Genesis 28 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 28:1-22

1Choncho Isake anayitanitsa Yakobo namudalitsa nʼkumuwuzitsa kuti, “Usakwatire mkazi wa kuno ku Kanaani. 2Panopo upite ku Padanaramu, ku nyumba kwa Betueli abambo a amayi akowa, kumeneko ukakwatire mmodzi mwa ana aakazi a Labani, mlongo wa amayi akowa. 3Mulungu Wamphamvuzonse akudalitse iwe nakupatse ana ambiri mpaka udzasanduke gulu lalikulu la mitundu ya anthu. 4Mulunguyo akudalitse iwe monga mmene anamudalitsira Abrahamu kuti zidzukulu zako zidzalandira dziko limene ukukhalamo ngati mlendo kuti lidzakhale lawo. Ili ndi dziko limene Mulungu anapereka kwa Abrahamu.” 5Ndipo Isake anamulola Yakobo kuti anyamuke kupita ku Padanaramu kwa Labani mwana wa Betueli Mwaramu. Labani anali mlongo wa Rebeka, mayi wa Yakobo ndi Esau.

6Tsopano Esau anadziwa kuti Isake anadalitsa Yakobo ndi kumutumiza ku Padanaramu kuti akakwatire kumeneko. Anawuzidwanso kuti, “Usakwatire mkazi wa ku Kanaani.” 7Yakobo anamvera abambo ake ndi amayi ake ndi kupita ku Padanaramu. 8Ndiye pamenepo Esau anazindikira kuti abambo ake Isake sankakondwera ndi akazi a ku Kanaani; 9anapita kwa Ismaeli mwana wa Abrahamu nakwatira Mahalati mwana wa Ismaeli, mlongo wake wa Nebayoti. Anatero kuwonjezera akazi amene anali nawo kale.

Maloto a Yakobo pa Beteli

10Yakobo ananyamuka pa ulendo kuchoka ku Beeriseba kupita ku Harani. 11Atafika pa malo pena, anayima kuti agonepo chifukwa dzuwa linali litalowa. Anatenga mwala wina pomwepo natsamiritsapo mutu wake, ndipo anagona. 12Mʼmaloto, anaona makwerero oyimikidwa pansi ndipo anakafika kumwamba. Angelo a Mulungu amakwera ndi kutsika pa makwereropo. 13Tsono Yehova anayimirira pambali pake, nati, “Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu kholo lake la Isake abambo ako. Ndidzakupatsa iwe ndi zidzukulu zako dziko limene ukugonamolo. 14Zidzukulu zako zidzachuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi ndipo zidzabalalikira kumadzulo ndi kummawa, kumpoto ndi kummwera. Anthu onse adzalandira madalitso kudzera mwa iwe ndi zidzukulu zako. 15Ine ndili nawe pamodzi ndipo ndidzakuyangʼanira kulikonse upiteko, ndipo ndidzakubwezera ku dziko lino. Sindidzakusiya mpaka nditachita zimene ndakulonjezazi.”

16Yakobo atadzidzimuka, anati, “Zoonadi Yehova ali pa malo ano, ndipo ine sindinadziwe.” 17Tsono anachita mantha ndipo anati, “Malo ano ndi woopsa ndithu. Zoonadi pano ndi pa nyumba ya Mulungu ndi khomo la kumwamba.”

18Mmamawa mwake Yakobo anatenga mwala umene anatsamira mutu wake uja nawuyimika ngati chipilala ndi kuthira mafuta pamwamba pake 19Iye anawatcha malowo Beteli, ngakhale kuti poyamba mzindawo ankawutcha Luzi.

20Pamenepo Yakobo analumbira kwa Yehova nati, “Ngati inu Mulungu mukhala ndi ine, kundiyangʼanira pa ulendo wangawu ndi kundipatsa chakudya ndi chovala; 21ngati inu mudzandibweretsa kwathu mu mtendere, ndiye kuti mudzakhala Mulungu wanga, 22ndipo mwala uwu ndawuyimikawu udzakhala Nyumba ya Mulungu. Ine ndidzakupatsani chakhumi cha zinthu zonse zimene mudzandipatse.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Начало 28:1-22

1Исхак позвал Якуба, благословил28:1 Или: «приветствовал». его и дал ему такой наказ:

– Не женись на хананеянке. 2Немедленно отправляйся в Паддан-Арам, в дом Бетуила, отца твоей матери. Возьми там себе жену из дочерей Лавана, брата твоей матери. 3Да благословит тебя Бог Всемогущий и сделает тебя плодовитым и размножит тебя, чтобы от тебя произошло множество народов. 4Да наделит Он тебя и твоих потомков благословением Ибрахима, чтобы ты приобрёл во владение землю, на которой ты ныне живёшь как пришелец; землю, которую Аллах дал Ибрахиму.

5Потом Исхак простился с Якубом, и тот пошёл в Паддан-Арам, к Лавану, сыну арамея Бетуила. Лаван был братом Рабиги, матери Якуба и Есава.

6Есав узнал, что Исхак благословил Якуба и послал его в Паддан-Арам, чтобы взять оттуда жену, и что он, благословляя, наказал ему: «Не женись на хананеянке», 7и что Якуб послушался отца и мать и пошёл в Паддан-Арам. 8Тогда Есав понял, как не по душе были хананеянки его отцу Исхаку; 9и он пошёл к Исмаилу и взял себе в жёны – помимо тех, которые у него уже были, – Махалату, сестру Навайота, дочь Исмаила, сына Ибрахима.

Сон Якуба и обещание Аллаха

10Якуб оставил Беэр-Шеву и направился в Харран. 11Дойдя до некоего места, он остановился на ночь, потому что солнце уже село. Он взял там один из камней, положил себе под голову и лёг спать. 12Ему приснился сон: он увидел лестницу, которая стояла на земле, а верхушкой достигала неба; и ангелы Аллаха поднимались и спускались по ней. 13Над ней стоял Вечный и говорил:

– Я – Вечный, Бог твоего деда Ибрахима и Бог отца твоего Исхака; землю, на которой ты сейчас лежишь, Я дам тебе и твоим потомкам. 14Твои потомки будут многочисленны, как земная пыль, и ты распространишься на запад и на восток, на север и на юг. Все народы на земле получат благословение через тебя и твоё потомство. 15Я с тобой и буду охранять тебя, куда бы ты ни пошёл, и верну тебя в эту землю. Я не покину тебя и исполню всё, что обещал тебе.

16Проснувшись, Якуб подумал: «Истинно, на этом месте Вечный, а я и не знал». 17Ему было страшно, и он сказал:

– Как устрашает это место! Не иначе как здесь дом Аллаха, и это – врата небес.

18Якуб поднялся рано утром, взял камень, который он клал себе под голову, поставил его памятным знаком и возлил на него масло28:18 В те времена люди, возливая оливковое масло на что-либо, тем самым посвящали это Аллаху.. 19Он назвал это место Вефиль («дом Всевышнего»), хотя вначале тот город назывался Луз. 20Затем Якуб дал клятву, сказав:

– Если Аллах будет со мной и сохранит меня в этом странствии, даст мне хлеба в пищу и одежду на плечи, 21так что я вернусь и буду жить в мире в доме моего отца, и если Вечный будет моим Богом, 22то этот камень, который я поставил, будет памятным знаком, и здесь будет место поклонения Аллаху28:22 Букв.: «будет домом Аллаха»., и от всего, что Он даст мне, я дам Ему десятую часть.