Genesis 38 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 38:1-30

Yuda ndi Tamara

1Pa nthawi imeneyi, Yuda anasiyana ndi abale ake napita kukakhala ndi munthu wina wa ku Adulamu wotchedwa Hira. 2Kumeneko, Yuda anaona mwana wamkazi wa munthu wina wa Chikanaani wotchedwa Suwa. Anamukwatira nagona naye malo amodzi. 3Iye anatenga pathupi, nabala mwana wamwamuna amene anamutcha Eri. 4Anatenganso pathupi nabala mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Onani. 5Anaberekanso mwana wina wamwamuna ndipo anamutcha Sela. Ameneyu anabadwa Yuda ali ku Kezibi.

6Yuda anamupezera mkazi mwana wake woyamba uja Eri, ndipo dzina la mkaziyo linali Tamara. 7Koma ntchito zoyipa za Eri, mwana wachisamba wa Yuda zinayipira Yehova. Choncho Mulungu anamulanga ndi imfa.

8Pamenepo Yuda anati kwa Onani, “Kwatira mkazi wamasiye wa mʼbale wako. Ulowe chokolo kuti mʼbale wako akhale ndi mwana.” 9Koma Onani anadziwa kuti mwanayo sadzakhala wake. Choncho nthawi zonse pamene amagona naye mkaziyo, ankatayira umuna pansi kuti asamuberekere mwana mʼbale wake. 10Zimene ankachitazi zinayipira Yehova. Choncho anamulanganso ndi imfa.

11Kenaka Yuda anati kwa mpongozi wake Tamara, “Bwererani ku nyumba ya abambo anu ndi kukhala kumeneko ngati wamasiye mpaka mwana wanga Sela atakula.” Ananena izi chifukwa ankaopa kuti Sela angafenso ngati abale ake aja. Choncho Tamara anapita kukakhala ku nyumba ya abambo ake.

12Patapita nthawi yayitali, Batishua, mkazi wa Yuda anamwalira. Yuda atatha kulira maliro a mkazi wake, anapita, iyeyu pamodzi ndi bwenzi lake Hira, Mwadulamu uja, ku Timna kumene ankameta nkhosa zawo.

13Tamara atamva kuti apongozi ake akupita ku Timna kukameta nkhosa, 14iye anavula zovala zake za umasiye, nadziphimba nkhope ndi nsalu kuti asadziwike, ndipo anakhala pansi pa chipata cha ku Enaimu popita ku Timna. Tamara anachita izi chifukwa anaona kuti ngakhale Selayo anali atakula tsopano, iye sanaperekedwe kuti amulowe chokolo.

15Yuda atamuona anangomuyesa mkazi wadama chabe, chifukwa anadziphimba nkhope. 16Tsono anapita kwa mkaziyo pamphepete pa msewu paja nati, “Tabwera ndigone nawe.” Apa Yuda sankadziwa kuti mkazi uja anali mpongozi wake.

Ndiye mkazi uja anamufunsa Yuda nati, “Mudzandipatsa chiyani kuti ndigone nanu?”

17Iye anati, “Ndidzakutumizira kamwana kambuzi ka mʼkhola mwanga.”

Mkaziyo anayankha kuti, “Chabwino, ndavomera, koma mungandipatse chikole mpaka mutanditumizira mbuziyo?”

18Iye anati, “Ndikupatse chikole chanji?”

Mkaziyo anayankha, “Mundipatse mphete yanuyo, chingwe chanucho pamodzi ndi ndodo imene ili mʼdzanja lanulo.” Choncho anazipereka kwa iye nagona naye ndipo anatenga pathupi. 19Kenaka Tamara anachoka, navula nsalu anadziphimba nayo ija, navalanso zovala zake za umasiye zija.

20Tsono Yuda anatuma bwenzi lake Mwadulamu uja ndi kamwana kambuzi kaja kuti akapereke kwa mkazi wadama uja, ndi kuti akatero amubwezere chikole chake chija. Koma atafika sanamupezepo. 21Anawafunsa anthu a komweko, “Kodi mkazi wadama uja amene ankakhala pambali pa msewu wa ku Enaimu, ali kuti?”

Iwo anayankha, “Sipanakhalepo mkazi wa dama aliyense pano.”

22Choncho anabwerera kwa Yuda nati, “Sindinamupeze mkazi uja. Kuwonjeza apo, anthu a kumeneko amati, ‘Sipanakhalepo mkazi wadama pano.’ ”

23Pamenepo Yuda anati, “Mulekeni atenge zinthuzo zikhale zake, kuopa kuti anthu angatiseke. Ine sindinalakwe, ndinamutumizira kamwana kambuzika, koma simunamupeze.”

24Patapita miyezi itatu, Yuda anawuzidwa kuti, “Mpongozi wanu Tamara anachita zadama, ndipo zotsatira zake nʼzakuti ali ndi pathupi.”

Yuda anati, “Kamutulutseni ndipo mukamutenthe kuti afe!”

25Akumutulutsa, iye anatuma mawu kwa apongozi ake. Anati, “Ndili ndi pathupi pa munthu amene ndi mwini wake wa zinthu izi. Taziyangʼanitsitsani, kodi mwini wa khoza, chingwe ndi ndodo yoyenderayi ndi yani?”

26Yuda anazizindikira zinthuzo ndipo anati, “Uyu ndi wolungama kuposa ine, chifukwa sindinamupereke kwa mwana wanga Sela.” Ndipo Yuda sanagone nayenso.

27Pamene Tamara nthawi inamukwanira yoti abeleke, mʼmimbamo munali mapasa. 28Pamene ankabereka, mmodzi wa iwo anatulutsa dzanja lake. Choncho mzamba anatenga kawulusi kofiira nakamangirira pa mkono pa mwanayo nati, “Uyu ndiye anayamba kubadwa.” 29Koma pamene anabweza mkonowo, mʼbale wake anabadwa ndipo mzamba anati, “Wachita kudziphotcholera wekha njira chonchi!” Ndipo anamutcha Perezi. 30Pambuyo pake mʼbale wake amene anali ndi ulusi wofiira pa mkono wake uja anabadwa ndipo anapatsidwa dzina lakuti Zera.

Thai New Contemporary Bible

ปฐมกาล 38:1-30

ยูดาห์กับทามาร์

1ครั้งนั้นยูดาห์แยกจากพี่น้องของเขาไปอาศัยอยู่กับชายชาวอดุลลัมผู้หนึ่งชื่อฮีราห์ 2ที่นั่น ยูดาห์พบบุตรสาวของชูอาชาวคานาอันและแต่งงานและหลับนอนกับนาง 3นางตั้งครรภ์ คลอดบุตรชาย และตั้งชื่อเขาว่าเอร์ 4นางตั้งครรภ์อีกครั้งหนึ่งคลอดบุตรชาย และตั้งชื่อเขาว่าโอนัน 5จากนั้นนางมีบุตรชายอีก และตั้งชื่อเขาว่าเชลาห์ นางคลอดบุตรคนนี้ที่เคซิบ

6ยูดาห์หาภรรยาให้เอร์บุตรหัวปี นางชื่อว่าทามาร์ 7แต่เอร์บุตรหัวปีของยูดาห์เป็นคนชั่วในสายพระเนตรขององค์พระผู้เป็นเจ้าดังนั้นองค์พระผู้เป็นเจ้าจึงทรงให้เขาถึงแก่ความตาย

8ยูดาห์จึงบอกโอนันว่า “เจ้าจงหลับนอนกับทามาร์พี่สะใภ้ ทำหน้าที่แทนพี่ชายที่ล่วงลับไปของเจ้า เพื่อลูกที่เกิดมาจะนับเป็นวงศ์วานของพี่ชายของเจ้าต่อไป” 9แต่โอนันรู้ว่าลูกที่เกิดมาจะไม่นับเป็นทายาทของเขา ฉะนั้นเมื่อเขาร่วมหลับนอนกับพี่สะใภ้คราวใด เขาจะปล่อยน้ำอสุจิตกดินไปเพื่อไม่ให้พี่ชายมีทายาทสืบตระกูล 10องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงเห็นว่าสิ่งที่เขาทำเป็นเรื่องชั่วร้าย พระองค์จึงทรงให้เขาตายเช่นกัน

11ยูดาห์จึงกล่าวกับทามาร์ลูกสะใภ้ของตนว่า “จงไปอาศัยในเรือนของบิดาของเจ้าอย่างหญิงม่ายคนหนึ่งจนกว่าเชลาห์ลูกชายของเราจะโตขึ้น” เพราะเขาคิดว่า “เชลาห์อาจจะตายเช่นเดียวกับพี่ชายทั้งสองคน” ทามาร์จึงกลับไปอาศัยอยู่ในเรือนของบิดา

12เวลาผ่านไปนานจนกระทั่งภรรยาของยูดาห์บุตรีของชูอาตายไป เมื่อยูดาห์คลายความโศกเศร้าแล้ว เขากับฮีราห์เพื่อนชาวอดุลลัมของเขาไปที่ทิมนาห์ ไปหาผู้คนซึ่งกำลังตัดขนแกะของเขา

13มีคนไปบอกทามาร์ว่า “พ่อสามีของเธอกำลังไปที่ทิมนาห์เพื่อตัดขนแกะของเขา” 14ทามาร์จึงเปลี่ยนเครื่องแต่งกายแม่ม่ายออก เอาผ้าคลุมหน้า ปลอมตัวมานั่งอยู่ริมทางเข้าหมู่บ้านเอนาอิมซึ่งเป็นทางไปทิมนาห์ เพราะทามาร์เห็นว่ายูดาห์ไม่ยอมให้ตนแต่งงานกับเชลาห์ แม้ว่าเขาจะโตแล้ว

15เมื่อยูดาห์เห็นนางก็คิดว่าเป็นผู้หญิงหากิน เนื่องจากนางเอาผ้าคลุมหน้าไว้ 16เขาจึงแวะเข้าไปหานางแล้วพูดว่า “มาสิ ให้ข้าร่วมหลับนอนกับเจ้า” โดยไม่รู้ว่านางคือลูกสะใภ้

นางถามว่า “ท่านจะให้อะไรเป็นค่าตอบแทน?”

17เขาตอบว่า “ข้าจะส่งลูกแพะมาให้ตัวหนึ่ง”

นางก็ถามว่า “ท่านจะให้อะไรเป็นมัดจำจนกว่าท่านจะส่งลูกแพะมาให้?”

18เขาถามว่า “เธออยากได้อะไรเป็นของมัดจำ?”

นางตอบว่า “ขอตราประจำตัวกับเชือกร้อยตราและไม้เท้าในมือของท่าน” เขาจึงมอบให้นาง นางก็ยินยอมหลับนอนกับเขา และนางก็ตั้งครรภ์กับเขา 19หลังจากนั้นนางจึงเอาผ้าคลุมหน้าออกและกลับมานุ่งห่มเครื่องแต่งกายแม่ม่ายตามเดิม

20เมื่อยูดาห์ขอให้ฮีราห์ชาวอดุลลัมเพื่อนของเขาเอาลูกแพะไปให้นาง เพื่อแลกของมัดจำคืนจากหญิงคนนั้น ฮีราห์กลับหานางไม่พบ 21เขาจึงเที่ยวถามบรรดาผู้ชายแถวนั้นว่า “หญิงโสเภณีประจำเทวสถานซึ่งอยู่ริมทางเอนาอิมนั้นอยู่ที่ไหน?”

พวกเขาตอบว่า “ไม่เคยมีหญิงโสเภณีประจำเทวสถานคนใดอยู่ที่นี่”

22ฮีราห์จึงกลับมาหายูดาห์แล้วบอกเขาว่า “ข้าหานางไม่พบ นอกจากนั้นบรรดาผู้ชายแถวนั้นก็บอกว่า ‘ไม่เคยมีหญิงโสเภณีประจำเทวสถานคนใดอยู่ที่นี่’ ”

23ยูดาห์จึงกล่าวว่า “ให้นางเก็บของพวกนั้นไว้ก็แล้วกัน มิฉะนั้นเราจะกลายเป็นตัวตลกให้คนหัวเราะ อย่างไรเสียเราก็ได้ส่งลูกแพะไปให้แล้วแต่หานางไม่พบ”

24ราวสามเดือนต่อมา มีคนมาบอกยูดาห์ว่า “ทามาร์ลูกสะใภ้ของท่านทำผิดด้วยการคบชู้สู่ชายจนตั้งครรภ์แล้ว”

ยูดาห์จึงสั่งว่า “นำตัวนางออกมาและเอาไปเผาให้ตาย!”

25แต่ขณะที่คนทั้งหลายกำลังพาตัวนางออกมา นางส่งคนมาบอกพ่อสามีว่า “ฉันตั้งครรภ์กับชายผู้เป็นเจ้าของสิ่งเหล่านี้ จงดูเถิดว่าท่านจำได้ไหมว่าตราประจำตัว เชือกร้อยตรา และไม้เท้านี้เป็นของใคร”

26ยูดาห์จำได้ว่าของเหล่านี้เป็นของตนจึงพูดว่า “นางชอบธรรมยิ่งกว่าเราเสียอีก เพราะเราไม่ยอมให้นางเป็นภรรยาของเชลาห์ลูกชายของเรา” และยูดาห์ก็ไม่ได้หลับนอนกับทามาร์อีกเลย

27เมื่อถึงกำหนดคลอด นางมีลูกแฝดชายสองคนอยู่ในครรภ์ 28ในขณะที่นางกำลังคลอด ทารกคนหนึ่งยื่นมือออกมา นางผดุงครรภ์จึงเอาด้ายแดงผูกข้อมือและพูดว่า “คนนี้ออกมาก่อน” 29แต่ทารกนั้นหดมือกลับ และอีกคนหนึ่งคลอดออกมา นางจึงพูดว่า “อ้าว! แหวกออกมาได้อย่างไร” เด็กนั้นจึงได้ชื่อว่าเปเรศ38:29 แปลว่าแหวกออกมา 30แล้วทารกคนที่มีด้ายแดงผูกข้อมือก็คลอดออกมาและได้ชื่อว่าเศราห์38:30 แปลว่าแดงเข้มหรือความเจิดจ้าก็ได้