Genesis 32 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 32:1-32

Yakobo Akonzekera Kukumana ndi Esau

1Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye. 2Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.

3Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu. 4Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano. 5Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’ ”

6Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”

7Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri. 8Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”

9Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’ 10Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri. 11Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe. 12Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”

13Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake: 14Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri, 15ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi. 16Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”

17Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’ 18Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’ ”

19Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye. 20Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’ ” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.” 21Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.

Yakobo Alimbana ndi Mulungu

22Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki. 23Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense. 24Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha. 25Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo. 26Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.”

Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”

27Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?”

Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”

28Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”

29Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.”

Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.

30Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”

31Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija. 32Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.

New Russian Translation

Бытие 32:1-32

Иаков готовится к встрече с братом Исавом

1Иаков продолжил свой путь, и ангелы Божьи встретили его. 2Когда Иаков увидел их, он сказал:

– Это Божий стан! – и назвал то место Маханаим32:2 Это название означает: «два стана»..

3Иаков послал впереди себя вестников к своему брату Исаву в землю Сеир, страну Эдом. 4Он дал им такой наказ:

– Скажите моему господину Исаву так: «Твой слуга Иаков говорит: Я жил у Лавана и был там до сего дня. 5У меня есть быки, ослы, овцы и козы, слуги и служанки. Я посылаю эту весть моему господину, чтобы найти милость в твоих глазах».

6Посланцы вернулись и сказали Иакову:

– Мы были у твоего брата Исава, и теперь он сам идет тебе навстречу и с ним четыреста человек.

7В великом страхе и смятении Иаков разделил людей, которые были с ним, а также стада крупного и мелкого скота и верблюдов. 8Он думал: «Если Исав нападет на одну половину32:8 Букв.: «один стан»., то другая уцелеет и спасется».

9Иаков взмолился:

– О Боже моего отца Авраама, Боже моего отца Исаака, о Господь, сказавший мне: «Вернись в твою землю, к твоим родственникам, и Я дам тебе процветание», 10я недостоин той милости и верности, которые Ты явил Твоему слуге. У меня ничего не было, кроме посоха, когда я перешел Иордан, а теперь я возвращаюсь двумя станами. 11Молю Тебя, спаси меня от руки моего брата Исава, потому что я боюсь, что он придет и нападет на меня и на матерей с детьми. 12Ведь Ты сказал: «Я непременно дам тебе процветание и сделаю потомство твое многочисленным, как морской песок, который не сосчитать».

13Он провел там ночь и из того, что у него было, выбрал подарок для своего брата Исава: 14двести коз и двадцать козлов, двести овец и двадцать баранов, 15тридцать верблюдиц с верблюжатами, сорок коров и десять быков, двадцать ослиц и десять ослов. 16Он поручил их слугам, каждое стадо особо, и сказал им:

– Идите впереди меня и держите между стадами некоторое расстояние.

17Он научил того, кто шел первым:

– Когда мой брат Исав встретит тебя и спросит: «Чей ты? Куда идешь? Чей скот ты гонишь?» – 18тогда ты скажи: «Скот твоего слуги Иакова. Это подарок от него моему господину Исаву, а сам он идет за нами».

19Он научил и второго, и третьего, и всех других, шедших за стадами:

– И вы так же скажете Исаву, когда он вас встретит. 20И еще скажите: «Твой слуга Иаков идет позади нас». Потому что он думал: «Я умиротворю его этими дарами, которые посылаю впереди себя, а потом, когда мы встретимся, он, быть может, примет меня». 21Так дары Иакова были отправлены вперед, а сам он провел ночь в лагере.

Иаков получает имя Израиль

22Той ночью Иаков встал и взял двух своих жен, двух служанок и одиннадцать сыновей и вброд перешел через реку Яббок. 23Он перевел их через поток и переправил все свое добро. 24И вот Иаков остался один, и Некто боролся с ним до самой зари. 25Увидев, что не может пересилить, Он коснулся сустава бедра Иакова, так что бедро было вывихнуто, когда он боролся с Ним. 26И Он сказал:

– Отпусти Меня, потому что восходит заря.

Но Иаков ответил:

– Не отпущу, пока не благословишь меня.

27Он спросил:

– Как твое имя?

– Иаков, – ответил он.

28Тогда Он сказал:

– Отныне твое имя будет не Иаков, а Израиль32:28 То есть «он борется с Богом»., потому что ты боролся с Богом и людьми и победил.

29Иаков сказал:

– Прошу Тебя, скажи мне Твое имя.

Но Он ответил:

– Зачем ты спрашиваешь Мое имя?

И Он благословил его. 30Иаков назвал то место Пениэл32:30 Это название означает «лицо Бога»., сказав: «Это потому, что я видел Бога лицом к лицу и остался жив».

31Солнце встало над ним, когда он проходил Пениэл32:31 Евр.: «Пенуэл» – вариант названия Пениэл., хромая из-за своего бедра. 32Вот почему до сего дня израильтяне не едят сухожилия на суставе бедра: ведь Он коснулся сустава бедра Иакова рядом с сухожилием.