Genesis 3 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 3:1-24

Kuchimwa kwa Munthu

1Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’ ”

2Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu, 3koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’ ”

4“Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo. 5“Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”

6Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso. 7Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.

8Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo. 9Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”

10Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”

11Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”

12Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”

13Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?”

Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”

14Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi,

“Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse

ndi nyama zakuthengo zonse.

Udzayenda chafufumimba

ndipo udzadya fumbi

masiku onse a moyo wako.

15Ndipo ndidzayika chidani

pakati pa iwe ndi mkaziyo,

pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake;

Iye adzaphwanya mutu wako

ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”

16Kwa mkaziyo Iye anati,

“Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati;

ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana.

Udzakhumba mwamuna wako,

ndipo adzakulamulira.”

17Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’

“Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe,

movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo

masiku onse a moyo wako.

18Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula

ndipo udzadya zomera zakuthengo.

19Kuti upeze chakudya udzayenera

kukhetsa thukuta,

mpaka utabwerera ku nthaka

pakuti unachokera kumeneko;

pakuti ndiwe fumbi

ku fumbi komweko udzabwerera.”

20Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.

21Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka. 22Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.” 23Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera. 24Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.

New International Version – UK

Genesis 3:1-24

The fall

1Now the snake was more crafty than any of the wild animals the Lord God had made. He said to the woman, ‘Did God really say, “You must not eat from any tree in the garden”?’

2The woman said to the snake, ‘We may eat fruit from the trees in the garden, 3but God did say, “You must not eat fruit from the tree that is in the middle of the garden, and you must not touch it, or you will die.” ’

4‘You will not certainly die,’ the snake said to the woman. 5‘For God knows that when you eat from it your eyes will be opened, and you will be like God, knowing good and evil.’

6When the woman saw that the fruit of the tree was good for food and pleasing to the eye, and also desirable for gaining wisdom, she took some and ate it. She also gave some to her husband, who was with her, and he ate it. 7Then the eyes of both of them were opened, and they realised that they were naked; so they sewed fig leaves together and made coverings for themselves.

8Then the man and his wife heard the sound of the Lord God as he was walking in the garden in the cool of the day, and they hid from the Lord God among the trees of the garden. 9But the Lord God called to the man, ‘Where are you?’

10He answered, ‘I heard you in the garden, and I was afraid because I was naked; so I hid.’

11And he said, ‘Who told you that you were naked? Have you eaten from the tree from which I commanded you not to eat?’

12The man said, ‘The woman you put here with me – she gave me some fruit from the tree, and I ate it.’

13Then the Lord God said to the woman, ‘What is this you have done?’

The woman said, ‘The snake deceived me, and I ate.’

14So the Lord God said to the snake, ‘Because you have done this,

‘Cursed are you above all livestock

and all wild animals!

You will crawl on your belly

and you will eat dust

all the days of your life.

15And I will put enmity

between you and the woman,

and between your offspring3:15 Or seed and hers;

he will crush3:15 Or strike your head,

and you will strike his heel.’

16To the woman he said,

‘I will make your pains in childbearing very severe;

with painful labour you will give birth to children.

Your desire will be for your husband,

and he will rule over you.’

17To Adam he said, ‘Because you listened to your wife and ate fruit from the tree about which I commanded you, “You must not eat from it,”

‘Cursed is the ground because of you;

through painful toil you will eat food from it

all the days of your life.

18It will produce thorns and thistles for you,

and you will eat the plants of the field.

19By the sweat of your brow

you will eat your food

until you return to the ground,

since from it you were taken;

for dust you are

and to dust you will return.’

20Adam3:20 Or The man named his wife Eve,3:20 Eve probably means living. because she would become the mother of all the living.

21The Lord God made garments of skin for Adam and his wife and clothed them. 22And the Lord God said, ‘The man has now become like one of us, knowing good and evil. He must not be allowed to reach out his hand and take also from the tree of life and eat, and live for ever.’ 23So the Lord God banished him from the Garden of Eden to work the ground from which he had been taken. 24After he drove the man out, he placed on the east side3:24 Or placed in front of the Garden of Eden cherubim and a flaming sword flashing to and fro to guard the way to the tree of life.