Genesis 27 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 27:1-46

Yakobo Alandira Madalitso kwa Isake

1Isake atakalamba maso ake anachita khungu mwakuti sankatha kuona. Iye anayitana mwana wake wamkulu Esau nati kwa iye, “Mwana wanga.”

Iye anayankha, “Ine abambo.”

2Isake anati, “Tsopano ine ndakalamba, ndipo sindidziwa tsiku langa lakufa. 3Tsono tenga zida zako, muvi wako ndi uta, pita kuthengo ukandiphere nyama. 4Undikonzere chakudya chabwino monga muja ndimakonderamu ndipo ubwere nacho kwa ine kuti ndidye ndi kuti ndikudalitse ndisanamwalire.”

5Koma Rebeka amamvetsera pamene Isake amayankhula ndi mwana wake Esau. Esau atanyamuka kupita kuthengo kukaphera abambo ake nyama, 6Rebeka anati kwa mwana wake Yakobo, “Taona ndamva abambo ako akuwuza mʼbale wako Esau kuti, 7‘Bweretsere nyama yakutchire ndipo undikonzere chakudya chokoma kuti ndidye; kuti ndikudalitse pamaso pa Yehova ndisanamwalire.’ 8Tsopano mwana wanga, mvetsetsa ndipo uchite zimene ndikuwuze: 9Pita ku khola, ukatenge ana ambuzi abwino awiri, kuti ndikonzere abambo ako chakudya chokoma monga amakondera. 10Kenaka upite nacho chakudyacho kwa abambo ako kuti adye ndi kukudalitsa asanafe.”

11Koma Yakobo anati kwa Rebeka amayi ake, “Komatu mʼbale wanga Esau ndi munthu wa khungu la ubweya zedi, ndipo ine ndine munthu wa khungu losalala. 12Mwina abambo anga adzandikhudza, ndipo ndidzaoneka kuti ndawapusitsa. Tsono ndizadzitengera temberero mʼmalo mwa madalitso.”

13Amayi ake anati kwa iye, “Mwana wanga, temberero limenelo ligwere ine. Iwe ungochita zimene ine ndikukuwuza; pita kanditengere timbuzito.”

14Choncho anapita nakatenga timbuzito ndi kubwera nato kwa amayi ake. Choncho Rebeka anaphika chakudya chokoma monga momwe Isake amakondera. 15Tsono Rebeka anatenga zovala zabwino kwambiri za Esau mwana wake wamkulu zimene zinali mʼnyumba namuveka Yakobo. 16Anamuvekanso manja ake ndi khosi lake ndi zikopa za mwana wambuzi. 17Kenaka, anamupatsa Yakobo chakudya chokoma chija chimene anaphika pamodzi ndi buledi.

18Yakobo anapita kwa abambo ake ndipo anati, “Abambo anga.”

Ndipo anayankha, “Eya, kodi ndiwe mwana wanga uti?”

19Yakobo anati kwa abambo ake, “Ndine Esau mwana wanu woyamba. Ndachita monga munandiwuzira. Chonde dzukani ndi kukhala tsonga kuti mudyeko nyama ndakukonzeraniyi kuti tsono mundidalitse.”

20Isake anafunsa mwana wake, “Wayipeza msanga chotere bwanji mwana wanga?”

Iye anayankha, “Yehova Mulungu wanu anandithandiza kuti ndiyipeze.”

21Pamenepo Isake anati kwa Yakobo, “Tabwera pafupi ndikukhudze mwana wanga, kuti ndidziwedi ngati uli mwana wanga Esau kapena ayi.”

22Yakobo anasendera kufupi ndi abambo ake Isake ndipo anamukhudza nati, “Mawuwa ndi mawu a Yakobo koma mikonoyi ndi mikono ya Esau.” 23Sanamuzindikire, popeza mikono yake inali ndi ubweya ngati ya mʼbale wake Esau; choncho anamudalitsa. 24Isake anafunsa, “Kodi ndiwedi mwana wanga Esau?”

Yakobo anayankha, “Inde ndine.”

25Ndipo iye anati, “Mwana wanga, patseko nyama yakoyo ndidye kuti ndikudalitse.”

Yakobo anabwera ndi nyama ija kwa Isake ndipo anadya. Kenaka anamupatsanso vinyo ndipo anamwa. 26Tsono Isake anati kwa Yakobo, “Bwera kuno mwana wanga undipsompsone.”

27Choncho anapita namupsompsona. Apa Isake anamva fungo la zovala zake, ndipo anamudalitsa nati,

“Haa, fungo la mwana wanga

lili ngati fungo la munda

umene Yehova waudalitsa.

28Mulungu akugwetsere mame akumwamba

ndipo minda yako ibale tirigu wambiri

ndi vinyo watsopano.

29Mitundu ya anthu ikutumikire iwe

ndipo anthu akugwadire iwe.

Ukhale wolamula abale ako,

ndipo ana aamuna a amayi ako akugwadire.

Amene akutemberera iwe atembereredwe

ndipo amene adalitsa iwe adalitsike.”

30Isake atatsiriza kudalitsa Yakobo, atangochoka pamaso pa abambo akewo, Esau anabwera kuchokera kosaka kuja. 31Nayenso anakonza chakudya chokoma nabwera nacho kwa abambo ake. Ndipo anati kwa iye, “Chonde abambo, dzukani mukhale tsonga kuti mudye nyamayi ndi kuti mundidalitse.”

32Abambo ake, Isake, anamufunsa kuti, “Ndiwe yani?”

Iye anayankha, “Ndine mwana wanu woyamba Esau.”

33Isake ananjenjemera kwambiri nati, “Nanga ndani uja anakapha nyama kutchire nʼkudzandipatsa? Ine ndadya kale, ndadya nyamayo iwe utangotsala pangʼono kubwera ndipo ndamudalitsa ndipo adzakhaladi wodalitsika.”

34Esau atamva mawu a abambo ake, analira mokweza ndi mowawidwa mtima nati kwa abambo ake, “Inenso dalitseni abambo anga!”

35Koma iye anati, “Mʼbale wako anabwera mwachinyengo ndipo watenga madalitso ako.”

36Esau anati, “Kodi nʼchifukwa chake iyeyu dzina lake lili Yakobo eti? Aka nʼkachiwiri kundinyenga: Anatenga ukulu wanga, pano watenga madalitso anga!” Kenaka anafunsa, “Kodi simunandisungireko ena madalitsowo?”

37Koma Isake anamuyankha nati, “Ndamudalitsa iye kuti akhale wokulamulira iwe. Ndaperekanso abale ake onse kuti akhale omutumikira iye, ndipo ndamudalitsa ndi tirigu wambiri, ndi vinyo watsopano. Ndiye ndingakuchitirenso chiyani mwana wanga?”

38Esau anati kwa abambo ake, “Kodi muli ndi dalitso limodzi lokhali, abambo anga? Inenso mundidalitse chonde abambo anga!” Pomwepo Esau analira mokuwa.

39Tsono Isake abambo ake anamuyankha kuti,

“Malo ako okhalapo

sadzabala dzinthu,

ndipo mvula sidzagwa pa minda yako.

40Udzakhala ndi moyo podalira lupanga

ndipo udzatumikira mʼbale wako.

Koma idzafika nthawi

pamene udzakhala mfulu

udzachotsa goli lake mʼkhosi mwako.”

Yakobo Athawira kwa Labani

41Ndipo Esau anamusungira chiwembu Yakobo chifukwa cha madalitso amene abambo ake anamupatsa. Esau anati kwa iye yekha, “Masiku olira abambo anga ayandikira; pambuyo pake ndidzamupha mʼbale wangayu Yakobo.”

42Pamene Rebeka anamva zimene mwana wake wamkulu Esau ankaganiza, anayitanitsa Yakobo nati kwa iye, “Mʼbale wako Esau akulingalira zakuti akuphe kuti akulipsire. 43Tsopano mwana wanga, chita zimene ndinene: Nyamuka tsopano, uthawire kwa mlongo wanga Labani ku Harani. 44Ukakhale naye kwa kanthawi mpaka mkwiyo wa mʼbale wako utatsika. 45Tsono mkwiyo wa mʼbale wakoyo ukadzatsika ndi kuyiwala zonse wamuchitirazi, ndidzatuma munthu kuti adzakutenge. Nanga nditayirenji nonse awiri nthawi imodzi?”

46Tsono Rebeka anati kwa Isake, “Ine sindikukondwera nawo anamwali a Chihiti. Ndipo ngati Yakobo angapeze mbeta kuno mwa anamwali a Chihitiwa, ndiye kuli bwino kungofa.”

Священное Писание

Начало 27:1-46

Якуб обманом получает благословение отца

1Когда Исхак состарился, и глаза его так ослабли, что он ничего не видел, он позвал Есава, своего старшего сына, и сказал ему:

– Сын мой!

– Я здесь, – ответил Есав.

2Исхак сказал:

– Я уже стар и не знаю, сколько мне ещё осталось жить. 3Возьми же своё оружие – колчан и лук – и выйди в поле добыть мне дичи. 4Приготовь мою любимую еду и принеси мне поесть, чтобы я благословил тебя перед смертью.

5Рабига слышала, как Исхак говорил со своим сыном Есавом, и когда Есав ушёл в поле, чтобы настрелять и принести дичи, 6Рабига сказала своему сыну Якубу:

– Я слышала, как твой отец сказал твоему брату Есаву: 7«Принеси дичи и приготовь мне вкусной еды, чтобы я благословил тебя перед Вечным, прежде чем умру». 8Слушай же меня внимательно, сын мой, и делай, как я тебе скажу. 9Пойди к стаду и принеси мне двух лучших козлят, чтобы мне приготовить вкусную еду для твоего отца, такую, как он любит. 10Потом отнеси её отцу, он поест и благословит тебя перед смертью.

11Якуб сказал Рабиге, своей матери:

– Но мой брат Есав весь волосат, а у меня кожа гладкая. 12Что, если отец ощупает меня? Я окажусь перед ним обманщиком и скорее навлеку на себя проклятие, а не благословение.

13Мать сказала ему:

– Проклятие пусть будет на мне, сын мой, а ты делай, как я говорю: пойди и принеси козлят.

14Он пошёл, взял козлят и принёс их матери, и она приготовила вкусную еду, такую, как любил его отец. 15Потом Рабига взяла лучшую одежду своего старшего сына Есава, какая была у неё в доме, и надела на младшего Якуба, 16а его руки и гладкую часть шеи покрыла шкурами козлят. 17И она дала своему сыну Якубу вкусную еду и лепёшки, которые приготовила.

18Он пришёл к отцу и сказал:

– Отец мой.

– Вот я, – ответил тот. – Ты который из моих сыновей?

19Якуб сказал отцу:

– Я – Есав, твой первенец. Я сделал, как ты сказал. Прошу, приподнимись, сядь и поешь моей дичи, чтобы ты мог благословить меня.

20Исхак спросил сына:

– Как же ты нашёл её так быстро, сын мой?

– Вечный, твой Бог, даровал мне успех, – ответил он.

21Исхак сказал Якубу:

– Подойди ближе, чтобы мне ощупать тебя, сын мой, действительно ли ты мой сын Есав или нет.

22Якуб подошёл ближе к своему отцу Исхаку, который ощупал его и сказал:

– Голос – как голос Якуба, но руки – как руки Есава.

23Он не узнал его, потому что руки у него были волосатые, как у Есава; и он благословил его.

24– Действительно ли ты сын мой Есав? – спросил Исхак; и он ответил:

– Да, это я.

25Исхак сказал:

– Сын мой, поднеси мне твою дичь поближе, и я поем, а потом благословлю тебя.

Якуб дал ему еду, и он поел, принёс вина, и он выпил.

26Потом его отец Исхак сказал ему:

– Подойди, сын мой, и поцелуй меня.

27Он подошёл и поцеловал его, и Исхак почувствовал запах его одежды и благословил его, сказав:

– Ах, запах моего сына, как запах поля, которое благословил Вечный. 28Пусть даст тебе Всевышний от небесной росы и от плодородия земли в изобилии зерна и молодого вина. 29Да служат тебе племена, и да поклонятся тебе народы. Будь господином над твоими братьями, и да склонятся перед тобой сыновья твоей матери. Да будет проклят проклинающий тебя, а благословляющий да будет благословен.

30Как только Исхак закончил благословение, и едва лишь Якуб вышел от отца, как пришёл с охоты его брат Есав. 31Он тоже приготовил вкусной еды и принёс отцу. Он сказал ему:

– Отец, приподнимись, сядь и поешь моей дичи, а потом благослови меня.

32Его отец Исхак спросил:

– Кто ты?

– Я твой сын, – ответил он, – твой первенец, Есав.

33Исхак весь задрожал и сказал:

– Кто же был тот, другой, который добыл дичи и принёс мне? Я ел её как раз перед твоим приходом и благословил его – он теперь и будет благословен!

34Услышав слова отца, Есав громко и горько закричал и сказал отцу:

– Благослови и меня, и меня тоже, отец!

35Но тот ответил:

– Твой брат пришёл с хитростью и отнял у тебя благословение.

36Есав сказал:

– Не по праву ли он назван Якубом?27:36 На языке оригинала наблюдается игра слов: имя Якуб (Яаков) и глагол «перехитрить» (акав). Дважды он обошёл меня: взял моё первородство, а теперь и моё благословение! – И спросил: – Не осталось ли у тебя благословения и для меня?

37Исхак ответил Есаву:

– Я сделал его господином над тобой, и всю его родню отдал ему в слуги, и одарил его хлебом и молодым вином. Что же я могу теперь сделать для тебя, мой сын?

38Есав сказал отцу:

– У тебя что же, только одно благословение, отец? Благослови и меня, отец мой!

И громко заплакал.

39Его отец Исхак ответил ему:

– Будет обитание твоё вдали от плодородия земли, вдали от росы небесной свыше. 40Ты будешь жить мечом и будешь служить своему брату. Но когда ты восстанешь, ты сбросишь его ярмо со своей шеи.

Побег Якуба в Харран к Лавану

41Есав затаил злобу на Якуба из-за благословения, которое дал ему отец, и сказал себе: «Дни плача по отцу близки – тогда я убью моего брата Якуба».

42Рабиге передали, что сказал её старший сын Есав, и она послала за младшим сыном, Якубом, и сказала ему:

– Твой брат Есав утешает себя мыслью убить тебя. 43Мой сын, сделай, как я скажу: немедленно беги в Харран к моему брату Лавану. 44Поживи у него какое-то время, пока не утихнет ярость твоего брата; 45когда же его гнев утихнет, и он забудет то, что ты ему сделал, тогда я пошлю сказать тебе, что пора возвращаться. Зачем мне терять вас обоих в один день?

46Потом Рабига сказала Исхаку:

– Я жизни не рада из-за этих дочерей хеттейских. Если Якуб возьмёт себе в жёны местную женщину, такую вот хеттеянку, как эти, то зачем мне и жить?