Genesis 18 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 18:1-33

Alendo Atatu a Abrahamu

1Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha. 2Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati, 3“Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu. 4Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu. 5Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.”

Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”

6Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”

7Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo. 8Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.

9Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?”

Iye anati, “Ali mu tentimu.”

10Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.”

Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi. 11Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka. 12Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”

13Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’ 14Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”

15Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.”

Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”

Abrahamu Apembedzera Sodomu

16Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza. 17Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa? 18Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye. 19Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”

20Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri 21choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”

22Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova. 23Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa? 24Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo? 25Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”

26Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”

27Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe, 28bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?”

Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”

29Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?”

Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”

30Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?”

Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”

31Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?”

Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”

32Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?”

Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”

33Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Mwanzo 18:1-33

Wageni Watatu

118:1 Mwa 12:7; 13:18; 14:13; 19:1; 23:10, 18; 34:20-24; Rut 4:1; Ebr 11:9; Za 69:12Bwana akamtokea Abrahamu karibu na mialoni ya Mamre wakati alipokuwa ameketi kwenye ingilio la hema lake wakati wa adhuhuri. 218:2 Mwa 17:2-3; 19:1, 10; 24:63; 32:24; 43:28; Yos 5:13; Ebr 13:2; Amu 13:6-11; Hos 12:2-4Abrahamu akainua macho akaona watu watatu wamesimama karibu naye. Alipowaona, aliharakisha kutoka kwenye ingilio la hema lake kuwalaki na kuwasujudia hadi nchi.

3Akasema, “Kama nimepata kibali machoni penu, ee bwana wangu, usimpite mtumishi wako. 418:4 Mwa 19:2; 24:32; 43:24; Amu 19:21; 2Sam 11:8; Lk 7:44Acha yaletwe maji kidogo, kisha ninyi nyote mnawe miguu yenu na mpumzike chini ya mti huu. 518:5 Amu 13:15; 19:5Niruhusuni niwapatie chakula kidogo mle, ili mpate nguvu mwendelee na safari yenu, kwa kuwa mmekuja kwa mtumishi wenu.”

Nao wakamjibu, “Vema sana, fanya kama unavyosema.”

618:6 Mwa 19:3; 2Sam 13:8Hivyo Abrahamu akaharakisha akaingia hemani kwa Sara, akamwambia, “Chukua vipimo vitatu vya unga laini haraka, ukande na uoke mikate.”

718:7 1Sam 28:24; Lk 15:23Kisha Abrahamu akakimbia kwenda kwenye kundi, akachagua ndama mzuri, laini na akampa mtumishi, ambaye aliharakisha kumtayarisha. 818:8 Isa 7:15, 22; Amu 4:19; 5:25; 6:19Kisha akaleta jibini, maziwa na nyama ya yule ndama iliyoandaliwa, akaviweka mbele ya wageni. Walipokuwa wakila, alisimama karibu nao chini ya mti.

918:9 Mwa 3:9; 24:67; Ebr 11:9Wakamuuliza, “Yuko wapi Sara mkeo?”

Akasema, “Yuko huko, ndani ya hema.”

1018:10 Mwa 17:6, 21; 21:2; 2Fal 4:16; Rum 6:6Kisha Bwana akasema, “Hakika nitakurudia tena majira kama haya mwakani na Sara mkeo atakuwa ana mwana.”

Sara alikuwa akiwasikiliza kwenye ingilio la hema, lililokuwa nyuma yake. 1118:11 Mwa 11:30; 17:17; Lk 1:18; Rum 4:19; Ebr 11:11-12Abrahamu na Sara walikuwa wazee tena waliosogea miaka, naye Sara alikuwa amekoma katika desturi ya wanawake. 1218:12 Mwa 17:17; 21:6; 1Pet 3:6Hivyo Sara akacheka kimoyomoyo alipokuwa akiwaza, “Baada ya mimi kuwa mkongwe hivi na bwana wangu amezeeka, je, nitaweza kufurahia jambo hili?”

1318:13 Mwa 17:17Ndipo Bwana akamwambia Abrahamu, “Kwa nini Sara amecheka na kusema, ‘Kweli nitazaa mtoto nami sasa ni mzee?’ 1418:14 Ay 42:2; Isa 40:29; 50:2; 51:9; Gal 4:23; Yer 32:17; Mt 19:26; Rum 4:21; 9:9; Mwa 17:19Je, kuna jambo lolote gumu lisilowezekana kwa Bwana? Nitakurudia mwakani majira kama haya, naye Sara atakuwa na mwana.”

15Sara akaogopa kwa kuwa alidanganya na kusema, “Mimi sikucheka.”

Lakini Bwana akasema, “Ndiyo, ulicheka!”

Abrahamu Aiombea Sodoma

16Wakati watu hao waliposimama ili waondoke, walielekeza nyuso zao Sodoma, Abrahamu akawatoa kitambo kidogo ili awasindikize. 1718:17 Amo 3:7; Mwa 19:24; Ay 1:16; Za 107:34Ndipo Bwana akasema, “Je, nimfiche Abrahamu jambo ninalokusudia kufanya? 1818:18 Mwa 12:2; Gal 3:8Hakika Abrahamu atakuwa taifa kubwa na lenye nguvu, kupitia kwake mataifa yote ya dunia yatabarikiwa. 1918:19 Mwa 16:11; 17:9; 22:12, 18; 26:5; Kum 4:9-10; 6:7; Isa 14:1; Efe 6:4; Yos 24:15; Yer 23:5; 2Sam 8:15; Za 17:2; 99:4Kwa maana nimemchagua yeye, ili awaongoze watoto wake na jamaa yake kufuata njia ya Bwana, kwa kuwa waadilifu na kutenda haki, ili Bwana atimize ahadi yake kwa Abrahamu.”

2018:20 Isa 1:10; Yer 23:14; Eze 16:46; Mwa 13:13; 19:13Basi Bwana akasema, “Kilio dhidi ya Sodoma na Gomora ni kikubwa sana na dhambi yao inasikitisha sana, 2118:21 Mwa 11:5kwamba nitashuka nione kama waliyoyatenda ni mabaya kiasi cha kilio kilichonifikia. Kama sivyo, nitajua.”

2218:22 Mwa 19:1, 27Basi wale watu wakageuka wakaenda kuelekea Sodoma, lakini Abrahamu akabaki amesimama mbele za Bwana. 2318:23 Kut 23:7; 2Pet 2:9; Law 4:3, 22, 27; Hes 16:22; Eze 18:4; Kum 27:25; 2Sam 24:17; Za 11:4-7; 94:21Ndipo Abrahamu akamsogelea akasema: “Je, utawaangamiza wenye haki na waovu? 2418:24 Yer 5:1Je, ikiwa watakuwepo watu wenye haki hamsini katika mji huo, hivi kweli utauangamiza na wala hutauacha kwa ajili ya hao watu hamsini wenye haki waliomo ndani yake? 2518:25 Mwa 20:4; 44:7; Kum 32:4; 1:16-17; Rum 3:6; Ay 8:3-7; 9:15; 34:10; 36:23; Isa 3:10-11; 5:20; Amo 5:15; Mal 2:17; 3:18; Amu 11:27; Za 7:11; 58:11; 75:7; 94:2; 119:137; Ebr 12:23; 2Nya 19:7; Ezr 9:15; Neh 9:33; Eze 18:25; Dan 4:37; 9:14Hilo na liwe mbali nawe, kufanya jambo kama hilo, kuwaua wenye haki pamoja na waovu, kuwatendea wenye haki sawasawa na waovu. Iwe mbali nawe! Je, Mwamuzi wa dunia yote hatafanya lililo sawa?”

26Bwana akasema, “Kama nikipata watu hamsini wenye haki katika mji wa Sodoma, nitausamehe huo mji wote kwa ajili yao.”

2718:27 Mwa 2:7; Ay 2:8Kisha Abrahamu akasema tena: “Sasa kwa kuwa nimekuwa na ujasiri wa kuzungumza na Bwana, ingawa mimi si kitu bali ni mavumbi na majivu; 28je, kama hesabu ya wenye haki imepungua watano katika hamsini, utauangamiza huo mji wote kwa ajili ya hao watano waliopungua?”

Bwana akamwambia, “Kama nikiwakuta huko watu arobaini na watano, sitauangamiza.”

29Abrahamu akazungumza naye kwa mara nyingine, “Je, kama huko watapatikana watu arobaini tu?”

Akamjibu, “Kwa ajili ya hao arobaini, sitauangamiza.”

3018:30 Mwa 44:18; Kut 32:22Ndipo akasema, “Bwana na asikasirike, lakini niruhusu nizungumze. Je, kama huko watakuwepo thelathini tu?”

Akajibu, “Sitapaangamiza ikiwa nitawakuta huko watu thelathini.”

31Abrahamu akasema, “Sasa kwa kuwa nimekuwa na ujasiri sana kuzungumza na Bwana, je, kama wakipatikana huko watu ishirini tu?”

Bwana akajibu, “Kwa ajili ya hao ishirini, sitauangamiza.”

3218:32 Amu 6:39; Yer 5:1Abrahamu akasema, “Bwana na asikasirike, lakini niruhusu nizungumze tena mara moja tu. Itakuwaje kama watapatikana huko watu kumi tu?”

Bwana akajibu, “Kwa ajili ya hao kumi, sitauangamiza.”

3318:33 Kut 31:18; Mwa 17:22; 31:55Bwana alipomaliza kuzungumza na Abrahamu, akaondoka, naye Abrahamu akarudi nyumbani kwake.