Je le prends sous ma responsabilité, tu m’en demanderas compte. Si je ne te le ramène pas, si je ne le fais pas revenir là, devant toi, je serai pour toujours coupable envers toi. 10Si nous n’avions pas tant tardé, nous serions déjà deux fois de retour.

11Leur père Israël leur dit : Eh bien ! Si c’est ainsi, faites ceci : Mettez dans vos bagages les meilleurs produits du pays et offrez-les à cet homme : un peu de baume et un peu de miel, de l’astragale, du laudanum, des pistaches et des amandes. 12Prenez avec vous le double de la somme voulue et restituez l’argent qui a été remis à l’entrée de vos sacs. Peut-être s’agissait-il d’une erreur. 13Emmenez votre frère et partez, retournez chez cet homme. 14Que le Dieu tout-puissant rende cet homme compatissant à votre égard. Qu’il vous rende votre autre frère ainsi que Benjamin. Quant à moi, comme je dois être privé d’enfants, que j’en sois privé !

15Alors ils se chargèrent du présent, prirent avec eux une double somme d’argent et emmenèrent Benjamin. Ainsi ils se mirent en route, se rendirent en Egypte et se présentèrent devant Joseph.

Le repas chez Joseph

16Joseph vit avec eux Benjamin, il dit alors à l’intendant qui gérait sa maison : Conduis ces gens chez moi, fais abattre une bête et qu’on l’apprête, car ces hommes mangeront avec moi à midi.

17L’intendant exécuta les ordres de son maître et conduisit ces gens à la maison de Joseph. 18Ceux-ci furent effrayés d’être introduits dans la maison de Joseph et dirent : C’est à cause de l’argent remis la dernière fois dans nos sacs qu’on nous fait venir. Ils vont débouler sur nous, tomber sur nous pour nous prendre comme esclaves et s’emparer de nos ânes.

19Ils s’approchèrent de l’intendant de la maison de Joseph et lui parlèrent à l’entrée de la maison : 20Excuse-nous, mon seigneur : en fait nous sommes déjà venus une première fois pour acheter des vivres. 21Quand nous sommes arrivés à l’étape où nous avons passé la nuit, nous avons ouvert nos sacs et chacun de nous a retrouvé son argent à l’ouverture de son sac, c’était exactement la somme que nous avions payée. Alors nous l’avons rapportée, 22et nous avons emporté avec nous une autre somme d’argent pour acheter des vivres. Nous ne savons pas qui a remis notre argent dans nos sacs !

23L’intendant répondit : Tout va bien ; ne craignez rien. C’est votre Dieu, le Dieu de votre père, qui a mis un trésor dans vos sacs. Votre argent m’a bien été remis.

Puis il relâcha Siméon et le leur fit amener. 24Il les introduisit ensuite dans la maison de Joseph. Il leur apporta de l’eau pour qu’ils se lavent les pieds et fit porter du fourrage pour leurs ânes. 25Ils préparèrent leur présent en attendant l’arrivée de Joseph pour midi ; ils avaient, en effet, appris qu’ils mangeraient là. 26Joseph rentra chez lui. Ils lui offrirent le présent qu’ils avaient apporté et se prosternèrent à terre devant lui. 27Il prit de leurs nouvelles et leur demanda : Votre père âgé dont vous m’avez parlé, se porte-t-il bien ? Vit-il encore ?

28Ils répondirent en s’inclinant et en se prosternant jusqu’à terre : Ton serviteur, notre père, est encore en vie et il va bien.

29En apercevant son frère Benjamin, fils de sa mère, il demanda : Est-ce là votre frère cadet dont vous m’avez parlé ? Et il ajouta : Que Dieu te témoigne sa grâce, mon fils !

30Joseph sortit en hâte car la vue de son frère l’avait profondément ému, et il chercha un endroit pour laisser couler ses larmes ; il se retira dans sa chambre et pleura. 31Puis il se lava le visage et ressortit. Il contint son émotion et ordonna de servir le repas. 32On les servit séparément, lui à une table, ses frères à une autre, et les Egyptiens qui mangeaient avec lui à une troisième table. En effet, les Egyptiens ne peuvent pas prendre leurs repas avec les Hébreux : ils considèrent cela comme une chose abominable. 33On fit asseoir les frères en face de Joseph, par ordre d’âge, de l’aîné au plus jeune, de sorte qu’ils se regardaient l’un l’autre avec stupéfaction. 34Joseph leur fit servir des mets de sa propre table ; Benjamin reçut une part cinq fois plus copieuse que celle des autres. Ainsi ils burent tout leur saoûl avec lui.