Genesis 33 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 33:1-20

Yakobo Akumana ndi Esau

1Yakobo atakweza maso ake anaona Esau akubwera ndi anthu ake 400. Choncho ana ake anawagawira Leya, Rakele ndi antchito awiri aja. 2Anayika antchito ndi ana awo patsogolo, kenaka nʼkubwera Leya ndi ana ake, ndipo pambuyo pawo Rakele ndi Yosefe. 3Iye mwini anakhala patsogolo nawerama mpaka kukhudza pansi kasanu ndi kawiri pamene amayandikira mʼbale wake.

4Koma Esau anathamanga kukakumana ndi Yakobo ndipo anamukupatira namupsompsona. Onse awiri ankangolira. 5Kenaka Esau ataona amayi ndi ana awo anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi anthu amene uli nawowa ndi a ndani?”

Yakobo anayankha kuti, “Awa ndi ana amene Mulungu, mwa kukoma mtima kwake, wapereka kwa mtumiki wanune.”

6Tsono antchito aja anayandikira naweramitsa mitu pansi. 7Kenaka, Leya ndi ana ake anabwera. Nawonso anaweramitsa mitu pansi. Potsiriza pa onse anabwera Yosefe ndi Rakele naweramitsanso mitu yawo pansi.

8Esau anafunsa kuti, “Kodi gulu la ziweto ndakumana nalo lija ndi layani?”

Yakobo anayankha nati, “Mbuye wanga, gulu lija ndi lanu kuti mundikomere mtima.”

9Koma Esau anati, “Mʼbale wanga, ine ndili nazo kale zambiri. Zinthu zakozi sunga.”

10Yakobo anati, “Chonde musatero. Ngati mwandikomera mtima, landirani mphatso yangayi kuchokera kwa ine. Pakuti ndi mmene mwandirandira bwinomu, ine ndikamaona nkhope yanu ndikuchita ngati ndikuona nkhope ya Mulungu. 11Chonde, landirani mphatso imene ndakutengeraniyi, popeza Mulungu wandikomera mtima kwambiri moti ndili ndi zonse zimene ndizifuna.” Ndipo popeza kuti Yakobo anamuwumiriza, Esau analandira.

12Ndipo Esau anati, “Tiyeni tizipita; nditsagana nanu.”

13Koma Yakobo anati kwa iye, “Mbuye wanga, inu mudziwa kuti anawa ndi a nthete ndiponso ndiyenera kusamalira nkhosa ndi ngʼombe zimene zikuyamwitsa ana awo. Ngati ndizimenya kuti zifulumire, tsiku limodzi lokha nyamazo zidzafa. 14Choncho, mbuye wanga lolani kuti mutsogole. Ine ndiziyenda pangʼonopangʼono pambuyo pa ziwetozi ndi anawa mpaka ndikafika ku Seiri.”

15Esau anati, “Ndiye bwanji ndikusiyireko ena mwa anthu anga.”

Koma Yakobo anati, “Koma muchitiranji zimenezi? Chachikulu nʼkuti mwandilandira bwino, mbuye wanga.”

16Choncho tsiku limenelo Esau anayamba ulendo wobwerera ku Seiri. 17Komabe Yakobo anapita ku Sukoti. Kumeneko anamanga nyumba yake ndi makola a ziweto zake. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Sukoti.

18Mmene ankabwerera kuchokera ku Padanaramu, Yakobo anafika ku Salemu, mzinda wa Sekemu ku Kanaani. Anamanga msasa pamalopo moyangʼanana ndi mzindawo. 19Malo amenewo anagula kwa zidzukulu za Hamori, abambo a Sekemu ndi ndalama 100 zasiliva. 20Pamalopo anamanganso guwa lansembe, nalitcha Eli Elohe Israeli.

Korean Living Bible

창세기 33:1-20

야곱과 에서의 만남

1야곱이 멀리 바라보니 에서가 400명의 사람들을 거느리고 오고 있었다. 그래서 그는 자식들을 나누어 레아와 라헬과 두 여종에게 맡기고

2여종과 그들의 자식들은 앞에 세우고 레아와 그녀의 자식들은 그 다음에, 그리고 라헬과 요셉은 뒤에 두고

3자기가 앞서 나아가 땅에 몸을 일곱 번 굽히면서 형에게 다가갔다.

4그러자 에서가 달려와서 그를 맞으며 목을 끌어안고 입을 맞췄다. 그러고서 그들은 서로 울었다.

5에서가 여자들과 아이들을 보고 “너와 함께 있는 이 사람들은 다 누구냐?” 하고 묻자 야곱은 “하나님이 나에게 은혜로 주신 자식들입니다” 하고 대답하였다.

6그때 여종들이 그 자식들과 함께 앞으로 나와 절하고

7다음으로 레아와 그 자식들이, 마지막으로 요셉과 라헬이 나와서 절하였다.

8그러자 에서가 다시 물었다. “내가 올 때 만난 그 짐승 떼는 무엇이냐?” “그것은 형님에게 드리는 선물입니다.”

9“내 동생아, 나에게 있는 것도 충분하니 네 소유는 네가 가져라.”

10“그러지 마십시오. 형님이 나에게 사랑을 베푸신다면 이 선물을 받아 주십시오. 이렇게 형님이 나를 따뜻하게 반겨 주시니 내가 형님의 얼굴을 보는 것이 꼭 하나님의 얼굴을 보는 것 같습니다.

11제발 내가 형님께 가져온 이 선물을 받으십시오. 하나님이 나에게 은혜를 베풀어 주셔서 내가 필요로 하는 것은 무엇이든지 다 가지고 있습니다.” 야곱이 계속 권하자 에서가 그 선물을 받고

12이렇게 말하였다. “자, 가자. 내가 길을 안내하겠다.”

13“형님도 아시겠지만 애들은 연약한 데다가 새끼에게 젖을 먹이는 양과 소들도 있으니 하루만 더 심하게 몬다면 모든 짐승이 다 죽고 말 것입니다.

14그러니 형님은 먼저 가십시오. 나는 앞서 가는 짐승들과 자식들에게 보조를 맞춰 천천히 가서 세일에서 형님을 뵙겠습니다.”

15“그렇다면 내 종 몇 사람을 너와 함께 머물게 하여 너를 돕도록 하겠다.” “형님, 그러실 필요는 없습니다. 33:15 또는 ‘나로 내 주께 은혜를 얻게 하소서’형님의 호의만으로도 족합니다.”

16그래서 그 날 에서는 세일로 돌아갔다.

17그러나 야곱은 숙곳으로 가서 거기에 집을 짓고 가축 우리를 만들었는데 숙곳이란 말은 그가 오두막이란 뜻으로 붙인 이름이었다.

18야곱은 메소포타미아에서 가나안의 세겜성에 무사히 도착하여 그 성 부근에 천막을 치고

19은화 100개로 자기가 천막을 친 그 밭을 세겜의 창설자인 하몰의 아들들에게서 사고

20거기에 단을 세워 그 이름을 33:20 ‘하나님 곧 이스라엘의 하나님’ 이라는 뜻.‘엘 – 엘로헤 – 이스라엘’ 이라고 하였다.