Genesis 26 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 26:1-35

Isake ndi Abimeleki

1Tsono kunagwa njala ina mʼdzikomo kuwonjezera pa ija ya poyamba ya nthawi ya Abrahamu ndipo Isake anapita kwa Abimeleki mfumu ya Afilisti ku Gerari. 2Yehova anadza kwa Isake nati, “Usapite ku Igupto; koma ukhale mʼdziko limene ndidzakuwuza kuti ukakhalemo. 3Khala mʼdziko lino ndipo ndidzakhala nawe ndi kukudalitsa. Pakuti kwa iwe ndi zidzukulu zako ndidzapereka mayiko onsewa. Choncho ndidzakwaniritsa pangano limene ndinalumbira kwa Abrahamu, abambo ako. 4Zidzukulu zako ndidzazichulukitsa ngati nyenyezi za mu mlengalenga ndi kuzipatsa mayiko onsewa. Ndiponso anthu onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa zidzukulu zako, 5chifukwa Abrahamu anandimvera, nasunga malamulo anga onse.” 6Choncho Isake anakhala ku Gerari.

7Anthu akumaloko atafunsa Isake za mkazi wake, iye anati, “Ndi mlongo wanga ameneyu.” Iye anaopa kunena kuti, “Ndi mkazi wanga ameneyu,” popeza ankaganiza kuti anthu akumeneku akhoza kumupha ndi kukwatira mkazi wake popeza Rebeka anali wokongola.

8Isake atakhalako kumeneko nthawi yayitali, Abimeleki mfumu ya Afilisti, anasuzumira pa zenera kuyangʼana kunja, ndipo anaona Isake akugwiragwira Rebeka, mkazi wake. 9Choncho Abimeleki anamuyitanitsa Isake nati, “Uyu ndi mkazi wako ndithu! Nanga bwanji umati, ‘Ndi mlongo wanga’?”

Ndipo Isake anamuyankha kuti, “Ine ndimaganiza kuti ndingataye moyo wanga chifukwa cha iyeyu.”

10Tsono Abimeleki anati, “Nʼchiyani chimene watichitira? Mmodzi mwa anthuwa anatsala pangʼono kugona ndi mkazi wako ndipo ukanatisandutsa ife kukhala olakwa.”

11Choncho Abimeleki analamula anthu ake onse nati, “Aliyense amene avutitse munthu uyu pamodzi ndi mkazi wake adzaphedwa ndithu.”

12Isake anadzala mbewu mʼmunda, ndipo chaka chomwecho anakolola zinthu zambiri chifukwa Yehova anamudalitsa. 13Isake analemera. Chuma chake chinkachulukirachulukira mpaka anasanduka munthu wolemera kwambiri. 14Anali ndi nkhosa, ngʼombe ndi antchito ambiri mwakuti Afilisti anamuchitira nsanje. 15Nthawi iyi nʼkuti Afilisti atakwirira ndi dothi zitsime zonse zimene antchito abambo ake Abrahamu anakumba mu nthawi ya abambo akewo.

16Ndipo Abimeleki anati kwa Isake, “Muchoke pakati pathu chifukwa mwasanduka wamphamvu kuposa ife.”

17Choncho Isake anachokako kumeneko nakakhala ku chigwa cha Gerari kumene anakhazikikako. 18Isake anafukulanso zitsime zija zimene zinakumbidwa mu nthawi ya abambo ake Abrahamu. Atamwalira Abrahamu, Afilisti anakwirira zitsimezi. Tsono anazitcha mayina omwewo amene abambo ake anazitcha.

19Antchito a Isake anakumba mʼchigwamo ndipo anapezamo kasupe wa madzi. 20Koma abusa a ku Gerari anakangana ndi abusa a Isake nati, “Madziwa ndi athu.” Motero iye anachitcha chitsimecho Mkangano chifukwa anakangana naye. 21Kenaka iwo anakumba chitsime china, koma anakangananso chifukwa cha chitsimecho. Choncho anachitcha dzina lakuti Chidani. 22Anachokapo pamenepo nakakumba china. Koma apa sanakanganiranenso ndi munthu. Iye anachitcha Kutakasuka, nati, “Tsopano Yehova watipatsa ife malo otakasukirako ndipo tilemera muno.”

23Kenaka Isake anachoka ku malo kuja kupita ku Beeriseba. 24Usiku umenewo Yehova anadza kwa Isake nati, “Ine ndine Mulungu wa abambo ako Abrahamu. Usachite mantha popeza Ine ndili ndi iwe. Ndidzakudalitsa ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri chifukwa cha mtumiki wanga Abrahamu.”

25Isake anamanga guwa lansembe pamenepo ndipo anapembedza Yehova. Pomwepo anamanga tenti yake, ndipo antchito ake anakumba chitsime.

26Abimeleki pamodzi ndi Ahuzati mlangizi wake ndi Fikolo mkulu wa ankhondo ake anabwera kwa Isake kuchokera ku Gerari. 27Tsopano Isake anawafunsa kuti, “Bwanji mwabwera kwa ine, popeza munandichitira nkhanza ndi kundithamangitsa?”

28Iwo anayankha, “Tsopano tadziwa kuti Yehova anali ndi iwe; ndiye taganiza kuti inu ndi ife tichite lumbiro. Ife tichite pangano ndi inu 29kuti inu simudzatichitira zoyipa monga ifenso sitinakuchitireni nkhondo. Ife tinakuchitirani zabwino zokhazokha, ndipo tinakulolani kuti musamuke kuchoka kwathu mu mtendere. Tsopano Yehova wakudalitsani.”

30Tsono Isake anawakonzera phwando, ndipo anadya ndi kumwa. 31Mmawa wake aliyense analumbira pangano kwa mnzake. Tsono Isake anawalola kuti anyamuke ndipo anamusiya mu mtendere.

32Tsiku limenelo, antchito a Isake anabwera namuwuza za chitsime chimene anakumba. Iwo anati, “Tawapeza madzi!” 33Iye chitsimecho anachitcha Pangano. Nʼchifukwa chake mzindawu umatchedwa Beeriseba mpaka lero.

34Pamene Esau anali ndi zaka 40, anakwatira Yuditi mwana wamkazi wa Beeri Mhiti. Anakwatiranso Basemati mwana wa mkazi wa Eloni Mhiti. 35Akazi awiriwa anasandutsa Isake ndi Rebeka kukhala ndi moyo wa madandawulo nthawi zonse.

New Russian Translation

Бытие 26:1-35

Исаак и Ревекка у Авимелеха

1В земле был голод, – не тот прежний голод, который был при Аврааме, – и Исаак пошел к Авимелеху, царю филистимлян, в Герар. 2Господь явился Исааку и сказал:

– Не иди в Египет; живи на той земле, где Я скажу тебе жить. 3Поселись на этой земле на время, и Я буду с тобой и благословлю тебя, потому что Я исполню клятву, которую дал твоему отцу Аврааму, и дам все эти земли тебе и твоим потомкам. 4Я сделаю твое потомство многочисленным, как звезды на небе, и дам им все эти земли, и через твое потомство получат благословение все народы на земле, 5потому что Авраам слушался Меня и хранил Мои повеления, заповеди, уставы и законы.

6И Исаак поселился в Гераре. 7Когда жители того места спросили у него о его жене, он сказал: «Это моя сестра», потому что боялся сказать: «Это моя жена». Он думал: «Жители этого места могут убить меня из-за Ревекки, потому что она красива».

8Однажды, когда Исаак уже долгое время прожил там, Авимелех, царь филистимлян, выглянул из окна и увидел, как Исаак ласкает свою жену Ревекку. 9Авимелех призвал Исаака и сказал:

– Итак, она твоя жена! Почему же ты сказал: «Она моя сестра»?

Исаак ответил ему:

– Потому что я думал, что могу за нее поплатиться жизнью.

10Тогда Авимелех сказал:

– Что же ты сделал с нами? Один из мужчин мог лечь с твоей женой, и ты навлек бы на нас вину.

11Авимелех приказал всему народу:

– Всякий, кто тронет этого человека или его жену, непременно будет предан смерти.

Спор с филистимлянами о колодцах

12Исаак засеял поля в той земле и в тот же год собрал урожай стократно, и Господь благословил его: 13он разбогател, и состояние его все росло, пока он не стал очень богатым. 14У него были такие большие стада мелкого и крупного скота и столько слуг, что филистимляне завидовали ему. 15Они засыпали землей все колодцы, которые еще во времена его отца выкопали слуги отца его Авраама.

16Авимелех сказал Исааку:

– Уходи от нас; ты стал слишком силен для нас.

17Исаак ушел оттуда, поселился в герарской долине и обосновался там. 18Исаак расчистил колодцы, которые были выкопаны во времена его отца Авраама, а затем засыпаны филистимлянами после его смерти, и дал им те же названия, какие прежде дал его отец.

19Слуги Исаака стали копать в долине и открыли там колодец с родниковой водой, 20но герарские пастухи затеяли ссору с пастухами Исаака, говоря: «Это наша вода!» Он назвал колодец Есек26:20 По-еврейски это название означает «спор»., потому что они спорили с ним. 21Потом они выкопали другой колодец, но и из-за него вышла ссора, поэтому он назвал его Ситна26:21 По-еврейски это название означает «вражда».. 22Он ушел оттуда и выкопал еще один колодец, из-за которого ссоры не было, и он назвал его Реховот26:22 По-еврейски это название означает «просторные места»., говоря: «Теперь Господь дал нам место, и мы умножимся в этой земле».

23Он направился оттуда в Вирсавию. 24В ту ночь Господь явился ему и сказал:

– Я – Бог твоего отца Авраама. Не бойся, Я с тобой. Я благословлю тебя и увеличу число твоих потомков ради Моего слуги Авраама.

25Исаак построил там жертвенник и призвал имя Господа и поставил там шатер, а слуги его выкопали колодец.

26Авимелех пришел к нему из Герара вместе с Ахузатом, своим личным советником, и Фихолом, начальником его войска. 27Исаак спросил их:

– Зачем вы пришли, ведь вы были враждебны ко мне и прогнали меня?

28Они ответили:

– Нам теперь ясно, что с тобой Господь, и мы решили, что у нас должно быть клятвенное соглашение, между нами и тобой. Давай заключим союз, 29что ты не причинишь нам вреда, как и мы не тронули тебя, но всегда обходились с тобой хорошо и отпустили тебя с миром. А теперь ты благословлен Господом.

30Исаак устроил для них пир, и они ели и пили. 31На другой день рано утром они дали друг другу клятву; Исаак простился с ними, и они ушли от него с миром.

32В тот же день слуги Исаака пришли и рассказали ему о колодце, который они выкопали. Они сказали:

– Мы нашли воду!

33Он назвал его Шева26:33 По звучанию это слово напоминает слово «клятва»., и до сего дня имя этого города – Вирсавия26:33 Евр.: «Беэр-Шева». По-еврейски это название означает «колодец клятвы» и «колодец семи» (см. также 21:31)..

Жены Исава

34Когда Исаву было сорок лет, он женился на Иегудифи, дочери хетта Беэра, и на Басемате, дочери хетта Елона; 35и от них было много огорчения Исааку и Ревекке.