Genesis 20 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 20:1-18

Abrahamu ndi Mfumu Abimeleki

1Abrahamu anachokako kumeneko napita ku Negevi ndipo anakakhala ku dziko la Gerari, limene lili pakati pa mzinda wa Kadesi ndi mzinda wa Suri. Anakhala ku Gerari kwa kanthawi, 2ndipo Abrahamu ankawawuza za Sara kuti, “Iyeyu ndi mlongo wanga.” Choncho Abimeleki, mfumu wa ku Gerari anamutenga Sara uja.

3Koma usiku, Mulungu anafika kwa Abimeleki kutulo nati, “Ufatu iwe chifukwa cha mkazi amene watengayu popeza ndi wokwatiwa.”

4Nthawi imeneyi nʼkuti Abimeleki asanamukhudze mkaziyo, kotero kuti anati, “Ambuye, kodi mudzawonongadi mtundu wolungama? 5Kodi Abrahamu sanandiwuze kuti iyeyu ndi mlongo wake? Ndiponso mkaziyu ankanena kuti Abrahamu ndi mlongo wake. Choncho ine pochita izi, ndinkachita moona mtima ndiponso mopanda chinyengo.”

6Tsono kumaloto komweko Mulungu anati kwa iye, “Inde ndikudziwa kuti wachita izi moona mtima, ndipo Ine sindinafune kuti undichimwire. Nʼchifukwa chake sindinakulole kuti umukhudze. 7Tsopano kabwezere mkaziyo kwa mwamuna wake. Iyeyu ndi mneneri, ndipo adzakupempherera kuti ukhale ndi moyo. Koma ukapanda kukamupereka, udziwiretu kuti udzafa pamodzi ndi onse a pa banja pako.”

8Mmamawa mwake Abimeleki anayitanitsa akuluakulu ake onse, ndipo atawafotokozera zimene zinachitika, iwo aja anachita mantha kwambiri. 9Kenaka Abimeleki anayitana Abrahamu ndipo anati, “Kodi wachita chiyani? Ndakulakwira chiyani kuti undibweretsere ine pamodzi ndi anthu anga chilango chachikulu chotere? Wandichitira zinthu zimene sizinayenera kuchitika.” 10Ndipo Abrahamu anafunsa Abimeleki kuti, “Chifukwa chiyani wachita zimenezi?”

11Abrahamu anayankha nati, “Ndinkaganiza kuti kuno kulibiretu munthu woopa Mulungu. Ndiye ndimati mwina adzandipha chifukwa cha mkazi wanga. 12Komabe kunena zoona, iyeyu ndi mlongo wangadi, mwana wamkazi wa abambo anga ngakhale kuti si ife a mayi mmodzi. Tsono akhoza kukhala mkazi wanga. 13Ndiye pamene Mulungu anati ndichoke ku nyumba ya abambo anga, ndinawuza mkazi wangayu kuti, ‘Kuti uwonetse kuti ndiwe mkazi wokoma mtima, uziwuza anthu kulikonse kumene tingapite kuti ndine mlongo wako.’ ”

14Tsono Abimeleki anapereka nkhosa, ngʼombe ndi antchito aamuna ndi aakazi kwa Abrahamu. Ndipo anamubwezeranso Abrahamu Sara, mkazi wake. 15Tsono Abimeleki anati kwa Abrahamu, “Dziko langa ndi limene ukulionali; ukhale paliponse pamene ufuna.”

16Ndipo kwa Sara, iye anati, “Ndikumupatsa mlongo wakoyu makilogalamu khumi ndi awiri a siliva kutsimikiza kuti iwe ndi wosalakwa pamaso pa onse amene ali ndi iwe; ulibedi mlandu.”

17Tsono Abrahamu anapemphera kwa Mulungu ndipo Mulunguyo anachiritsa Abimeleki, mkazi wake pamodzi ndi adzakazi ake kuti athenso kubereka ana. 18Paja Yehova nʼkuti atatseka akazi onse a mʼbanja la Abimeleki kuti asabereke ana chifukwa cha Sara, mkazi wa Abrahamu.

Persian Contemporary Bible

پيدايش 20:1‏-18

ابراهيم و ابيملک

1‏-2آنگاه ابراهيم به سوی سرزمين نِگِب كوچ كرد و در بين قادش و شور ساكن شد. وقتی او در شهر جرار بود، ساره را خواهر خود معرفی كرد. پس ابيملک، پادشاه جرار، كسانی فرستاد تا ساره را به قصر وی ببرند.

3اما همان شب خدا در خواب بر ابيملک ظاهر شده، گفت: «تو خواهی مُرد، زيرا زن شوهرداری را گرفته‌ای.»

4ابيملک هنوز با او همبستر نشده بود، پس عرض كرد: «خداوندا، من بی‌تقصيرم. آيا تو مرا و قومم را خواهی كشت؟ 5خودِ ابراهيم به من گفت كه او خواهرش است و ساره هم سخن او را تصديق كرد و گفت كه او برادرش می‌باشد. من هيچگونه قصد بدی نداشتم.»

6خدا گفت: «بلی، می‌دانم؛ به همين سبب بود كه تو را از گناه باز داشتم و نگذاشتم به او دست بزنی. 7اكنون اين زن را به شوهرش بازگردان. او يک نبی است و برای تو دعا خواهد كرد و تو زنده خواهی ماند. ولی اگر زن او را بازنگردانی، تو و اهل خانه‌ات خواهيد مُرد.»

8پادشاه روز بعد، صبح زود از خواب برخاسته، با عجله تمامی درباريان را به حضور طلبيد و خوابی را كه ديده بود برای آنها تعريف كرد و همگی بسيار ترسيدند.

9‏-10آنگاه پادشاه، ابراهيم را به حضور خوانده، گفت: «اين چه كاری بود كه با ما كردی؟ مگر من به تو چه كرده بودم كه مرا و مملكتم را به چنين گناه عظيمی دچار ساختی؟ هيچكس چنين كاری نمی‌كرد كه تو كردی. چرا به من بدی كردی؟»

11‏-12ابراهيم در جواب گفت: «فكر كردم مردم اين شهر ترسی از خدا ندارند و برای اين كه همسرم را تصاحب كنند، مرا خواهند كشت. علاوه بر اين، او خواهر ناتنی من نيز هست. هر دو از يک پدر هستيم و من او را به زنی گرفتم. 13هنگامی كه خداوند مرا از زادگاهم به سرزمينهای دور و بيگانه فرستاد، از ساره خواستم اين خوبی را در حق من بكند كه هر جا برويم بگويد خواهر من است.»

14پس ابيملک گوسفندان و گاوان و غلامان و كنيزان به ابراهيم بخشيد و همسرش ساره را به وی بازگردانيد، 15و به او گفت: «تمامی سرزمين مرا بگرد و هر جا را كه پسنديدی برای سكونت خود انتخاب كن.» 16سپس رو به ساره نموده، گفت: «هزار مثقال نقره به برادرت می‌دهم تا بی‌گناهی تو بر آنانی كه با تو هستند ثابت شود و مردم بدانند كه نسبت به تو به انصاف رفتار شده است.»

17آنگاه ابراهيم نزد خدا دعا كرد و خدا پادشاه و همسر و كنيزان او را شفا بخشيد تا بتوانند صاحب اولاد شوند؛ 18زيرا خداوند به اين دليل كه ابيملک، ساره زن ابراهيم را گرفته بود، همهٔ زنانش را نازا ساخته بود.