Genesis 16 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 16:1-16

Sarai ndi Hagara

1Tsono Sarai, mkazi wa Abramu anali asanamuberekere ana Abramuyo. Koma anali ndi wantchito wamkazi wa ku Igupto dzina lake Hagara; 2ndipo Sarai anati kwa Abramu, “Yehova sanalole kuti ine ndikhale ndi ana. Bwanji mulowe mwa wantchito wanga wamkaziyu kuti mwina ndingaone ana kudzera mwa iyeyu.”

Abramu anamvera Sarai. 3Tsono Sarai anatenga Hagara wantchito wake wamkazi wa ku Igupto uja namupereka kwa Abramu mwamuna wake kuti akhale mkazi wake. Izi zinachitika Abramu atakhala ku Kanaani zaka khumi. 4Abramu atalowana ndi Hagara, Hagara uja anatenga mimba.

Pamene Hagara anadziwa kuti anali woyembekezera anayamba kunyoza mbuye wake Sarai. 5Pamenepo Sarai anati kwa Abramu, “Inu ndinu amene mwandiputira nkhanza zikundichitikirazi. Ndinakupatsani wantchito wanga wamkazi kuti akhale mkazi wanu, ndiye tsopano wayamba kundinyoza ine chifukwa wadziwa kuti ndi woyembekezera. Yehova ndiye amene aweruze pakati pa inu ndi ine.”

6Abramu anati, “Wantchito wakoyu ali mʼmanja mwako. Chita naye chilichonse chimene ukuganiza kuti ndi chokukomera.” Tsono Sarai anazunza Hagara mpaka anathawa.

7Mngelo wa Yehova anamupeza Hagara pafupi ndi chitsime mʼchipululu. Chinali chitsime chimene chili mʼmphepete mwa msewu wopita ku Suri. 8Ndipo mngeloyo anati, “Hagara, iwe wantchito wa Sarai, ukuchokera kuti ndipo ukupita kuti?”

Iye anayankha, “Ndikuthawa mbuye wanga Sarai.”

9Mngelo wa Yehova anamuwuza kuti, “Bwerera kwa mbuye wako ndipo ukamugonjere. 10Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri zoti munthu sangaziwerenge.”

11Mngelo wa Yehova uja anamuwuzanso kuti,

“Ndiwe woyembekezera

ndipo udzabala mwana wamwamuna.

Udzamutcha dzina lake Ismaeli,

pakuti Yehova wamva kulira chifukwa cha kuzunzika kwako.

12Iye adzakhala munthu wa khalidwe ngati mʼmbulu wamisala;

adzadana ndi aliyense

ndipo anthu onse adzadana naye,

adzakhala mwaudani pakati pa abale ake

onse.”

13Hagara anatcha Yehova amene anamuyankhula uja dzina loti: “Ndinu Mulungu amene mumandiona,” popeza anati, “Ndakumana ndi Yehova atatha kundikomera mtima.” 14Nʼchifukwa chake chitsime chija chimene chili pakati pa Kadesi ndi Beredi chinatchedwa Beeri-lahai-roi.

15Tsono Hagara anamuberekera Abramu mwana wamwamuna ndipo Abramu anamutcha mwanayo Ismaeli. 16Pamene Hagara anamubalira Ismaeli nʼkuti Abramuyo ali ndi zaka 86.

Luganda Contemporary Bible

Olubereberye 16:1-16

Ibulaamu ne Agali

116:1 a Lub 11:30; Bag 4:24-25 b Lub 21:9Salaayi mukyala wa Ibulaamu yali teyamuzaalira mwana; 216:2 Lub 30:3-4, 9-10Salaayi n’agamba Ibulaamu nti, “Laba Mukama tampadde mwana; weebake n’omuweereza wange, oboolyawo nnyinza okufuna abaana mu ye.”

Awo Ibulaamu n’awulira eddoboozi lya Salaayi.16:2 Obugumba kyatwalibwanga okuba ekibonerezo okuva eri Katonda. Era empisa mu biro ebyo yakkirizanga omukazi omugumba okulondera bba omuwala, bba gw’ayinza okuzaalako abaana. Abaana abo baabanga ba mukazi omugumba. 316:3 Lub 12:5Bw’atyo Ibulaamu bwe yali yaakamala emyaka kkumi mu nsi ya Kanani, Salaayi mukazi we n’addira Agali Omumisiri, omuweereza we n’amuwa Ibulaamu abeere mukazi we. 4Ibulaamu ne yeegatta ne Agali, Agali n’aba olubuto.

Agali bwe yalaba ng’ali lubuto, n’anyooma Salaayi, mugole we. 516:5 Lub 31:53Salaayi n’agamba Ibulaamu nti, “Ekibi ekinkoleddwako kibeere ku ggwe. Nakuwa omuweereza wange mu kifuba kyo naye bw’alabye ng’ali lubuto n’annyooma. Mukama atulamule nze naawe!” 6Naye Ibulaamu n’agamba Salaayi nti, “Laba, omuweereza wo ali mu buyinza bwo; mukole nga bw’oyagala.” Awo Salaayi natandika okubonyaabonya Agali; Agali n’adduka okuva w’ali.

Agali ne Isimayiri

716:7 a Lub 21:17; 22:11, 15; 31:11 b Lub 20:1Malayika wa Mukama n’amusanga ku nsulo y’amazzi mu ddungu, ensulo y’amazzi eri ku kkubo eriraga e Ssuuli. 8N’agamba nti, “Agali, omuweereza wa Salaayi, ovudde wa era ogenda wa?” N’amuddamu nti, “Nziruka mugole wange Salaayi.”

9Malayika wa Mukama n’amugamba nti, “Ddayo eri mugole wo omugondere.” 1016:10 Lub 13:16; 17:20Era Malayika wa Mukama n’amugamba nti, “Ezadde lyo ndiryaza waleme kubeerawo asobola kulibala.”

1116:11 Kuv 2:24; 3:7, 9Ate malayika wa Mukama n’amugamba nti,

“Laba, olina omwana mu nda yo,

aliba wabulenzi,

olimutuuma Isimayiri,

kubanga Mukama ategedde okubonaabona kwo.

1216:12 Lub 25:18Aliba ng’entulege,

anaalwananga na buli muntu

era na buli muntu anaalwananga naye,

era anaabanga mu bulabe

ne baganda be.”

1316:13 Lub 32:30Awo n’akoowoola erinnya lya Mukama eyayogera naye, n’agamba nti, “Oli Katonda alaba”, kubanga yagamba nti, “Ndabidde ddala Katonda ne nsigala nga ndi mulamu nga maze okumulaba.” 14Oluzzi kye lwava luyitibwa Beerirakayiro, luli wakati wa Kadesi ne Beredi.

1516:15 Bag 4:22Awo Agali n’azaalira Ibulaamu omwana owoobulenzi, Ibulaamu n’atuuma mutabani wa Agali gwe yamuzaalira, erinnya Isimayiri. 16Ibulaamu yali wa myaka kinaana mu mukaaga Agali bwe yamuzaalira Isimayiri.