Genesis 3 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 3:1-24

Kuchimwa kwa Munthu

1Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’ ”

2Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu, 3koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’ ”

4“Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo. 5“Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”

6Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso. 7Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.

8Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo. 9Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”

10Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”

11Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”

12Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”

13Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?”

Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”

14Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi,

“Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse

ndi nyama zakuthengo zonse.

Udzayenda chafufumimba

ndipo udzadya fumbi

masiku onse a moyo wako.

15Ndipo ndidzayika chidani

pakati pa iwe ndi mkaziyo,

pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake;

Iye adzaphwanya mutu wako

ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”

16Kwa mkaziyo Iye anati,

“Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati;

ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana.

Udzakhumba mwamuna wako,

ndipo adzakulamulira.”

17Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’

“Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe,

movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo

masiku onse a moyo wako.

18Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula

ndipo udzadya zomera zakuthengo.

19Kuti upeze chakudya udzayenera

kukhetsa thukuta,

mpaka utabwerera ku nthaka

pakuti unachokera kumeneko;

pakuti ndiwe fumbi

ku fumbi komweko udzabwerera.”

20Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.

21Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka. 22Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.” 23Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera. 24Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.

New International Reader’s Version

Genesis 3:1-24

Adam and Eve Fall Into Sin

1The serpent was more clever than any of the wild animals the Lord God had made. The serpent said to the woman, “Did God really say, ‘You must not eat fruit from any tree in the garden’?”

2The woman said to the serpent, “We may eat fruit from the trees in the garden. 3But God did say, ‘You must not eat the fruit from the tree in the middle of the garden. Do not even touch it. If you do, you will die.’ ”

4“You will certainly not die,” the serpent said to the woman. 5“God knows that when you eat fruit from that tree, you will know things you have never known before. Like God, you will be able to tell the difference between good and evil.”

6The woman saw that the tree’s fruit was good to eat and pleasing to look at. She also saw that it would make a person wise. So she took some of the fruit and ate it. She also gave some to her husband, who was with her. And he ate it. 7Then both of them knew things they had never known before. They realized they were naked. So they sewed together fig leaves and made clothes for themselves.

8Then the man and his wife heard the Lord God walking in the garden. It was during the coolest time of the day. They hid from the Lord God among the trees of the garden. 9But the Lord God called out to the man. “Where are you?” he asked.

10“I heard you in the garden,” the man answered. “I was afraid, because I was naked. So I hid.”

11The Lord God said, “Who told you that you were naked? Have you eaten fruit from the tree I commanded you not to eat from?”

12The man said, “It’s the fault of the woman you put here with me. She gave me some fruit from the tree. And I ate it.”

13Then the Lord God said to the woman, “What have you done?”

The woman said, “The serpent tricked me. That’s why I ate the fruit.”

14So the Lord God spoke to the serpent. He said, “Because you have done this,

“You are set apart from all livestock

and all wild animals.

I am putting a curse on you.

You will crawl on your belly.

You will eat dust

all the days of your life.

15I will make you and the woman hate each other.

Your children and her children will be enemies.

Her son will crush your head.

And you will bite his heel.”

16The Lord God said to the woman,

“I will increase your pain when you give birth.

You will be in great pain when you have children.

You will long for your husband.

And he will rule over you.”

17The Lord God said to Adam, “You listened to your wife’s suggestion. You ate fruit from the tree I warned you about. I said, ‘You must not eat its fruit.’

“So I am putting a curse on the ground because of what you did.

All the days of your life you will have to work hard.

It will be painful for you to get food from the ground. 18You will eat plants from the field,

even though the ground produces thorns and prickly weeds.

19You will have to work hard and sweat a lot

to produce the food you eat.

You were made out of the ground.

You will return to it when you die.

You are dust,

and you will return to dust.”

20Adam named his wife Eve. She would become the mother of every living person.

21The Lord God made clothes out of animal skins for Adam and his wife to wear. 22The Lord God said, “Just like one of us, the man can now tell the difference between good and evil. He must not be allowed to reach out and pick fruit from the tree of life and eat it. If he does, he will live forever.” 23So the Lord God drove the man out of the Garden of Eden. He sent the man to farm the ground he had been made from. 24The Lord God drove him out and then placed angels on the east side of the garden. He also placed there a flaming sword that flashed back and forth. The angels and the sword guarded the way to the tree of life.