Genesis 39 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 39:1-23

Yosefe ndi Mkazi wa Potifara

1Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.

2Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto. 3Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino. 4Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake. 5Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda. 6Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya.

Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola. 7Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”

8Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga. 9Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?” 10Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.

11Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo. 12Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.

13Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba, 14iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri. 15Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”

16Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba. 17Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane. 18Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”

19Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri. 20Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu.

Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo 21koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe. 22Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo. 23Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

Persian Contemporary Bible

پيدايش 39:1-23

يوسف و زن فوطيفار

1و اما يوسف به دست تاجران اسماعيلی به مصر برده شد. فوطيفار كه يكی از افسران فرعون و رئيس محافظان دربار بود، او را از ايشان خريد. 2خداوند يوسف را در خانهٔ اربابش بسيار بركت می‌داد، به طوری كه آنچه يوسف می‌كرد موفقيت آميز بود. 3فوطيفار متوجه اين موضوع شده و دريافته بود كه خداوند با يوسف می‌باشد. 4از اين رو يوسف مورد لطف اربابش قرار گرفت. طولی نكشيد كه فوطيفار وی را بر خانه و كليه امور تجاری خود ناظر ساخت. 5خداوند فوطيفار را به خاطر يوسف بركت داد چنانكه تمام امور خانهٔ او به خوبی پيش می‌رفت و محصولاتش فراوان و گله‌هايش زياد می‌شد. 6پس فوطيفار مسئوليت ادارهٔ تمام اموال خود را به دست يوسف سپرد و ديگر او برای هيچ چيز فكر نمی‌كرد جز اين كه چه غذايی بخورد.

يوسف جوانی خوش‌اندام و خوش‌قيافه بود. 7پس از چندی، نظر همسر فوطيفار به يوسف جلب شد و به او پيشنهاد كرد كه با وی همبستر شود. 8اما يوسف نپذيرفت و گفت: «اربابم آنقدر به من اعتماد دارد كه هر آنچه در اين خانه است به من سپرده 9و تمام اختيار اين خانه را به من داده است. او چيزی را از من مضايقه نكرده جز تو را كه همسر او هستی. پس چگونه مرتكب چنين عمل زشتی بشوم؟ اين عمل، گناهی است نسبت به خدا.» 10اما او دست بردار نبود و هر روز از يوسف می‌خواست كه با وی همبستر شود. ولی يوسف به سخنان فريبنده او گوش نمی‌داد و تا آنجا كه امكان داشت از وی دوری می‌كرد.

11روزی يوسف طبق معمول به كارهای منزل رسيدگی می‌كرد. آن روز شخص ديگری هم در خانه نبود. 12پس آن زن چنگ به لباس او انداخته، گفت: «با من بخواب.» ولی يوسف از چنگ او گريخت و از منزل خارج شد، اما لباسش در دست وی باقی ماند.

13آن زن چون وضع را چنين ديد، 14‏-15با صدای بلند فرياد زده، خدمتكاران را به كمک طلبيد و به آنها گفت: «شوهرم اين غلام عبرانی را به خانه آورد، حالا او ما را رسوا می‌سازد! او به اتاقم آمد تا به من تجاوز كند، ولی چون مقاومت كردم و فرياد زدم، فرار كرد و لباس خود را جا گذاشت.»

16پس آن زن لباس را نزد خود نگاه داشت و وقتی شوهرش به منزل آمد 17داستانی را كه ساخته بود، برايش چنين تعريف كرد: «آن غلامِ عبرانی كه به خانه آورده‌ای می‌خواست به من تجاوز كند، 18ولی من با داد و فرياد، خود را از دستش نجات دادم. او گريخت، ولی لباسش را جا گذاشت.»

19فوطيفار چون سخنان زنش را شنيد، بسيار خشمگين شد 20و يوسف را به زندانی كه ساير زندانيان پادشاه در آن در زنجير بودند انداخت. 21اما در آنجا هم خداوند با يوسف بود و او را بركت می‌داد و وی را مورد لطف رئيس زندان قرار داد. 22طولی نكشيد كه رئيس زندان، يوسف را مسئول ادارهٔ زندان نمود، به طوری كه همهٔ زندانيان زير نظر او بودند. 23رئيس زندان در مورد كارهايی كه به يوسف سپرده بود نگرانی نداشت، زيرا خداوند با يوسف بود و او را در انجام كارهايش موفق می‌ساخت.