Genesis 42 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 42:1-38

Abale a Yosefe Apita ku Igupto

1Yakobo atamva kuti ku Igupto kuli tirigu, anati kwa ana ake, “Nʼchifukwa chiyani mukungoyangʼanana wina ndi mnzake? 2Ine ndamva kuti ku Igupto kuli tirigu. Pitani kumeneko mukatigulireko kuti tisafe ndi njala.”

3Choncho abale ake khumi a Yosefe anapita kukagula tirigu ku Igupto. 4Koma Yakobo sanamulole Benjamini mngʼono wake wa Yosefe kuti apite nawo chifukwa anaopa kuti choyipa chingamuchitikire. 5Choncho ana a Israeli aja anapita pamodzi ndi gulu la anzawo kukagula tirigu pakuti ku Kanaani kunalinso njala.

6Pakuti Yosefe anali nduna yayikulu yolamulira dziko la Igupto, ndiye kuti analinso amene ankagulitsa tirigu kwa anthu onse. Choncho abale ake a Yosefe nawonso anabwera, ndipo anamugwadira pansi. 7Yosefe atangowaona abale ake anawazindikira, koma ananamizira kukhala ngati mlendo nawayankhula mwaukali kuwafunsa kuti, “Mwachokera kuti?”

Iwo anayankha, “Ku dziko la Kanaani, tikudzagula chakudya.”

8Ngakhale Yosefe anawazindikira abale ake, koma iwo sanamuzindikire. 9Pamenepo anakumbukira maloto aja amene analota za iwo ndipo anati, “Inu ndinu akazitape! Mwabwera kudzazonda dziko lathu kuti muone pamene palibe chitetezo.”

10Iwo anayankha, “Ayi mbuye wathu, antchito anufe tabwera kudzagula chakudya. 11Tonse ndife ana a munthu mmodzi. Ndife antchito anu okhulupirika osati akazitape.”

12Iye anawawuza kuti, “Ayi! Inu mwabwera kudzaona pamene palibe chitetezo mʼdziko muno.”

13Koma iwo anayankha, “Tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri. Abambo athu ndi mmodzi, ndipo kwathu ndi ku Kanaani. Panopo wotsiriza ali ndi abambo athu ndipo wina anamwalira.”

14Yosefe anawawuza kuti, “Ndi momwe ndaneneramo: Inu ndinu akazitape. 15Ndiye ndikuyesani motere: Ine ndikulumbira pali Farao ndithu, inuyo simudzachoka malo ano mpaka wotsirizayo atabwera kuno. 16Tumizani mmodzi wa inu akamutenge mʼbale wanuyo ndipo ena nonsenu musungidwa mʼndende, kuti titsimikize ngati zimene mukunenazi ndi zoona. Apo ayi, pali Farao ndithu, inu ndinu akazitape!” 17Ndipo onse anawayika mʼndende kwa masiku atatu.

18Pa tsiku lachitatu Yosefe anawawuza kuti, “Popeza ine ndimaopa Mulungu, ndipo inuyo ngati mukufuna kukhala ndi moyo muchite izi: 19Ngati muli anthu achilungamo, mmodzi wa inu atsale mʼndende, pamene ena nonse mupite kwanu kuti muwatengere chakudya anthu akwanu kuli njalako. 20Mukabwere naye kuno mngʼono wanu wotsirizayo kuti titsimikizire zimene munanena kuti musafe.” Ndipo anachita zomwezo.

21Iwo anati kwa wina ndi mnzake, “Ndithu ife tinalakwira mʼbale wathu uja popeza kuti ngakhale tinaona kuvutika kwake ndi kumva kulira kwake pamene ankatidandaulira kuti timuchitire chifundo, koma ife sitinamvere. Nʼchifukwa chake masautso awa atigwera.”

22Rubeni anayankha, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musamuchite kanthu mnyamata uja? Koma inu simunamvere! Tsopano tikulandira malipiro a magazi ake.” 23Koma sanadziwe kuti Yosefe ankawamva popeza kuti ankagwiritsa ntchito wotanthauzira poyankhula naye.

24Yosefe anapita pambali payekha kukalira. Kenaka anabweranso nadzayankhula nawo. Iye anatenga Simeoni namumanga iwo akuona.

25Yosefe analamula kuti awadzazire matumba awo ndi tirigu, awayikiremo ndalama zawo momwemo ndiponso awapatse chakudya cha panjira. Izi anawachitiradi. 26Abale a Yosefe aja anasenzetsa abulu awo tirigu amene anagula uja ndipo ananyamuka ulendo wawo.

27Atafika pamalo pena poti agone, mmodzi mwa iwo anatsekula thumba lake kuti atapemo chakudya cha bulu wake. Atangomasula anaona kuti ndalama zake zili pakamwa pa thumba. 28Iye anati kwa abale akewo, “Ndalama zanga andibwezera, izi zili mʼthumba mwangamu.”

Mitima yawo inachita ngati yachokamo ndipo anali ndi mantha ambiri, nati, “Ndi chiyani chimene Mulungu watichitira?”

29Atafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani anafotokoza zonse zimene zinawachitikira nati, 30“Nduna yayikulu ya mʼdzikomo inatiyankhula mwa ukali kwambiri ndipo inkatiyesa kuti ndife akazitape. 31Koma tinamuwuza kuti, ‘Ndife anthu woona mtima osati akazitape. 32Ife tonse tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri, abambo mmodzi. Mmodzi anamwalira, ndipo wamngʼono ali ndi abambo athu ku Kanaani.’ ”

33Ndipo nduna ija inati kwa ife, “Kuti ndidziwedi kuti ndinu anthu owona mtima muchite izi: Mmodzi mwa inu atsale ndi ine kuno, ndipo enanu mutenge chakudya ndi kubwerera kwanu kumene kuli njalako. 34Koma mundibweretsere wotsirizayo kuti ndidziwedi kuti sindinu akazitape koma anthu achilungamo. Kenaka ndidzakubwezerani mʼbale wanuyu ndipo mukhoza kuchita malonda mʼdzikoli.”

35Pamene amakhuthula matumba awo a tirigu aliyense anapeza kuti kathumba kake ka ndalama kali momwemo. Ataona zimenezi, iwo pamodzi ndi abambo awo anachita mantha kwambiri. 36Abambo awo Yakobo anawawuza kuti, “Mwandilanda ana anga ine. Yosefe anamwalira ndipo Simeoni palibenso, ndiye tsopano mukufuna mutengenso Benjamini. Zonsezi zandigwera ine!”

37Koma Rubeni anati kwa abambo ake, “Ngati sindidzabwera naye kwa inu, mudzaphe ana anga aamuna awiri. Muperekeni mʼmanja mwangamu ndipo ndidzamusamala ndi kubwera naye kwa inu.”

38Koma Yakobo anati, “Mwana wanga sapita nanu kumeneko; mkulu wake anamwalira ndipo watsala yekha. Ngati choyipa chitamuchitikira pa ulendo mukupitawu, ndiye kuti ndi mmene ndakalambiramu inu mudzandipha ndi chisoni chotere.”

New International Reader’s Version

Genesis 42:1-38

Joseph’s Brothers Go Down to Egypt

1Jacob found out that there was grain in Egypt. So he said to his sons, “Why do you just keep looking at one another?” 2He continued, “I’ve heard there’s grain in Egypt. Go down there. Buy some for us. Then we’ll live and not die.”

3So ten of Joseph’s brothers went down to Egypt to buy grain there. 4But Jacob didn’t send Joseph’s brother Benjamin with them. He was afraid Benjamin might be harmed. 5Israel’s sons were among the people who went to buy grain. There wasn’t enough food in the land of Canaan.

6Joseph was the governor of the land. He was the one who sold grain to all its people. When Joseph’s brothers arrived, they bowed down to him with their faces to the ground. 7As soon as Joseph saw his brothers, he recognized them. But he pretended to be a stranger. He spoke to them in a mean way. “Where do you come from?” he asked.

“From the land of Canaan,” they replied. “We’ve come to buy food.”

8Joseph recognized his brothers, but they didn’t recognize him. 9Then Joseph remembered his dreams about them. So he said to them, “You are spies! You have come to see the places where our land isn’t guarded very well.”

10“No, sir,” they answered. “We’ve come to buy food. 11All of us are the sons of one man. We’re honest men. We aren’t spies.”

12“No!” he said to them. “You have come to see the places where our land isn’t guarded very well.”

13But they replied, “We were 12 brothers. All of us were the sons of one man. He lives in the land of Canaan. Our youngest brother is now with our father. And one brother is gone.”

14Joseph said to them, “I still say you are spies! 15So I’m going to test you. And here’s the test. You can be sure that you won’t leave this place unless your youngest brother comes here. You can be just as sure of this as you are sure that Pharaoh lives. I give you my word that you won’t leave here unless your brother comes. 16Send one of you back to get your brother. The rest of you will be kept in prison. I’ll test your words. Then we’ll find out whether you are telling the truth. You can be sure that Pharaoh lives. And you can be just as sure that if you aren’t telling the truth, we’ll know that you are spies!” 17So Joseph kept all of them under guard for three days.

18On the third day, Joseph spoke to them again. He said, “Do what I say. Then you will live, because I have respect for God. 19If you are honest men, let one of your brothers stay here in prison. The rest of you may go and take grain back to your hungry families. 20But you must bring your youngest brother to me. That will prove that your words are true. Then you won’t die.” So they did what he said.

21They said to one another, “God is surely punishing us because of our brother. We saw how upset he was when he begged us to let him live. But we wouldn’t listen. That’s why all this trouble has come to us.”

22Reuben replied, “Didn’t I tell you not to sin against the boy? But you wouldn’t listen! Now we’re being paid back for killing him.” 23They didn’t realize that Joseph could understand what they were saying. He was using someone else to explain their words to him in the Egyptian language.

24Joseph turned away from his brothers and began to weep. Then he came back and spoke to them again. He had Simeon taken and tied up right there in front of them.

25Joseph gave orders to have their bags filled with grain. He had each man’s money put back into his sack. He also made sure they were given food for their journey. 26Then the brothers loaded their grain on their donkeys and left.

27When night came, they stopped. One of them opened his sack to get feed for his donkey. He saw his money in the top of his sack. 28“My money has been given back,” he said to his brothers. “Here it is in my sack.”

They had a sinking feeling in their hearts. They began to tremble. They turned to one another and said, “What has God done to us?”

29They came to their father Jacob in the land of Canaan. They told him everything that had happened to them. They said, 30“The man who is the governor of the land spoke to us in a mean way. He treated us as if we were spying on the land. 31But we said to him, ‘We’re honest men. We aren’t spies. 32We were 12 brothers. All of us were the sons of one father. But now one brother is gone. And our youngest brother is with our father in Canaan.’

33“Then the man who is the governor of the land spoke to us. He said, ‘Here’s how I will know whether you are honest men. Leave one of your brothers here with me. Take food for your hungry families and go. 34But bring your youngest brother to me. Then I’ll know that you are honest men and not spies. I’ll give your brother back to you. And you will be free to trade in the land.’ ”

35They began emptying their sacks. There in each man’s sack was his bag of money! When they and their father saw the money bags, they were scared to death. 36Their father Jacob said to them, “You have taken my children away from me. Joseph is gone. Simeon is gone. Now you want to take Benjamin. Everything is going against me!”

37Then Reuben spoke to his father. He said, “You can put both of my sons to death if I don’t bring Benjamin back to you. Trust me to take care of him. I’ll bring him back.”

38But Jacob said, “My son will not go down there with you. His brother is dead. He’s the only one left here with me. Suppose he’s harmed on the journey you are taking. Then I would die as a sad old man.”