Genesis 3 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 3:1-24

Kuchimwa kwa Munthu

1Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’ ”

2Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu, 3koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’ ”

4“Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo. 5“Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”

6Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso. 7Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.

8Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo. 9Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”

10Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”

11Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”

12Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”

13Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?”

Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”

14Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi,

“Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse

ndi nyama zakuthengo zonse.

Udzayenda chafufumimba

ndipo udzadya fumbi

masiku onse a moyo wako.

15Ndipo ndidzayika chidani

pakati pa iwe ndi mkaziyo,

pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake;

Iye adzaphwanya mutu wako

ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”

16Kwa mkaziyo Iye anati,

“Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati;

ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana.

Udzakhumba mwamuna wako,

ndipo adzakulamulira.”

17Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’

“Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe,

movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo

masiku onse a moyo wako.

18Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula

ndipo udzadya zomera zakuthengo.

19Kuti upeze chakudya udzayenera

kukhetsa thukuta,

mpaka utabwerera ku nthaka

pakuti unachokera kumeneko;

pakuti ndiwe fumbi

ku fumbi komweko udzabwerera.”

20Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.

21Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka. 22Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.” 23Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera. 24Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.

Persian Contemporary Bible

پيدايش 3:1-24

سقوط انسان

1مار از همهٔ حيواناتی كه خداوند به وجود آورد، زيركتر بود. روزی مار نزد زن آمده، به او گفت: «آيا حقيقت دارد كه خدا شما را از خوردن ميوهٔ تمام درختان باغ منع كرده است؟»

2‏-3زن در جواب گفت: «ما اجازه داريم از ميوهٔ همهٔ درختان بخوريم، به‌جز ميوهٔ درختی كه در وسط باغ است. خدا امر فرموده است كه از ميوهٔ آن درخت نخوريم و حتی آن را لمس نكنيم و گرنه می‌ميريم.»

4مار گفت: «مطمئن باش نخواهيد مُرد! 5بلكه خدا خوب می‌داند زمانی كه از ميوهٔ آن درخت بخوريد، چشمان شما باز می‌شود و مانند خدا می‌شويد و می‌توانيد خوب را از بد تشخيص دهيد.»

6آن درخت در نظر زن، زيبا آمد و با خود انديشيد: «ميوهٔ اين درختِ دلپذير، می‌تواند، خوش طعم باشد و به من دانايی ببخشد.» پس از ميوهٔ درخت چيد و خورد و به شوهرش هم داد و او نيز خورد. 7آنگاه چشمانِ هر دو باز شد و از برهنگی خود آگاه شدند؛ پس با برگهای درختِ انجير پوششی برای خود درست كردند.

8عصر همان روز، آدم و زنش، صدای خداوند را كه در باغ راه می‌رفت شنيدند و خود را لابلای درختان پنهان كردند. 9خداوند آدم را ندا داد: «ای آدم، چرا خود را پنهان می‌كنی؟»3‏:9 يا «ای آدم، کجا هستی؟».‏

10آدم جواب داد: «صدای تو را در باغ شنيدم و ترسيدم، زيرا برهنه بودم؛ پس خود را پنهان كردم.»

11خداوند فرمود: «چه كسی به تو گفت كه برهنه‌ای؟ آيا از ميوهٔ آن درختی خوردی كه به تو گفته بودم از آن نخوری؟»

12آدم جواب داد: «اين زن كه يار من ساختی، از آن ميوه به من داد و من هم خوردم.»

13آنگاه خداوند از زن پرسيد: «اين چه كاری بود كه كردی؟»

زن گفت: «مار مرا فريب داد.»

14پس خداوند به مار فرمود: «به سبب انجام اين كار، از تمام حيوانات وحشی و اهلی زمين ملعونتر خواهی بود. تا زنده‌ای روی شكمت خواهی خزيد و خاک خواهی خورد. 15بين تو و زن، و نيز بين نسل تو و نسل زن، خصومت می‌گذارم. نسلِ زنْ سر تو را خواهد كوبيد و تو پاشنهٔ وی را خواهی زد.»

16آنگاه خداوند به زن فرمود: «درد زايمان تو را زياد می‌كنم و تو با درد فرزندان خواهی زاييد. مشتاق شوهرت خواهی بود و او بر تو تسلط خواهد داشت.»

17سپس خداوند به آدم فرمود: «چون گفتهٔ زنت را پذيرفتی و از ميوهٔ آن درختی خوردی كه به تو گفته بودم از آن نخوری، زمين زير لعنت قرار خواهد گرفت و تو تمام ايام عمرت با رنج و زحمت از آن كسب معاش خواهی كرد. 18از زمين خار و خاشاک برايت خواهد روييد و گياهان صحرا را خواهی خورد. 19تا آخر عمر به عرق پيشانی‌ات نان خواهی خورد و سرانجام به همان خاكی باز خواهی گشت كه از آن گرفته شدی؛ زيرا تو از خاک سرشته شدی و به خاک هم برخواهی گشت.»

20آدم، زن خود را حَوّا (يعنی «زندگی») ناميد، چون او می‌بايست مادر همهٔ زندگان شود.

21خداوند لباسهايی از پوست حيوان تهيه كرد و آدم و همسرش را پوشانيد. 22سپس خداوند فرمود: «حال كه آدم مانند ما شده است و خوب و بد را می‌شناسد، نبايد گذاشت از ميوهٔ ”درخت حيات“ نيز بخورد و تا ابد زنده بماند.» 23پس خداوند او را از باغ عدن بيرون راند تا برود و در زمينی كه از خاکِ آن سرشته شده بود، كار كند. 24بدين ترتيب او آدم را بيرون كرد و در سمت شرقی باغ عدن فرشتگانی قرار داد تا با شمشير آتشينی كه به هر طرف می‌چرخيد، راه «درخت حيات» را محافظت كنند.