Genesis 18 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 18:1-33

Alendo Atatu a Abrahamu

1Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha. 2Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati, 3“Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu. 4Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu. 5Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.”

Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”

6Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”

7Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo. 8Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.

9Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?”

Iye anati, “Ali mu tentimu.”

10Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.”

Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi. 11Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka. 12Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”

13Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’ 14Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”

15Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.”

Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”

Abrahamu Apembedzera Sodomu

16Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza. 17Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa? 18Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye. 19Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”

20Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri 21choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”

22Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova. 23Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa? 24Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo? 25Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”

26Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”

27Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe, 28bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?”

Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”

29Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?”

Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”

30Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?”

Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”

31Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?”

Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”

32Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?”

Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”

33Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.

New Russian Translation

Бытие 18:1-33

Три гостя Авраама

1Господь явился Аврааму у дубравы Мамре, когда он сидел у входа в свой шатер во время дневного зноя. 2Авраам поднял взгляд и увидел, что неподалеку стоят три человека. Увидев их, он побежал от входа в шатер им навстречу и поклонился до земли.

3Он сказал:

– Если я нашел милость в Твоих глазах, Владыка18:3 Евр.: «Адонай»., не пройди мимо Твоего слуги. 4Пусть принесут немного воды, чтобы вам вымыть ноги и отдохнуть под этим деревом, 5а я принесу вам что-нибудь поесть. Вы подкрепитесь и продолжите свой путь – раз уж вы пришли к вашему слуге.

– Очень хорошо, – ответили они. – Делай, как говоришь.

6Авраам поспешил в шатер к Сарре и сказал:

– Скорее, достань три саты18:6 Три саты что равняется 22 литрам (примерно 14 кг муки). лучшей муки, замеси тесто и испеки хлеба.

7Затем он побежал к стаду, выбрал лучшего, нежного теленка и отдал слуге, который быстро приготовил его. 8Потом он принес творога, молока и приготовленного теленка и поставил перед ними. Пока они ели, он стоял рядом с ними под деревом.

9– Где твоя жена Сарра? – спросили они.

– Там, в шатре, – ответил он.

10Тогда Господь18:10 Букв.: «Он». сказал:

– Я непременно вернусь к тебе в следующем году, примерно в это же время, и у Сарры, твоей жены, будет сын.

Сарра слушала, стоя у Него за спиной, у входа в шатер. 11Авраам и Сарра были уже стары и в преклонных годах, и то, что обычно бывает у женщин, у Сарры прекратилось. 12Поэтому Сарра рассмеялась про себя, подумав: «Я уже состарилась, и господин мой стар; мне ли иметь еще такую радость?»18:12 Или: «наслаждение».

13Тогда Господь сказал Аврааму:

– Почему Сарра смеется и говорит: «Неужели у меня в самом деле будет ребенок, ведь я стара?» 14Есть ли что-нибудь слишком трудное для Господа? Я вернусь к тебе через год в назначенное время, и у Сарры будет сын.

15Сарра испугалась и солгала, сказав:

– Я не смеялась.

Но Он сказал:

– Нет, ты смеялась.

Просьба Авраама о сохранении города Содома

16Мужи поднялись и пошли в сторону Содома. Авраам же пошел с ними, чтобы проводить их. 17Господь сказал:

– Скрою ли Я от Авраама то, что собираюсь сделать? 18От Авраама непременно произойдет великий и сильный народ, и все народы на земле получат благословение через него. 19Ведь Я избрал его, чтобы он заповедал своим детям и всем своим потомкам хранить путь Господа, поступая правильно и справедливо, чтобы Господь исполнил то, что обещал Аврааму.

20Господь сказал:

– Вопль против Содома и Гоморры так велик, их грех так тяжек, 21что Я сойду и посмотрю, верен ли вопль, достигший Меня, так ли скверно они поступают. Если нет, Я узнаю.

22Мужи повернулись и пошли к Содому, но Господь остался стоять перед Авраамом18:22 Так по древней текстовой традиции. В нормативном еврейском тексте «но Авраам остался стоять перед Господом».. 23Авраам приблизился к Нему и сказал:

– Неужели Ты уничтожишь праведного вместе с грешным? 24Что, если в городе есть пятьдесят праведников? Неужели Ты уничтожишь и не пощадишь18:24 Или: «не простишь»; также в ст. 26. этого места ради пятидесяти праведников? 25Не можешь Ты сделать такое – погубить праведного вместе с нечестивым, обойтись с праведным и нечестивым одинаково. Не можешь Ты сделать так! Разве Судья всей земли может творить неправду?

26Господь сказал:

– Если Я найду в Содоме пятьдесят праведников, то пощажу ради них все это место.

27Тогда Авраам сказал вновь:

– Вот, я осмелился говорить с Владыкой, хотя я лишь прах и пепел; 28что, если число праведных на пять меньше пятидесяти? Уничтожишь ли Ты весь город из-за пяти человек?

– Если Я найду там сорок пять, – ответил Он, – то не уничтожу его.

29Авраам обратился к Нему еще раз:

– Что, если там найдутся лишь сорок?

Он ответил:

– Ради сорока Я не сделаю этого.

30Тогда тот сказал:

– Да не разгневается Владыка, но позволит мне сказать. Что, если найдутся там только тридцать?

Он ответил:

– Я не сделаю этого, если найду там тридцать.

31Авраам сказал:

– Вот, я был так смел, что решился говорить Владыке. Что, если найдутся там лишь двадцать?

Он сказал:

– Ради двадцати Я не уничтожу его.

32Тогда Авраам сказал:

– Да не разгневается Владыка, но позволит мне сказать еще лишь один раз. Что, если найдутся там лишь десять?

Он ответил:

– Ради десяти Я не уничтожу его.

33Когда Господь закончил говорить с Авраамом, Он ушел, а Авраам вернулся домой.