Genesis 13 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 13:1-18

Abramu Asiyana ndi Loti

1Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo. 2Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.

3Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba, 4ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.

5Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti. 6Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi. 7Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.

8Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale. 9Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”

10Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora). 11Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana. 12Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu. 13Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.

14Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo. 15Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya. 16Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako. 17Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”

18Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.

La Bible du Semeur

Genèse 13:1-18

Abram se fixe au pays de Canaan

1Abram quitta donc l’Egypte avec sa femme et tout ce qu’il possédait en direction du Néguev. Loth était avec lui. 2Abram était très riche en troupeaux, en argent et en or. 3D’étape en étape, il retourna du Néguev jusqu’à Béthel, au lieu où il avait auparavant établi son campement, entre Béthel et Aï, 4c’est-à-dire à l’endroit où était l’autel qu’il avait précédemment érigé, et il y pria l’Eternel.

5Loth, qui accompagnait Abram, avait aussi des moutons, des chèvres, des bovins et des tentes, 6et le pays ne suffisait pas pour qu’ils puissent demeurer ensemble, car leurs troupeaux étaient trop nombreux, ils ne pouvaient pas rester ensemble. 7Il y eut une dispute entre les bergers d’Abram et ceux de Loth ; or les Cananéens et les Phéréziens13.7 Faisaient partie des populations primitives de ce qui deviendra le pays d’Israël. habitaient alors le pays. 8Abram dit à Loth : Nous sommes de la même famille. Qu’il n’y ait donc pas de dispute entre nous, entre mes bergers et les tiens. 9Séparons-nous plutôt. Tout le pays est à ta disposition. Si tu vas à gauche, j’irai à droite, et si tu vas à droite, j’irai à gauche.

10Loth regarda et vit toute la plaine du Jourdain qui s’étendait jusqu’à Tsoar : avant que l’Eternel eût détruit Sodome et Gomorrhe13.10 Voir chap. 18 et 19., elle était comme le jardin de l’Eternel, comme la terre d’Egypte. 11Loth choisit donc pour lui toute la plaine du Jourdain et il se dirigea vers l’est. Ainsi, ils se séparèrent l’un de l’autre. 12Abram se fixa dans le pays de Canaan, et Loth s’établit au milieu des villes de la plaine, dressant ses tentes jusqu’à Sodome. 13Or, les gens de Sodome étaient mauvais, ils commettaient beaucoup de péchés contre l’Eternel.

Abram parcourt le pays promis

14L’Eternel dit à Abram après que Loth se fut séparé de lui : Lève les yeux et regarde depuis l’endroit où tu es, vers le nord, le sud, l’est et l’ouest : 15tout le pays que tu vois, je te le donnerai, à toi et à ta descendance pour toujours. 16Je rendrai ta descendance aussi nombreuse que les grains de poussière de la terre ; si l’on peut compter les grains de poussière de la terre, alors on pourra aussi compter ta descendance. 17Lève-toi, parcours le pays en long et en large car je te le donnerai.

18Alors Abram déplaça son campement et vint se fixer près des chênes de Mamré aux environs d’Hébron13.18 L’une des plus anciennes villes du Moyen-Orient (Nb 13.22), à 35 kilomètres au sud-ouest de Jérusalem., et il bâtit là un autel à l’Eternel.