Genesis 15 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 15:1-21

Pangano la Mulungu ndi Abramu

1Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati:

“Usaope Abramu.

Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza.

Mphotho yako idzakhala yayikulu.”

2Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko? 3Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”

4Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.” 5Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”

6Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.

7Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”

8Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”

9Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”

10Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati. 11Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.

12Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba. 13Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400. 14Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri. 15Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino. 16Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”

17Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija. 18Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate. 19Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni, 20Ahiti, Aperezi, Arefaimu, 21Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

創世記 15:1-21

上帝與亞伯蘭立約

1這些事以後,耶和華在異象中對亞伯蘭說:「亞伯蘭,你不用害怕,我是你的盾牌,我要大大賞賜你。」 2亞伯蘭說:「主耶和華啊,你要賜我什麼呢?我沒有兒子,繼承我家業的人是大馬士革以利以謝。」 3亞伯蘭又說:「你沒有賜我兒子,我家中的僕人將繼承我的產業。」 4耶和華又對他說:「這人不會成為你的繼承人,你親生的兒子才是你的繼承人。」 5耶和華把亞伯蘭帶到外面,對他說:「你抬頭看看天空,數數繁星,你能數得盡嗎?你的後裔必這麼多。」 6亞伯蘭信耶和華,耶和華便算他為義人。

7耶和華又對他說:「我是耶和華,我帶你離開了迦勒底吾珥,為要把這片土地賜給你。」 8亞伯蘭說:「主耶和華啊,我怎麼知道我會得到這片土地呢?」 9耶和華說:「你要給我預備三歲的母牛、母山羊和公綿羊各一頭,斑鳩和雛鴿各一隻。」 10亞伯蘭一一照辦,把牲畜都劈成兩半,一半對著一半地擺列,但沒有劈開雀鳥。 11有鷙鳥飛到那些屍體上,亞伯蘭趕走了牠們。

12太陽下山的時候,亞伯蘭睡得很沉,忽然有可怕的黑暗籠罩著他。 13耶和華對他說:「你要清楚知道,你的後裔必流落異鄉,被奴役、虐待四百年。 14但我必懲罰奴役他們的國家,之後他們必帶著大量的財物離開那裡。 15而你必享長壽,安然離世。 16到了第四代15·16 」希伯來文可能指人一生的年日。,你的子孫必重回此地,因為亞摩利人現在還沒有惡貫滿盈。」

17太陽下山後,大地黑暗,突然有冒煙的火爐和點著的火炬在肉塊中經過。 18就在那天,耶和華跟亞伯蘭立約,說:「我必將這片土地賜給你的後代,使他們得到從埃及河到幼發拉底河一帶的土地, 19就是基尼人、基尼洗人、甲摩尼人、 20人、比利洗人、利乏音人、 21亞摩利人、迦南人、革迦撒人和耶布斯人的土地。」