Genesis 21 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 21:1-34

Kubadwa kwa Isake

1Yehova anakomera mtima Sara monga ananenera, ndipo Yehovayo anachita monga momwe analonjezera. 2Sara anakhala ndi pathupi ndipo anamuberekera Abrahamu mwana wamwamuna mu ukalamba wake, pa nyengo imene Mulungu anamulonjeza. 3Abrahamu anapereka dzina loti Isake kwa mwana wamwamuna amene Sara anamuberekera. 4Isake atakwanitsa masiku asanu ndi atatu, Abrahamu anamuchita mdulidwe monga Mulungu anamulamulira. 5Abrahamu anali ndi 100 pamene mwana wake Isake anabadwa.

6Sara anati, “Mulungu wandibweretsera mseko, ndipo aliyense amene adzamva zimenezi adzaseka nane pamodzi.” 7Ndipo anawonjezera kuti, “Ndani akanamuwuza Abrahamu kuti Sara nʼkudzayamwitsako ana? Chonsecho ndamubalira mwana wamwamuna kuwukalamba wake.”

Kuchotsedwa kwa Hagara ndi Ismaeli

8Mwana uja anakula mpaka kumuletsa kuyamwa. Tsiku lomuletsa Isake kuyamwa, Abrahamu anakonza phwando lalikulu. 9Koma Sara anaona kuti mwana wamwamuna amene Hagara Mwigupto anamuberekera Abrahamu amamuseka, 10ndipo anati kwa Abrahamu, “Muchotse mdzakazi ndi mwana wake wamwamunayu, pakuti mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wanga Isake.”

11Nkhaniyi inamumvetsa chisoni kwambiri Abrahamu chifukwa imakhudza mwana wake. 12Koma Mulungu anamuwuza Abrahamu kuti, “Usamve chisoni motero ndi mnyamatayu ndi mdzakazi wakoyu. Mvetsera chilichonse chomwe Sara akukuwuza, chifukwa zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake. 13Mwana wa mdzakazi wakoyu ndidzamusandutsa mtundu wa anthu chifukwa ndi mwana wako.”

14Mmamawa wake, Abrahamu anatenga chakudya ndi botolo la madzi nazipereka kwa Hagara. Anasenzetsa Hagara nawaperekeza pangʼono ndi mnyamatayo. Hagara ananyamuka nayendayenda mʼchipululu cha Beeriseba.

15Madzi atatha mʼbotolo muja, anamuyika mnyamatayo pansi pa zitsamba. 16Kenaka Hagara anachoka nakakhala pansi cha pakatalipo, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi, popeza mʼmaganizo mwake amati, “Sindingaonerere mwanayu akufa.” Ndipo anakhala pansi cha poteropo nʼkumalira.

17Mulungu anamva mnyamatayo akulira ndipo mngelo wa Mulungu anayankhula kwa Hagara kuchokera kumwamba nati, “Chavuta nʼchiyani Hagara? Usachite mantha; Mulungu wamva kulira kwa mnyamatayo pamene wagonapo. 18Munyamule mnyamatayo ndipo umugwire dzanja pakuti ndidzamupanga kukhala mtundu waukulu.”

19Kenaka Mulungu anatsekula maso a Hagara ndipo anaona chitsime cha madzi. Choncho anapita nadzaza botolo lija ndi madzi ndi kumupatsa mnyamatayo kuti amwe.

20Mulungu anali ndi mnyamatayo pamene ankakula. Anakhala ku chipululu nakhala katswiri wolasa uta. 21Akukhala ku chipululu cha Parani, mayi ake anamupezera mkazi wochokera ku Igupto.

Pangano la ku Beeriseba

22Pa nthawiyo, Abimeleki ndi Fikolo wamkulu wankhondo wake anati kwa Abrahamu, “Mulungu ali nawe pa chilichonse umachita. 23Tsopano undilumbirire ine pano pamaso pa Mulungu kuti sudzachita mwa chinyengo ndi ine kapena ana anga kapena zidzukulu zanga. Undionetse ine pamodzi ndi dziko limene ukukhalamo ngati mlendo, kukoma mtima kokhala ngati kumene ndinakuonetsa ine.”

24Abrahamu anati, “Ine ndikulumbira.”

25Kenaka Abrahamu anadandaula kwa Abimeleki pa za chitsime chimene antchito a Abimeleki analanda. 26Koma Abimeleki anati, “Ine sindikudziwa amene anachita zimenezi. Iwe sunandiwuze, ndipo ndazimva lero zimenezi.”

27Choncho Abrahamu anabweretsa nkhosa ndi ngʼombe nazipereka kwa Abimeleki, ndipo anthu awiriwo anachita pangano. 28Abrahamu anapatulako ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri kuchoka pagulu la nkhosa zina, 29ndipo Abimeleki anafunsa Abrahamu, “Kodi tanthauzo lake la ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri amene wawapatula pawokhawa nʼchiyani?”

30Iye anayankha kuti, “Landirani ana ankhosa aakazi kuchokera mʼdzanja langa ngati umboni kuti ndinakumba chitsime ichi.”

31Kotero malo amenewo anatchedwa Beeriseba, chifukwa anthu awiriwo analumbirirapo malumbiro.

32Atatha kuchita pangano pa Beeriseba, Abimeleki ndi Fikolo mkulu wankhondo wake anabwerera ku dziko la Afilisti. 33Abrahamu anadzala mtengo wa bwemba ku Beeriseba, ndipo anapemphera pamenepo mʼdzina la Yehova, Mulungu Wamuyaya. 34Ndipo Abrahamu anakhala mʼdziko la Afilisti kwa nthawi yayitali.

Persian Contemporary Bible

پيدايش 21:1‏-34

تولد اسحاق

1‏-2خداوند به وعدهٔ خود وفا كرد و ساره در زمانی كه خداوند مقرر فرموده بود، حامله شد و برای ابراهيم در سن پيری پسری زاييد. 3ابراهيم پسرش را اِسحاق (يعنی «خنده») نام نهاد. 4‏-5او طبق فرمان خدا اسحاق را هشت روز بعد از تولدش ختنه كرد. هنگام تولدِ اسحاق، ابراهيم صد ساله بود.

6ساره گفت: «خدا برايم خنده و شادی آورده است. هر كس خبر تولد پسرم را بشنود با من شادی خواهد كرد. 7چه كسی باور می‌كرد كه روزی من بچهٔ ابراهيم را شير بدهم؟ ولی اكنون برای ابراهيم در سن پيری او پسری زاييده‌ام!»

8اسحاق بزرگ شده، از شير گرفته شد و ابراهيم به اين مناسبت جشن بزرگی بر پا كرد.

هاجر و اسماعيل از خانه رانده می‌شوند

9يک روز ساره متوجه شد كه اسماعيل، پسر هاجر مصری، اسحاق را اذيت می‌كند. 10پس به ابراهيم گفت: «اين كنيز و پسرش را از خانه بيرون كن، زيرا اسماعيل با پسر من اسحاق وارث تو نخواهد بود.» 11اين موضوع ابراهيم را بسيار رنجاند، چون اسماعيل نيز پسر او بود.

12اما خدا به ابراهيم فرمود: «دربارهٔ پسر و كنيزت آزرده خاطر مباش. آنچه ساره گفته است انجام بده، زيرا توسط اسحاق است كه تو صاحب نسلی می‌شوی كه وعده‌اش را به تو داده‌ام. 13از پسر آن كنيز هم قومی به وجود خواهم آورد، چون او نيز پسر توست.»

14پس ابراهيم صبح زود برخاست و نان و مشكی پُر از آب برداشت و بر دوش هاجر گذاشت، و او را با پسر روانه ساخت. هاجر به بيابان بئرشِبَع رفت و در آنجا سرگردان شد. 15وقتی آب مشک تمام شد، هاجر پسرش را زير بوته‌ها گذاشت 16و خود حدود صد متر دورتر از او نشست و با خود گفت: «نمی‌خواهم ناظر مرگ فرزندم باشم.» و زارزار بگريست.

17آنگاه خدا به ناله‌های پسر توجه نمود و فرشتهٔ خدا از آسمان هاجر را ندا داده، گفت: «ای هاجر، چه شده است؟ نترس! زيرا خدا ناله‌های پسرت را شنيده است. 18برو و او را بردار و در آغوش بگير. من قوم بزرگی از او به وجود خواهم آورد.» 19سپس خدا چشمان هاجر را گشود و او چاه آبی در مقابل خود ديد. پس به طرف چاه رفته، مشک را پر از آب كرد و به پسرش نوشانيد. 20‏-21و خدا با اسماعيل بود و او در بيابانِ فاران بزرگ شده، در تيراندازی ماهر گشت و مادرش دختری از مصر برای او گرفت.

عهد بين ابراهيم و ابيملک

22در آن زمان ابيملکِ پادشاه، با فرماندهٔ سپاهش فيكول نزد ابراهيم آمده، گفت: «خدا در آنچه می‌كنی با توست! 23اكنون به نام خدا سوگند ياد كن كه به من و فرزندان و نواده‌های من خيانت نكنی و همانطوری كه من با تو به خوبی رفتار كرده‌ام، تو نيز با من و مملكتم كه در آن ساكنی، به خوبی رفتار نمايی.»

24ابراهيم پاسخ داد: «سوگند می‌خورم چنانكه گفتيد رفتار كنم.»

25سپس ابراهيم دربارهٔ چاهِ آبی كه خدمتگزاران ابيملک به زور از او گرفته بودند، نزد وی شكايت كرد. 26ابيملکِ پادشاه گفت: «اين اولين باری است كه راجع به اين موضوع می‌شنوم و نمی‌دانم كدام يک از خدمتگزارانم در اين كار مقصر است. چرا پيش از اين به من خبر ندادی؟»

27آنگاه ابراهيم، گوسفندان و گاوانی به ابيملک داد و با يكديگر عهد بستند. 28سپس ابراهيم هفت بره از گله جدا ساخت. 29پادشاه پرسيد: «چرا اين كار را می‌كنی؟»

30ابراهيم پاسخ داد: «اينها هدايايی هستند كه من به تو می‌دهم تا همه بدانند كه اين چاه از آنِ من است.»

31از آن پس اين چاه، بئرشبع (يعنی «چاه سوگند») ناميده شد، زيرا آنها در آنجا با هم عهد بسته بودند. 32آنگاه ابيملک و فيكول فرماندهٔ سپاهش به سرزمين خود فلسطين بازگشتند. 33ابراهيم در كنار آن چاه درخت گزی كاشت و خداوند، خدای ابدی را عبادت نمود. 34ابراهيم مدت زيادی در سرزمين فلسطين زندگی كرد.