Genesis 2 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 2:1-25

1Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.

2Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse. 3Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.

Adamu ndi Hava

4Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi:

Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba, 5zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka, 6koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse. 7Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.

8Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja. 9Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.

10Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi. 11Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide. 12(Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi). 13Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi. 14Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.

15Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira. 16Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu; 17koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”

18Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”

19Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake. 20Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse.

Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza. 21Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu. 22Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.

23Munthu uja anati,

“Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga

ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga;

adzatchedwa ‘mkazi,’

popeza wachokera mwa mwamuna.”

24Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.

25Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

創世記 2:1-25

1天地萬物都造好了。 2第七天,上帝完成了祂的創造之工,就在第七天歇了一切的工。 3上帝賜福給第七天,將其定為聖日,因為祂在這一天歇了祂一切的創造之工。 4這是有關創造天地的記載。

上帝造亞當和夏娃

耶和華上帝創造天地的時候, 5地上還沒有草木菜蔬,因為耶和華上帝還沒有降雨在地上,土地也沒有人耕作, 6但有水從地裡湧出,澆灌大地。 7耶和華上帝用地上的塵土造了人,把生命的氣息吹進他的鼻孔裡,他就成了有生命的人。 8耶和華上帝在東方的伊甸開闢了一個園子,把祂所造的人安置在裡面。 9耶和華上帝使地面長出各種樹木,它們既好看又能結出可吃的果子。在園子的中間有生命樹和分別善惡的樹。

10有一條河從伊甸流出來灌溉那園子,又從那裡分出四條支流。 11第一條支流叫比遜河,它環繞著哈腓拉全境。那裡有金子, 12且是上好的金子,還有珍珠和紅瑪瑙。 13第二條支流是基訓河,它環繞著古實全境。 14第三條支流名叫底格里斯河,它流經亞述的東邊。第四條支流是幼發拉底河。

15耶和華上帝把那人安置在伊甸的園子裡,讓他在那裡耕種、看管園子。 16耶和華上帝吩咐那人說:「你可以隨意吃園中所有樹上的果子, 17只是不可吃那棵分別善惡樹的果子,因為你若吃了,當天必死。」

18耶和華上帝說:「那人獨自一人不好,我要為他造一個相配的幫手。」 19耶和華上帝用塵土造了各種田野的走獸和空中的飛鳥,把牠們帶到那人跟前,看他怎麼稱呼這些動物。他叫這些動物什麼,牠們的名字就是什麼。 20那人給所有的牲畜及田野的走獸和空中的飛鳥都起了名字。可是他找不到一個跟自己相配的幫手。 21耶和華上帝使那人沉睡,然後從他身上取出一根肋骨,再把肉合起來。 22耶和華上帝用那根肋骨造成一個女人,帶到那人跟前。 23那人說:

「這才是我的同類,

我骨中的骨,肉中的肉,

要稱她為女人,

因為她是從男人身上取出來的。」

24因此,人要離開父母,與妻子結合,二人成為一體。 25當時,他們夫婦二人都赤身露體,並不覺得羞恥。