Genesis 36 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 36:1-43

Zidzukulu za Esau

1Nazi zidzukulu za Esau amene ankatchedwanso Edomu:

2Esau anakwatira akazi atatu a ku Kanaani. Iwowa ndiwo Ada mwana wa Eloni Mhiti; Oholibama mwana wa Ana amene anali mwana wa Zibeoni Mhivi 3ndi Basemati mwana wa Ismaeli, amenenso anali mlongo wa Nabayoti.

4Ada anaberekera Esau, Elifazi; Basemati anabereka Reueli; 5ndipo Oholibama anabereka Yeusi, Yolamu ndi Kora. Amenewa anali ana a Esau amene anabadwira ku Kanaani.

6Esau anatenga akazi ake, ana ake aamuna ndi aakazi ndi ena onse a pa banja pake. Anatenganso ziweto zake ndi ziweto zake zonse pamodzi ndi katundu wake yense amene anamupata ku Kanaani, ndipo anachoka ku dziko la Kanaani kupatukana ndi mʼbale wake Yakobo. 7Iwo anatero chifukwa dziko limene ankakhalamo silikanakwanira awiriwo. Iwowa anali ndi ziweto zochuluka motero kuti sakanatha kukhala pamodzi. 8Choncho Esau (amene ndi Edomu) anakakhazikika ku dziko la mapiri ku Seiri.

9Nazi zidzukulu za Esau, kholo la Aedomu amene ankakhala ku Seiri.

10Awa ndi mayina a ana aamuna a Esau:

Elifazi, mwana wa Ada, mkazi wa Esau, ndi Reueli, mwana wamwamuna wa Basemati, mkazi wa Esau.

11Awa ndi mayina a ana a Elifazi:

Temani, Omari, Zefo, Gatamu ndi Kenazi.

12Timna anali mzikazi wa Elifazi, mwana wa Esau. Iyeyo anaberekera Elifazi mwana dzina lake Amaleki. Amenewa ndiwo zidzukulu za Ada, mkazi wa Esau.

13Awa ndi ana a Reueli:

Nahati, Zera, Sama ndi Miza. Amenewa ndi ana a Basemati, mkazi wa Esau.

14Ana aamuna a Oholibama, mkazi wa Esau, mwana wa Ana ndi mdzukulu wa Zebeoni ndi awa:

Yeusi, Yolamu ndi Kora.

15Nawa mafumu a zidzukulu za Esau:

Mwa ana a Elifazi, mwana woyamba wa Esau panali mafumu awa:

Temani, Omari, Zefo, ndi Kenazi, 16Kora, Gatamu, ndi Amaleki. Awa anali mafumu mwa ana a Elifazi ku Edomu ndipo onsewa anali zidzukulu za Ada.

17Mwa ana a Reueli, mwana wa Esau munali mafumu awa:

Nahati, Zera, Sama ndi Miza. Awa anali mafumu mwa ana a Reueli ku Edomu. Iwowa anali zidzukulu za Basemati mkazi wa Esau.

18Mwa ana a Oholibama, mkazi wa Esau munali mafumu awa:

Yeusi, Yolamu, ndi Kora. Amenewa anali mafumu mwa ana a mkazi wa Esau, Oholibama, mwana wa Ana.

19Amenewa ndiwo zidzukulu za Esau (amene ndi Edomu) ndiponso mafumu awo.

20Awa ndi ana a Seiri Mhori, amene ankakhala mʼdzikomo:

Lotani, Sobala, Zibeoni, Ana, 21Disoni, Ezeri ndi Disani. Amenewa ndiwo ana a Seiri a ku Edomu ndipo analinso mafumu a Ahori.

22Ana aamuna a Lotani anali awa:

Hori ndi Homamu. Timna anali mlongo wake wa Lotani.

23Ana aamuna a Sobala anali awa:

Alivani, Manahati, Ebala, Sefo ndi Onamu.

24Ana aamuna a Zibeoni anali awa:

Ayiwa ndi Ana. Uyu ndi Ana amene anapeza akasupe a madzi amoto mʼchipululu pamene ankadyetsa abulu abambo wake Zibeoni.

25Ana a Ana anali:

Disoni ndi Oholibama mwana wake wamkazi.

26Ana aamuna a Disoni anali awa:

Hemudani, Esibani, Itirani ndi Kerani.

27Ana aamuna a Ezeri anali awa:

Bilihani, Zaavani ndi Akani.

28Ana aamuna a Disani anali awa:

Uzi ndi Arani.

29Mafumu a Ahori anali awa:

Lotani, Sobala, Zibeoni, Ana, 30Disoni, Ezeri ndi Disani. Amenewa ndiwo mafumu a Ahori, monga mwa mafuko awo, mʼdziko la Seiri.

Mafumu a ku Edomu

31Awa ndi mafumu amene ankalamulira dziko la Edomu, mfumu iliyonse ya Israeli isanayambe kulamulira kumeneko:

32Bela mwana wa Beori anakhala mfumu ya ku Edomu. Mzinda wake ankawutcha Dinihaba.

33Bela atamwalira, Yobabu mwana wa Zera wochokera ku Bozira analowa ufumu mʼmalo mwake.

34Atafa Yobabu, Husamu wochokera ku dziko la Atemani, analowa mʼmalo mwake ngati mfumu.

35Husamu atamwalira, Hadadi mwana wa Bedadi, amene anagonjetsa Amidiyani mʼdziko la Mowabu, analowa ufumu mʼmalo mwake. Mzinda wake unkatchedwa Aviti.

36Hadadi atamwalira, Samila wochokera ku Masireka, analowa ufumu mʼmalo mwake.

37Samila atamwalira, Sauli wochokera ku Rehoboti wa ku Mtsinje, analowa ufumu mʼmalo mwake.

38Sauli atamwalira, Baala-Hanani, mwana wa Akibori analowa ufumu mʼmalo mwake.

39Pamene Baala-Hanani mwana wa Akibori anamwalira, Hadari analowa ufumu mʼmalo mwake. Mzinda wake unkatchedwa Pau, ndipo dzina la mkazi wake linali Mehatabeli, mwana wamkazi wa Matiredi, mwana wamkazi wa Me-Zahabu.

40Mayina a mafumu ochokera mwa zidzukulu za Esau malingana ndi mafuko awo ndi malo a fuko lililonse anali awa:

Timna, Aliva, Yeteti, 41Oholibama, Ela, Pinoni, 42Kenazi, Temani, Mibezari, 43Magidieli ndi Iramu. Awa anali mafumu a ku Edomu molingana ndi malo awo okhala mʼdzikomo.

Umenewu ndi mndandanda wa mʼbado wa Esau, kholo la Aedomu.

Священное Писание

Начало 36:1-43

Потомки Есава

(1 Лет. 1:35-42)

1Вот родословие Есава (он же Эдом).

2Есав взял себе жён из Ханаана: Аду, дочь хетта Елона, Оливему, дочь Анаха и внучку хивея Цивеона, 3а также Басемафу, дочь Исмаила, сестру Навайота.

4Ада родила Есаву Елифаза, Басемафа родила Рагуила, 5Оливема родила Иеуша, Иалама и Кораха. Это сыновья Есава, рождённые ему в Ханаане.

6Есав взял своих жён, сыновей, дочерей и всех домашних, взял стада, и скот и всё имущество, которое он приобрёл в Ханаане, и перебрался в другую землю, на некоторое расстояние от своего брата Якуба, 7потому что у них было слишком много добра, чтобы им оставаться вместе. У них было столько скота, что земля, где они жили пришельцами, не могла прокормить их обоих. 8Так Есав (он же Эдом) поселился в нагорьях Сеира.

9Вот родословие Есава, отца эдомитян, жившего в нагорьях Сеира.

10Вот имена сыновей Есава:

Елифаз, сын Есава от его жены Ады, Рагуил, сын Есава от его жены Басемафы.

11Сыновья Елифаза:

Теман, Омар, Цефо, Гатам и Кеназ.

12У сына Есава Елифаза была наложница по имени Тимна, которая родила ему Амалика. Это внуки жены Есава Ады.

13Сыновья Рагуила:

Нахат, Зерах, Шамма и Миза. Это внуки жены Есава Басемафы.

14Сыновья Есава от его жены Оливемы, дочери Анаха и внучки Цивеона, которых она родила Есаву:

Иеуш, Иалам и Корах.

15Вот вожди среди потомков Есава.

Сыновья Елифаза, первенца Есава:

вожди Теман, Омар, Цефо, Кеназ, 16Корах, Гатам и Амалик. Это вожди, произошедшие от Елифаза в Эдоме; они были внуками Ады.

17Сыновья Рагуила, сына Есава:

вожди Нахат, Зерах, Шамма и Миза. Это вожди, произошедшие от Рагуила в Эдоме; они были внуками жены Есава Басемафы.

18Сыновья Есава от его жены Оливемы:

вожди Иеуш, Иалам и Корах. Это вожди, произошедшие от жены Есава Оливемы, дочери Анаха.

19Вот сыновья Есава (он же Эдом) и вот их вожди.

20Вот сыновья Сеира хорреянина, жившие в той области:

Лотан, Шовал, Цивеон, Анах, 21Дишон, Ецер и Дишан. Эти сыновья Сеира в Эдоме были вождями хорреев.

22Сыновья Лотана:

Хори и Гомам. Тимна была сестрой Лотана.

23Сыновья Шовала:

Алван, Манахат, Евал, Шефо и Онам.

24Сыновья Цивеона:

Аях и Анах. Это тот Анах, который открыл в пустыне горячие ключи, когда пас ослов своего отца Цивеона.

25Дети Анаха:

Дишон и Оливема, дочь Анаха.

26Сыновья Дишона:

Хемдан, Эшбан, Ифран и Херан.

27Сыновья Ецера:

Билган, Зааван и Акан.

28Сыновья Дишана:

Уц и Аран.

29Вот вожди хорреев:

Лотан, Шовал, Цивеон, Анах, 30Дишон, Ецер и Дишан. Они были вождями хорреев по родам их в земле Сеир.

Правители Эдома

(1 Лет. 1:43-54)

31Вот цари, которые правили в Эдоме ещё до того, как цари появились в Исраиле:

32Бела, сын Беора, был царём в Эдоме. Его город назывался Динхава.

33После смерти Белы царём вместо него стал Иовав, сын Зераха, из Боцры.

34После смерти Иовава царём вместо него стал Хушам из земли теманитян.

35После смерти Хушама царём вместо него стал Хадад, сын Бедада, который разбил мадианитян в земле Моава. Его город назывался Авит.

36После смерти Хадада царём вместо него стал Самла из Масреки.

37После смерти Самлы царём вместо него стал Шаул из Реховота, что у реки36:37 Река – по-видимому, Евфрат..

38После смерти Шаула царём вместо него стал Баал-Ханан, сын Ахбора.

39После смерти Баал-Ханана, сына Ахбора, царём вместо него стал Хадад. Его город назывался Пау, а имя его жены было Мехетавиль; она была дочерью Матреды, внучкой Мезахава.

40Вот имена вождей – потомков Есава, по их кланам и землям:

Тимна, Алва, Иетет, 41Оливема, Ела, Пинон, 42Кеназ, Теман, Мивцар, 43Магдиил и Ирам.

Это вожди Эдома, по их поселениям в земле, которой они владеют.

Это был Есав – отец эдомитян.