Genesis 41 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 41:1-57

Maloto a Farao

1Patapita zaka ziwiri zathunthu, Farao analota atayimirira mʼmbali mwa mtsinje wa Nailo, 2ndipo anangoona ngʼombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zooneka bwino ndi zonenepa zikutuluka mu mtsinje muja ndi kuyamba kudya msipu wa mu mawango. 3Kenaka ngʼombe zina zazikazi zisanu ndi ziwiri zosaoneka bwino ndi zowonda zinatulukanso mu mtsinje wa Nailo ndipo zinayimirira pambali pa zina zija zimene zinali mʼmphepete mwa mtsinje uja. 4Ndipo ngʼombe zosaoneka bwino ndi zowonda zija zinadya ngʼombe zonenepa zija. Kenaka Farao anadzidzimuka.

5Posakhalitsa anagonanso ndipo analota kachiwiri: Analota ngala zisanu ndi ziwiri za tirigu zathanzi labwino zitabala pa phata limodzi. 6Kenaka ngala zina zisanu ndi ziwiri zinaphuka. Izi zinali zowonda ndi zowauka ndi mphepo ya kummawa. 7Ngala zowonda zija zinameza ngala zathanzi ndi zonenepa zija. Farao anadzidzimuka ndipo anaona kuti anali maloto chabe.

8Mmawa, Farao anavutika mu mtima kotero anayitanitsa amatsenga ndi anzeru onse a mu Igupto. Iwo atabwera, iye anawawuza maloto ake, koma panalibe ndi mmodzi yemwe amene anatha kutanthauzira malotowo kwa Farao.

9Ndipo mkulu wa operekera zakumwa anati kwa Farao, “Lero ndakumbukira kulephera kwanga. 10Paja nthawi ina Farao anapsera mtima antchito akefe, ndipo anatitsekera (ine ndi mkulu wa ophika buledi) mʼndende, mʼnyumba ya mkulu wa alonda. 11Tsiku lina tonse awiri tinalota maloto, ndipo loto lililonse linali ndi tanthauzo lake. 12Tsono momwemo munali mnyamata wina Wachihebri, wantchito wa mkulu wa alonda. Ife tinamufotokozera maloto athu, ndipo anatitanthauzira malotowo. Munthu aliyense anamupatsa tanthauzo la loto lake. 13Ndipo zinthu zinachitikadi monga mmene anatitanthauzira. Ine anandibwezera pa ntchito yanga ndipo winayo anapachikidwa.”

14Choncho Farao anamuyitanitsa Yosefe, ndipo mofulumira anabwera naye kuchokera mʼdzenje muja. Ndipo atameta, ndi kusintha zovala, anapita kwa Farao.

15Farao anati kwa Yosefe, “Ndinalota maloto ndipo palibe amene watha kunditanthauzira. Tsono ndawuzidwa kuti iwe ukamva loto umadziwanso kulimasulira.”

16Yosefe anamuyankha Farao kuti, “Sindingathe koma Mulungu apereka yankho limene Farao akufuna.”

17Ndipo Farao anati kwa Yosefe, “Ndinalota nditayimirira mʼmphepete mwa mtsinje wa Nailo, 18ndipo ngʼombe zisanu ndi ziwiri zonenepa ndi zooneka bwino zinatuluka mu mtsinje muja ndi kumadya msipu wa mu mawango. 19Kenaka, ngʼombe zina zisanu ndi ziwiri zinatuluka. Izi zinali zosaoneka bwino ndiponso zowonda ndipo sindinaonepo ngʼombe zosaoneka bwino chonchi mʼdziko lonse la Igupto. 20Ngʼombe zosaoneka bwino ndi zowonda zija zinadya zisanu ndi ziwiri zonenepa zimene zinatuluka poyamba zija. 21Koma ngakhale ngʼombezi zinadya zinazo, palibe amene akanatha kuzindikira kuti zinatero popeza zinali zosaonekabe bwino monga poyamba. Ndipo ndinadzidzimuka.

22“Nditagonanso kachiwiri, ndinalota ngala zisanu ndi ziwiri za tirigu zathanzi ndi zonenepa zitabala pa phata limodzi. 23Kenaka panaphukanso ngala zina zisanu ndi ziwiri zofota, zowonda ndi zowauka ndi mphepo ya kummawa. 24Ngala zowondazo zinameza ngala zisanu ndi ziwiri zabwino zija. Ndinawawuza amatsenga koma palibe ndi mmodzi yemwe anatha kundimasulira.”

25Ndipo Yosefe anati kwa Farao, “Maloto awiriwa ndi ofanana ndipo ali ndi tanthauzo limodzi. Mulungu waululira Farao chimene atachite. 26Ngʼombe zisanu ndi ziwiri zabwinozo ndi zaka zisanu ndi ziwiri. Ndipo ngala zisanu ndi ziwiri zabwinozo ndi zaka zisanu ndi ziwiri. Kutanthauza kwa maloto nʼkumodzi. 27Ngʼombe zisanu ndi ziwiri zowonda ndi zosaoneka bwino zimene zinatuluka pambuyozo ndiponso ngala zisanu ndi ziwiri zachabechabe, zowauka ndi mphepo ya kummawa zija ndi zaka zisanu ndi ziwiri za njala.

28“Tsono ndi monga ndafotokozeramu kuti Mulungu wakuwuziranitu zimene adzachite. 29Zaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zochuluka zikubwera mu dziko lonse la Igupto, 30koma zidzatsatana ndi zaka zina zisanu ndi ziwiri za njala. Chakudya chochuluka cha mu Igupto chija chidzayiwalika ndipo njalayo idzawononga dziko. 31Zakudya zochuluka za mʼdzikomo zija sizidzakumbukirikanso chifukwa njala imene iti idzabwereyo idzakhala yoopsa. 32Popeza kuti malotowa aperekedwa kwa inu Mfumu kawiri, ndiye kuti Mulungu watsimikiza kuti adzachitadi zimenezi posachedwapa.

33“Tsopano Farao apezeretu munthu wozindikira ndi wanzeru ndipo amuyike kukhala woyangʼanira dziko lonse la Igupto. 34Asankhenso akuluakulu a mʼdziko lino. Iwowa azitenga ndi kuyika padera limodzi la magawo asanu aliwonse a zokolola za mʼdziko muno mu zaka zonse zisanu ndi ziwiri za chakudya chochuluka. 35Iwo asonkhanitse zakudya zonse za mʼzaka zabwino zikubwerazi. Pansi pa ulamuliro wa Farao, akuluakuluwo asonkhanitse ndi kusunga bwino tirigu mʼmizinda yonse. 36Chakudya chimenechi chisungidwe kuti chidzagwiritsidwe ntchito mʼzaka zisanu ndi ziwiri za njala imene ikubwerayo mu Igupto, kuti anthu a mʼdzikoli asadzafe ndi njalayo.”

37Farao ndi nduna zake anagwirizana nawo malangizo a Yosefe. 38Choncho Farao anafunsa nduna zake nati, “Kodi tingathe kumupeza munthu wina ngati uyu, amene ali ndi mzimu wa Mulungu?”

39Farao anati kwa Yosefe, “Pakuti Mulungu wakudziwitsa iwe zonsezi, palibe wina wodziwa zinthu ndi wanzeru ngati iwe. 40Iwe ukhala nduna yayikulu mu dziko langa ndipo anthu onse adzamvera zimene walamula. Ine ndekha ndiye amene ndidzakuposa mphamvu chifukwa ndimakhala pa mpando waufumu.”

Yosefe Alamulira Dziko la Igupto

41Choncho Farao anati kwa Yosefe, “Ine ndikukuyika iwe kukhala nduna yoyangʼanira dziko lonse la Igupto.” 42Ndipo Farao anavula mphete ku chala chake nayiveka ku chala cha Yosefe. Anamuvekanso mkanjo wonyezimira ndi nkufu wagolide mʼkhosi mwake. 43Anamukweza Yosefe pa galeta ngati wachiwiri pa ulamuliro. Ndipo anthu anafuwula pamaso pake nati, “Mʼgwadireni!” Motero anakhala nduna yayikulu ya dziko lonse la Igupto.

44Kenaka Farao anati kwa Yosefe, “Ine ndine Farao; tsono iwe ukapanda kulamula, palibe amene akhoza kuchita chilichonse ngakhale kuyenda kumene mʼdziko lonse la Igupto.” 45Farao anamupatsa Yosefe dzina lakuti Zafenati-Panea ndipo anamupatsanso Asenati mwana wa mkazi wa Potifara, wansembe wa Oni, kuti akhale mkazi wake. Choncho Yosefe anayendera dziko lonse la Igupto.

46Yosefe anali ndi zaka 30 pamene amayamba ntchito kwa Farao, mfumu ya ku Igupto. Ndipo Yosefe anachoka pa maso pa Farao nayendera dziko lonse la Igupto. 47Mʼzaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zambiri zija, anthu mʼdzikomo anakolola zochuluka. 48Yosefe anasonkhanitsa zakudya zonse zokololedwa mʼzaka zisanu ndi ziwiri zija ndipo anazisunga mʼmizinda. Mu mzinda uliwonse anayikamo chakudya chimene chinalimidwa mʼminda yozungulira komweko. 49Yosefe anasunga tirigu wochuluka kwambiri ngati mchenga wa ku nyanja. Kunali tirigu wochuluka kwambiri motero kuti analeka nʼkulembera komwe.

50Zisanafike zaka zanjala, Yosefe anabereka ana aamuna awiri mwa Asenati mwana wa mkazi wa Potifara, wansembe wa Oni. 51Yosefe anamutcha mwana wake woyamba, Manase popeza anati, “Mulungu wandiyiwalitsa zovuta zanga zija ndiponso banja la abambo anga.” 52Mwana wachiwiri wa mwamuna anamutcha Efereimu popeza anati, “Mulungu wandipatsa ana mʼdziko la masautso anga.”

53Zaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zochuluka zija zinatha, 54ndipo zaka zisanu ndi ziwiri za njala zija zinayamba monga ananenera Yosefe. Njalayi inafika ku mayiko ena onse koma ku dziko lonse la Igupto kunali chakudya. 55Pamene njala ija inakwanira dziko lonse la Igupto anthu analilira Farao kuti awapatse chakudya. Koma Farao anawawuza kuti, “Pitani kwa Yosefe ndipo mukachite zimene akakuwuzeni.”

56Pamene njala inafalikira dziko lonse, Yosefe anatsekula nkhokwe za zakudya namagulitsa tirigu kwa anthu a ku Igupto aja, pakuti njala inafika poyipa kwambiri mu Igupto monse. 57Anthu ankabwera ku Igupto kuchokera ku mayiko ena onse kudzagula tirigu kwa Yosefe, chifukwa njala inafika poyipa kwambiri pa dziko lonse lapansi.

Persian Contemporary Bible

پيدايش 41:1-57

خوابهای فرعون

1دو سال بعد از اين واقعه، شبی فرعون خواب ديد كه كنار رود نيل ايستاده است. 2ناگاه هفت گاو چاق و فربه از رودخانه بيرون آمده، شروع به چريدن كردند. 3بعد هفت گاو ديگر از رودخانه بيرون آمدند و كنار آن هفت گاو ايستادند، ولی اينها بسيار لاغر و استخوانی بودند. 4سپس گاوهای لاغر، گاوهای چاق را بلعيدند. آنگاه فرعون از خواب پريد.

5او باز خوابش برد و خوابی ديگر ديد. اين بار ديد كه هفت خوشهٔ گندم روی يک ساقه قرار دارند كه همگی پُر از دانه‌های گندم رسيده هستند. 6سپس هفت خوشهٔ نازک ديگر كه باد شرقی آنها را خشكانيده بود، ظاهر شدند. 7خوشه‌های نازک و خشكيده، خوشه‌های پُر و رسيده را بلعيدند. آنگاه فرعون از خواب بيدار شد و فهميد كه همه را در خواب ديده است.

8صبح روز بعد، فرعون كه فكرش مغشوش بود، تمام جادوگران و دانشمندان مصر را احضار نمود و خوابهايش را برای ايشان تعريف كرد، ولی كسی قادر به تعبير خوابهای او نبود.

9آنگاه رئيس ساقيان پيش آمده، به فرعون گفت: «الان يادم آمد كه چه خطای بزرگی مرتكب شده‌ام. 10‏-11مدتی پيش، وقتی كه بر غلامان خود غضب نمودی و مرا با رئيس نانوايان به زندانِ رئيس محافظانِ دربار انداختی، هر دو ما در يک شب خواب ديديم. 12ما خوابهايمان را برای جوانی عبرانی كه غلامِ رئيس محافظان دربار و با ما همزندان بود، تعريف كرديم و او خوابهايمان را برای ما تعبير كرد؛ 13و هر آنچه كه گفته بود اتفاق افتاد. من به خدمت خود برگشتم و رئيس نانوايان به دار آويخته شد.»

14فرعون فوراً فرستاد تا يوسف را بياورند، پس با عجله وی را از زندان بيرون آوردند. او سر و صورتش را اصلاح نمود و لباسهايش را عوض كرد و به حضور فرعون رفت.

15فرعون به او گفت: «من ديشب خوابی ديدم و كسی نمی‌تواند آن را برای من تعبير كند. شنيده‌ام كه تو می‌توانی خوابها را تعبير كنی.»

16يوسف گفت: «من خودم قادر نيستم خوابها را تعبير كنم، اما خدا معنی خوابت را به تو خواهد گفت.»

17پس فرعون خوابش را برای يوسف اينطور تعريف كرد: «در خواب ديدم كنار رود نيل ايستاده‌ام. 18ناگهان هفت گاو چاق و فربه از رودخانه بيرون آمده، مشغول چريدن شدند. 19سپس هفت گاو ديگر را ديدم كه از رودخانه بيرون آمدند، ولی اين هفت گاو بسيار لاغر و استخوانی بودند. هرگز در تمام سرزمين مصر، گاوهايی به اين زشتی نديده بودم. 20اين گاوهای لاغر آن هفت گاو چاقی را كه اول بيرون آمده بودند، بلعيدند. 21پس از بلعيدن، هنوز هم گاوها لاغر و استخوانی بودند. در اين موقع از خواب بيدار شدم. 22كمی بعد باز به خواب فرو رفتم. اين بار در خواب هفت خوشهٔ گندم روی يک ساقه ديدم كه همگی پر از دانه‌های رسيده بودند. 23اندكی بعد، هفت خوشه كه باد شرقی آنها را خشكانيده بود، نمايان شدند. 24ناگهان خوشه‌های نازک خوشه‌های پُر و رسيده را خوردند. همهٔ اينها را برای جادوگران خود تعريف كردم، ولی هيچكدام از آنها نتوانستند تعبير آنها را برای من بگويند.»

25يوسف به فرعون گفت: «معنی هر دو خواب يكی است. خدا تو را از آنچه كه در سرزمين مصر انجام خواهد داد، آگاه ساخته است. 26هفت گاو چاق و فربه و هفت خوشهٔ پُر و رسيده كه اول ظاهر شدند، نشانهٔ هفت سالِ فراوانی است. 27هفت گاو لاغر و استخوانی و هفت خوشهٔ نازک و پژمرده، نشانهٔ هفت سال قحطی شديد است كه به دنبال هفت سال فراوانی خواهد آمد. 28بدين ترتيب، خدا آنچه را كه می‌خواهد بزودی در اين سرزمين انجام دهد، بر تو آشكار ساخته است. 29طی هفت سال آينده در سراسر سرزمين مصر محصول، بسيار فراوان خواهد بود. 30‏-31اما پس از آن، چنان قحطی سختی به مدت هفت سال پديد خواهد آمد كه سالهای فراوانی از خاطره‌ها محو خواهد شد و قحطی، سرزمين را از بين خواهد برد. 32خوابهای دوگانه تو نشانهٔ اين است كه آنچه برايت شرح دادم، بزودی به وقوع خواهد پيوست، زيرا از جانب خدا مقرر شده است. 33من پيشنهاد می‌كنم كه فرعون مردی دانا و حكيم بيابد و او را بر ادارهٔ امور كشاورزی اين سرزمين بگمارد. 34‏-35سپس مأمورانی مقرر كند تا در هفت سال فراوانی، يک پنجم محصولات را در شهرها، در انبارهای سلطنتی ذخيره كنند، 36تا در هفت سال قحطی بعد از آن، با كمبود خوراک مواجه نشويد. در غير اين صورت، سرزمين شما در اثر قحطی از بين خواهد رفت.»

يوسف شخص دوم مملكت می‌شود

37فرعون و همه افرادش پيشنهاد يوسف را پسنديدند. 38سپس فرعون گفت: «چه كسی بهتر از يوسف می‌تواند از عهده اين كار برآيد، مردی كه روح خدا در اوست.»

39سپس فرعون رو به يوسف نموده، گفت: «چون خدا تعبير خوابها را به تو آشكار كرده است، پس داناترين و حكيم‌ترين شخص تو هستی. 40هم اكنون تو را بر اين امر مهم می‌گمارم. تو شخص دوم سرزمين مصر خواهی شد و فرمانت در سراسر كشور اجرا خواهد گرديد.» 41‏-43سپس فرعون انگشتر سلطنتی خود را به انگشت يوسف كرد و لباس فاخری بر او پوشانيده، زنجير طلا به گردنش آويخت، و او را سوار دومين عرابهٔ سلطنتی كرد. او هر جا می‌رفت جلو او جار می‌زدند: «زانو بزنيد!»

بدين ترتيب يوسف بر تمامی امور مصر گماشته شد.

44فرعون به يوسف گفت: «من فرعون، پادشاه مصر، اختيارات سراسر كشور مصر را به تو واگذار می‌كنم.» 45فرعون به يوسف، نام مصری صفنات فعنيح را داد و اسنات دختر فوطی فارع، كاهن اون را به عقد وی درآورد. و يوسف در سراسر كشور مصر مشهور گرديد.

46يوسف سی ساله بود كه فرعون او را به خدمت گماشت. او دربار فرعون را ترک گفت تا به امور سراسر كشور رسيدگی كند.

47طی هفت سالِ فراوانی محصول، غله در همه جا بسيار فراوان بود. 48در اين سالها يوسف محصولات مزارع را در شهرهای اطراف ذخيره نمود. 49به قدری غله در سراسر كشور جمع شد كه ديگر نمی‌شد آنها را حساب كرد.

50قبل از پديد آمدن قحطی، يوسف از همسرش اسنات، دختر فوطی فارع، كاهن اون صاحب دو پسر شد. 51يوسف پسر بزرگ خود را منسی (يعنی «فراموشی») ناميد و گفت: «با تولد اين پسر خدا به من كمک كرد تا تمامی خاطرهٔ تلخ جوانی و دوری از خانهٔ پدر را فراموش كنم.» 52او دومين پسر خود را افرايم (يعنی «پرثمر») ناميد و گفت: «خدا مرا در سرزمينِ سختیهايم، پرثمر گردانيده است.»

53سرانجام هفت سالِ فراوانی به پايان رسيد 54و همانطور كه يوسف گفته بود، هفت سالِ قحطی شروع شد. در كشورهای همسايهٔ مصر قحطی بود، اما در انبارهای مصر غلهٔ فراوان يافت می‌شد. 55گرسنگی بر اثر كمبود غذا آغاز شد و مردمِ مصر برای طلب كمک نزد فرعون رفتند و فرعون نيز آنها را نزد يوسف فرستاده، گفت: «برويد و آنچه يوسف به شما می‌گويد انجام دهيد.»

56‏-57در اين موقع، قحطی سراسر جهان را فرا گرفته بود. يوسف انبارها را گشوده، غلهٔ مورد نياز را به مصريان و به مردمی كه از خارج می‌آمدند می‌فروخت.