Genesis 30 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 30:1-43

1Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”

2Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”

3Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”

4Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha, 5ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna. 6Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.

7Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri. 8Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.

9Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye. 10Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna. 11Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.

12Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri. 13Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.

14Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”

15Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.”

Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”

16Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.

17Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu. 18Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.

19Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi. 20Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.

21Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.

22Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana. 23Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.” 24Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”

Nkhosa za Yakobo Zichuluka

25Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu. 26Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”

27Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.” 28Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”

29Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira. 30Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”

31Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?”

Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira: 32Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga. 33Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”

34Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.” 35Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta. 36Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.

37Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera. 38Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana. 39Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho. 40Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani. 41Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija. 42Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo. 43Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Начало 30:1-43

1Рахиля видела, что она не рожает Якубу детей, и позавидовала своей сестре Лии. Она сказала Якубу:

– Дай мне детей, или я умру!

2Якуб разгневался на неё и сказал:

– Разве я Всевышний, Который не даёт тебе детей?

3Она сказала:

– Вот Билха, моя служанка. Ляг с ней, чтобы она родила мне на колени30:3 По-видимому, здесь говорится об обряде усыновления, после которого ребёнок должен был быть признан сыном Рахили., и у меня будут дети через неё30:3 По древнему ближневосточному обычаю бесплодная жена могла дать свою служанку мужу, чтобы усыновить родившихся от этого детей..

4Так она дала ему в жёны свою служанку Билху; Якуб лёг с ней, 5она забеременела и родила ему сына. 6Тогда Рахиля сказала: «Всевышний оправдал меня; Он внял моей мольбе и дал мне сына». Поэтому она назвала его Дон («он оправдал»). 7Билха, служанка Рахили, снова забеременела и родила Якубу второго сына. 8Тогда Рахиля сказала: «Великой борьбой боролась я с моей сестрой и победила». И она назвала его Неффалим («моя борьба»).

9Увидев, что она перестала рожать детей, Лия взяла свою служанку Зелфу и дала её Якубу в жёны. 10Зелфа, служанка Лии, родила Якубу сына. 11Тогда Лия сказала: «Какая удача!» И она назвала его Гад («удача»). 12Зелфа, служанка Лии, родила Якубу второго сына. 13Тогда Лия сказала: «Как я счастлива! Женщины будут звать меня счастливицей!» И она назвала его Ошер («счастье»).

14Во время жатвы пшеницы, Рувим вышел в поле, нашёл мандрагоры30:14 Мандрагора – растение из семейства паслёновых, плоды которого также называли яблоками любви. Считалось, что мандрагоровые яблоки вызывают чувственное влечение и способствуют деторождению. и принёс их матери. Рахиля сказала Лии:

– Пожалуйста, дай мне несколько мандрагор твоего сына.

15Но та сказала ей:

– Ты уже забрала у меня мужа, а теперь хочешь забрать и мандрагоры сына моего?

– Хорошо, – сказала Рахиля, – пусть он ляжет с тобой сегодня ночью в обмен на мандрагоры твоего сына.

16Когда вечером Якуб пришёл с полей, Лия вышла встретить его и сказала:

– Ты должен лечь со мной. Я заплатила за тебя мандрагорами сына.

И он лёг с ней в ту ночь. 17Всевышний услышал Лию, она забеременела и родила Якубу пятого сына. 18Тогда Лия сказала: «Всевышний вознаградил меня за то, что я дала мужу мою служанку». И она назвала его Иссокор («вознаграждение»). 19Лия снова забеременела и родила Якубу шестого сына. 20Тогда она сказала: «Всевышний подарил мне драгоценный подарок. Теперь муж станет чтить меня, потому что я родила ему шестерых сыновей». И она назвала его Завулон («честь»). 21Через какое-то время она родила дочь и назвала её Дина.

22Тогда Всевышний вспомнил Рахилю. Он услышал её и открыл ей утробу: 23она забеременела и родила сына, и сказала: «Всевышний снял мой позор». 24Она назвала его Юсуф («пусть прибавит»), потому что она сказала: «Да добавит мне Вечный ещё одного сына».

Обогащение Якуба

25После того как Рахиля родила Юсуфа, Якуб сказал Лобону:

– Отпусти меня, чтобы я мог вернуться в родные края. 26Дай мне моих жён и детей, за которых я служил тебе, и я тронусь в путь. Ты знаешь, как много я работал на тебя.

27Но Лобон сказал ему:

– Если я нашёл милость в твоих глазах, прошу тебя, останься: я узнал через гадание30:27 Гадание – ненавистно для Всевышнего и запрещено законами Таврота (см. Лев. 19:26; Втор. 18:10-12)., что Вечный благословляет меня благодаря тебе, – 28и добавил: – Назови свою цену, я заплачу её.

29Якуб ответил ему:

– Ты знаешь, как я работал на тебя и каковы твои стада благодаря моей заботе. 30Они были немногочисленны до моего прихода, но теперь их число многократно увеличилось, и Вечный благословлял тебя из-за меня. Когда же, наконец, я смогу скопить что-нибудь и для собственного дома?

31Лобон спросил:

– Что тебе дать?

– Мне ничего не надо, – ответил Якуб. – Сделай для меня лишь одно, и я буду и дальше пасти и охранять твой скот: 32давай я обойду все твои стада – выбери из них всех крапчатых и пятнистых овец, всех тёмных ягнят и всех пятнистых и крапчатых козлов. Они и будут моей платой. 33Честность моя будет мне порукой в будущем, когда бы ты ни решил проверить плату, отданную мне. Если найдётся у меня не крапчатый и не пятнистый козёл или не тёмный ягнёнок, то они будут считаться крадеными.

34– Договорились, – сказал Лобон. – Пусть будет так, как ты сказал.

35И в тот же день он отделил всех козлов с крапинами или пятнами, всех пятнистых и крапчатых коз – тех, на которых было белое, – и всех тёмных ягнят, и отдал их под надзор сыновей. 36Он назначил расстояние между собой и Якубом в три дня пути, а Якуб продолжал пасти остальной мелкий скот Лобона.

37Якуб нарезал свежих веток тополя, миндаля и чинары и сделал на них белые полоски, сняв кору и обнажив белое дерево внутри. 38Он положил ветки с нарезкой во все поилки, чтобы они были прямо перед скотом, когда скот приходил пить. Во время брачной поры, когда животные приходили пить, 39они спаривались перед ветками, и потомство рождалось пёстрым, крапчатым или пятнистым. 40Якуб ставил этот молодняк отдельно, а остальных поворачивал к пёстрым и тёмным животным, которые принадлежали Лобону. Так у него появились собственные стада, и он держал их отдельно от скота Лобона. 41Когда пить приходили крепкие животные, Якуб клал перед ними в корыта ветки, чтобы они спаривались перед ветками, 42а если животные были слабые, он не клал веток. Так слабый скот доставался Лобону, а сильный – Якубу. 43Якуб начал богатеть, у него теперь были большие стада, а также служанки, слуги, верблюды и ослы.