Genesis 36 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 36:1-43

Zidzukulu za Esau

1Nazi zidzukulu za Esau amene ankatchedwanso Edomu:

2Esau anakwatira akazi atatu a ku Kanaani. Iwowa ndiwo Ada mwana wa Eloni Mhiti; Oholibama mwana wa Ana amene anali mwana wa Zibeoni Mhivi 3ndi Basemati mwana wa Ismaeli, amenenso anali mlongo wa Nabayoti.

4Ada anaberekera Esau, Elifazi; Basemati anabereka Reueli; 5ndipo Oholibama anabereka Yeusi, Yolamu ndi Kora. Amenewa anali ana a Esau amene anabadwira ku Kanaani.

6Esau anatenga akazi ake, ana ake aamuna ndi aakazi ndi ena onse a pa banja pake. Anatenganso ziweto zake ndi ziweto zake zonse pamodzi ndi katundu wake yense amene anamupata ku Kanaani, ndipo anachoka ku dziko la Kanaani kupatukana ndi mʼbale wake Yakobo. 7Iwo anatero chifukwa dziko limene ankakhalamo silikanakwanira awiriwo. Iwowa anali ndi ziweto zochuluka motero kuti sakanatha kukhala pamodzi. 8Choncho Esau (amene ndi Edomu) anakakhazikika ku dziko la mapiri ku Seiri.

9Nazi zidzukulu za Esau, kholo la Aedomu amene ankakhala ku Seiri.

10Awa ndi mayina a ana aamuna a Esau:

Elifazi, mwana wa Ada, mkazi wa Esau, ndi Reueli, mwana wamwamuna wa Basemati, mkazi wa Esau.

11Awa ndi mayina a ana a Elifazi:

Temani, Omari, Zefo, Gatamu ndi Kenazi.

12Timna anali mzikazi wa Elifazi, mwana wa Esau. Iyeyo anaberekera Elifazi mwana dzina lake Amaleki. Amenewa ndiwo zidzukulu za Ada, mkazi wa Esau.

13Awa ndi ana a Reueli:

Nahati, Zera, Sama ndi Miza. Amenewa ndi ana a Basemati, mkazi wa Esau.

14Ana aamuna a Oholibama, mkazi wa Esau, mwana wa Ana ndi mdzukulu wa Zebeoni ndi awa:

Yeusi, Yolamu ndi Kora.

15Nawa mafumu a zidzukulu za Esau:

Mwa ana a Elifazi, mwana woyamba wa Esau panali mafumu awa:

Temani, Omari, Zefo, ndi Kenazi, 16Kora, Gatamu, ndi Amaleki. Awa anali mafumu mwa ana a Elifazi ku Edomu ndipo onsewa anali zidzukulu za Ada.

17Mwa ana a Reueli, mwana wa Esau munali mafumu awa:

Nahati, Zera, Sama ndi Miza. Awa anali mafumu mwa ana a Reueli ku Edomu. Iwowa anali zidzukulu za Basemati mkazi wa Esau.

18Mwa ana a Oholibama, mkazi wa Esau munali mafumu awa:

Yeusi, Yolamu, ndi Kora. Amenewa anali mafumu mwa ana a mkazi wa Esau, Oholibama, mwana wa Ana.

19Amenewa ndiwo zidzukulu za Esau (amene ndi Edomu) ndiponso mafumu awo.

20Awa ndi ana a Seiri Mhori, amene ankakhala mʼdzikomo:

Lotani, Sobala, Zibeoni, Ana, 21Disoni, Ezeri ndi Disani. Amenewa ndiwo ana a Seiri a ku Edomu ndipo analinso mafumu a Ahori.

22Ana aamuna a Lotani anali awa:

Hori ndi Homamu. Timna anali mlongo wake wa Lotani.

23Ana aamuna a Sobala anali awa:

Alivani, Manahati, Ebala, Sefo ndi Onamu.

24Ana aamuna a Zibeoni anali awa:

Ayiwa ndi Ana. Uyu ndi Ana amene anapeza akasupe a madzi amoto mʼchipululu pamene ankadyetsa abulu abambo wake Zibeoni.

25Ana a Ana anali:

Disoni ndi Oholibama mwana wake wamkazi.

26Ana aamuna a Disoni anali awa:

Hemudani, Esibani, Itirani ndi Kerani.

27Ana aamuna a Ezeri anali awa:

Bilihani, Zaavani ndi Akani.

28Ana aamuna a Disani anali awa:

Uzi ndi Arani.

29Mafumu a Ahori anali awa:

Lotani, Sobala, Zibeoni, Ana, 30Disoni, Ezeri ndi Disani. Amenewa ndiwo mafumu a Ahori, monga mwa mafuko awo, mʼdziko la Seiri.

Mafumu a ku Edomu

31Awa ndi mafumu amene ankalamulira dziko la Edomu, mfumu iliyonse ya Israeli isanayambe kulamulira kumeneko:

32Bela mwana wa Beori anakhala mfumu ya ku Edomu. Mzinda wake ankawutcha Dinihaba.

33Bela atamwalira, Yobabu mwana wa Zera wochokera ku Bozira analowa ufumu mʼmalo mwake.

34Atafa Yobabu, Husamu wochokera ku dziko la Atemani, analowa mʼmalo mwake ngati mfumu.

35Husamu atamwalira, Hadadi mwana wa Bedadi, amene anagonjetsa Amidiyani mʼdziko la Mowabu, analowa ufumu mʼmalo mwake. Mzinda wake unkatchedwa Aviti.

36Hadadi atamwalira, Samila wochokera ku Masireka, analowa ufumu mʼmalo mwake.

37Samila atamwalira, Sauli wochokera ku Rehoboti wa ku Mtsinje, analowa ufumu mʼmalo mwake.

38Sauli atamwalira, Baala-Hanani, mwana wa Akibori analowa ufumu mʼmalo mwake.

39Pamene Baala-Hanani mwana wa Akibori anamwalira, Hadari analowa ufumu mʼmalo mwake. Mzinda wake unkatchedwa Pau, ndipo dzina la mkazi wake linali Mehatabeli, mwana wamkazi wa Matiredi, mwana wamkazi wa Me-Zahabu.

40Mayina a mafumu ochokera mwa zidzukulu za Esau malingana ndi mafuko awo ndi malo a fuko lililonse anali awa:

Timna, Aliva, Yeteti, 41Oholibama, Ela, Pinoni, 42Kenazi, Temani, Mibezari, 43Magidieli ndi Iramu. Awa anali mafumu a ku Edomu molingana ndi malo awo okhala mʼdzikomo.

Umenewu ndi mndandanda wa mʼbado wa Esau, kholo la Aedomu.

Hoffnung für Alle

1. Mose 36:1-43

Esaus Nachkommen

1Es folgt der Stammbaum von Esau, der auch Edom genannt wurde:

2-3Er hatte drei Frauen aus Kanaan geheiratet: Ada, eine Tochter des Hetiters Elon; Oholibama, eine Tochter Anas und Enkelin des Horiters Zibon, und Basemat, eine Tochter Ismaels und Schwester Nebajots. 4Von Ada hatte er einen Sohn mit Namen Elifas; von Basemat stammte Reguël, 5und mit Oholibama zeugte er Jëusch, Jalam und Korach. Alle wurden im Land Kanaan geboren.

6Später verließ Esau das Land. Seine Frauen, Kinder und alle, die zu ihm gehörten, nahm er mit; dazu seine Viehherden und den Besitz, den er in Kanaan erworben hatte. Er zog in das Land Seïr, fort von seinem Bruder Jakob. 7Sie besaßen beide so große Viehherden, dass es im Land Kanaan nicht genug Weidefläche für sie gab. 8Deshalb ließ sich Esau, der Stammvater der Edomiter, im Bergland Seïr nieder.

9Dies ist die Liste der Nachkommen von Esau; es sind die Edomiter, die im Land Seïr leben. 10Die Söhne Esaus: Von seinen beiden Frauen Ada und Basemat hatte Esau je einen Sohn; Ada brachte Elifas zur Welt und Basemat Reguël. 11Elifas’ Söhne waren Teman, Omar, Zefo, Gatam, Kenas 12und Amalek. Amalek war der Sohn von Elifas’ Nebenfrau Timna. 13Reguël hatte vier Söhne: Nahat, Serach, Schamma und Misa. 14Oholibama, die Tochter Anas und Enkelin Zibons, bekam drei Söhne: Jëusch, Jalam und Korach.

15-16Esaus Söhne wurden zu Oberhäuptern verschiedener Stämme. Von Esaus ältestem Sohn Elifas stammen die Fürsten Teman, Omar, Zefo, Kenas, Korach, Gatam und Amalek. Sie gehen auf Esaus Frau Ada zurück. 17Von Esaus Sohn Reguël stammen die Fürsten Nahat, Serach, Schamma und Misa. Sie gehen auf Esaus Frau Basemat zurück. 18Von Esaus Frau Oholibama stammen die Fürsten Jëusch, Jalam und Korach. 19Diese Fürsten sind Nachkommen Esaus und bilden das Volk der Edomiter.

Seïrs Nachkommen

20-21Die Einwohner im Land Edom gehen auf den Horiter Seïr zurück. Seine Söhne waren Lotan, Schobal, Zibon, Ana, Dischon, Ezer und Dischan. Sie waren die Oberhäupter von den verschiedenen Stämmen der Horiter.

22Lotans Söhne hießen Hori und Hemam, seine Schwester hieß Timna. 23Schobals Söhne waren Alwan, Manahat, Ebal, Schefi und Onam. 24Zibons Söhne waren Ajja und Ana. Ana fand eine heiße Quelle in der Wüste, als er dort die Esel seines Vaters Zibon weidete. 25Ana hatte einen Sohn namens Dischon und eine Tochter mit Namen Oholibama. 26Dischons Söhne hießen Hemdan, Eschban, Jitran und Keran. 27Ezers Söhne waren Bilhan, Saawan und Akan. 28Dischans Söhne hießen Uz und Aran.

29-30Aus diesen entstanden die Stämme der Horiter, denen die Stammesfürsten Lotan, Schobal, Zibon, Ana, Dischon, Ezer und Dischan als Oberhäupter vorstanden.

Könige und Oberhäupter der Edomiter

31Noch bevor die Israeliten einen König hatten, regierten im Land Edom nacheinander folgende Könige:

32König Bela, der Sohn von Beor, in der Stadt Dinhaba;

33König Jobab, der Sohn von Serach, aus Bozra;

34König Huscham aus dem Gebiet der Temaniter;

35König Hadad, der Sohn von Bedad, in der Stadt Awit; sein Heer schlug die Midianiter im Gebiet von Moab;

36König Samla aus Masreka;

37König Schaul aus Rehobot am Fluss;

38König Baal-Hanan, der Sohn von Achbor;

39König Hadad in der Stadt Pagu; seine Frau hieß Mehetabel, sie war eine Tochter von Matred und Enkelin von Me-Sahab.

40-43Folgende Oberhäupter der Edomiter stammen von Esau ab: Timna, Alwa, Jetet, Oholibama, Ela, Pinon, Kenas, Teman, Mibzar, Magdiël und Iram. Nach ihnen werden die verschiedenen Stämme und ihre Gebiete benannt.