Genesis 39 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 39:1-23

Yosefe ndi Mkazi wa Potifara

1Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.

2Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto. 3Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino. 4Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake. 5Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda. 6Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya.

Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola. 7Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”

8Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga. 9Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?” 10Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.

11Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo. 12Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.

13Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba, 14iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri. 15Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”

16Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba. 17Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane. 18Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”

19Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri. 20Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu.

Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo 21koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe. 22Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo. 23Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

New Serbian Translation

1. Мојсијева 39:1-23

Јосиф и Петефријева жена

1Јосифа су довели у Египат, где га је од Исмаиљаца, који су га тамо одвели, купио Египћанин Петефрије, фараонов дворанин и заповедник његове телесне страже.

2Али Господ је био с Јосифом, те му је све полазило за руком. Зато је живео у дому свога господара Египћанина. 3Његов господар је видео да је Господ с Јосифом и да му Господ даје успех у свему што ради. 4Тако је Јосиф задобио његову наклоност, па га је поставио за управитеља свога дома и поверио му сву своју имовину. 5Од како га је поставио за надгледника свога дома и све своје имовине, Господ је због Јосифа благословио Египћанинов дом. Господњи благослов је био над свим што је Петефрије имао у кући и на пољу. 6Тако је све што је имао препустио Јосифовој бризи, тако да није бринуо ни за шта, осим за храну коју је јео.

А Јосиф је био стасит и наочит младић. 7После неког времена, жена његовог господара баци око на Јосифа, па му рече: „Лези са мном!“

8Али он то одби и рече жени свога господара: „Види, од како сам ја овде, мој се господар не брине ни о чему у кући, него је све препустио мени. 9Он у овој кући нема више власти од мене; ништа ми није ускратио осим тебе, јер си његова жена. Па како бих могао да учиним тако велико зло и згрешим против Бога?“ 10Тако је наговарала Јосифа из дана у дан, али он није пристајао ни да легне с њом ни да буде близу ње.

11Једног дана Јосиф уђе у кућу да ради свој посао. У кући није било никога од слугу. 12Она тада зграби његов огртач и рече му: „Лези са мном!“ Но, Јосиф остави огртач у њеној руци, те побегне изјуривши напоље.

13Кад је видела да је оставио огртач у њеној руци и да је изјурио из куће, 14она позва слуге и рече им: „Гледајте! Јеврејина нам је довео да нас исмева. Дошао је ту да легне са мном, али сам ја почела да вичем из свег гласа. 15Кад је чуо да сам повисила глас и почела да вичем, оставио је свој огртач код мене и побегао напоље.“

16Његов огртач је држала уз себе док се његов господар није вратио кући. 17Онда је и њему испричала исту причу: „Онај роб Јеврејин кога си нам довео, дошао је к мени да ме исмева. 18Али кад сам повисила глас и почела да вичем, он је оставио свој огртач код мене и побегао напоље.“

19Кад је његов господар чуо причу своје жене, која му је рекла: „Ето, тако је са мном поступио твој роб“, разгневио се. 20Тада господар зграби Јосифа и баци га у тамницу, тамо где су били затворени царски затвореници.

Јосиф је остао у тамници. 21Ипак, Господ је био с њим и смиловао му се, учинивши да Јосиф стекне наклоност управитеља тамнице. 22Управитељ тамнице је поверио Јосифу управу над свим затвореницима који су били у тамници. 23Управитељ тамнице није надгледао ништа што је поверио Јосифу, јер је с овим био Господ који му је давао успех у свему што би предузео.