Genesis 23 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 23:1-20

Kumwalira kwa Sara

1Sara anakhala ndi moyo zaka 127. 2Anamwalirira ku Kiriyati-Araba, kumeneku ndi ku Hebroni, mʼdziko la Kanaani, ndipo Abrahamu anapita kukakhuza maliro a Sara, namulirira.

3Kenaka Abrahamu ananyamuka pamene panali mtembo wa mkazi wakepo kupita kukayankhula ndi anthu a ku Hiti. Ndipo anati, 4“Ine ndine mlendo wongoyendayenda kwanu kuno. Bwanji mundigulitse malo woti akhale manda kuti ndiyikepo thupi la mkazi wanga.”

5Anthu a ku Hiti aja anamuyankha Abrahamu kuti, 6“Tatimverani mbuye wathu, inu ndinu mwana wa mfumu wamkulu pakati pathu. Chonde ikani thupi la mkazi wanu mʼmanda aliwonse amene mungafune. Palibe mmodzi wa ife amene adzakukanizani manda ake kuti musayike mkazi wanu.”

7Tsono Abrahamu anayimirira naweramira anthu a dziko la Hiti aja 8nati, “Ngati mwaloladi kuti ndiyike mkazi wanga kuno, ndiye ndimvereni. Mundipemphere kwa Efroni mwana wa Zohari 9kuti andigulitse phanga la Makipela, limene lili kumapeto kwa munda wake. Mumupemphe kuti andigulitse pamtengo wake ndithu inu mukuona kuti akhale manda.”

10Pamenepo nʼkuti Efroni Mhiti ali pomwepo pakati pa anthuwo amene anabwera ku chipata cha mzindawo. Ndipo onse akumva anamuyankha Abrahamu 11nati, “Ayi mbuye wanga tandimverani, ine ndikukupatsani mundawo ndiponso phanga limene lili mʼmenemo. Ndikukupatsani malowa pamaso pa anthu a mtundu wanga. Chonde ikani mtembo wamkazi wanu.”

12Apo Abrahamu anaweramanso mwaulemu pamaso pa anthu a mʼdzikolo 13ndipo anthu onse akumva Abrahamu anati kwa Efroni, “Ngati kungatheke, chonde ndimvereni. Ine ndichita kugula mundawu. Landirani ndalama za mundawu kuti ine ndiyike mkazi wanga mʼmenemo.”

14Koma Efroni anamuyankha Abrahamu nati, 15“Mundimvere mbuye wanga; mundawo mtengo wake ndi masekeli asiliva okwana 400. Koma zimenezo nʼchiyani pakati pa ine ndi inu? Ikani mtembo wa mkazi wanu.”

16Abrahamu anavomera mtengo umene ananena Efroni Ahiti onse akumva ndipo anamuwerengera masekeli asiliva okwana 400 monga mwa mtengo wa ndalama umene amalonda a nthawi imeneyo ankagwiritsa ntchito.

17Choncho munda wa Efroni wa ku Makipela umene unali kufupi ndi Mamre, kuphatikiza munda, phanga linali mʼmenemo pamodzi ndi mitengo yonse ya mʼmundamo, zinaperekedwa 18kwa Abrahamu ngati chuma chake pamaso pa anthu onse a ku Hiti amene anabwera ku chipata cha mzindawo. 19Zitatha izi, Abrahamu anayika mkazi wake Sara mʼphanga la mʼmunda wa ku Makipela, kufupi ndi ku Mamre (kumene ndi ku Hebroni) mʼdziko la Kanaani. 20Choncho Ahiti anapereka munda pamodzi ndi phanga la mʼmenemo kwa Abrahamu kuti akhale manda.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

創世記 23:1-20

亞伯拉罕買地葬撒拉

1撒拉享年一百二十七歲, 2迦南境內的基列·亞巴,即希伯崙去世。亞伯拉罕在那裡痛哭,哀悼她。 3他從妻子屍體旁邊站起來對人說: 4「我是寄居在你們這裡的異鄉人,請你們給我一塊地,我好埋葬我的亡妻。」 5人回答說: 6「我主,請聽我們說,你在我們中間是一位尊貴的王子,你可以選我們這裡最好的墳地,沒有人會反對你使用他的墳地埋葬你的妻子。」 7亞伯拉罕就向他們下拜,說: 8「如果你們真的准我安葬妻子,就請你們代我求瑣轄的兒子以弗崙9請他當著你們的面,把他田地盡頭的麥比拉洞按實價賣給我作墳地。」

10當時以弗崙正坐在人當中,於是他在城門口人聚集的地方當眾答覆亞伯拉罕說: 11「不可!我主,請聽我說,我當著族人的面,把那塊地和山洞送給你,你只管去安葬你的妻子!」 12亞伯拉罕向當地的人下拜, 13當眾對以弗崙說:「你若願意,請聽我說,我要把地錢給你,請你收下,好讓我安葬我的妻子。」 14以弗崙回答說: 15「我主,請聽我說,四公斤半銀子的地對你我來說算什麼呢?去安葬你的妻子吧!」 16於是,亞伯拉罕就照以弗崙當眾提出的價錢,按通用的重量單位秤了四公斤半銀子給他。

17這樣,以弗崙麥比拉、靠近幔利的那塊地和山洞及地界內所有的樹木, 18都歸了亞伯拉罕。這是在城門口的人面前買下的。

19之後,亞伯拉罕把妻子撒拉安葬在迦南幔利附近、麥比拉田間的洞裡。幔利就是希伯崙20這塊人的地和其中的山洞從此成了亞伯拉罕家的墳地。