Genesis 12 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 12:1-20

Mulungu Ayitana Abramu

1Tsiku lina Yehova anamuwuza Abramu kuti, “Tuluka mʼdziko lako. Siya abale ako ndi banja la abambo ako ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.

2“Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu wa anthu

ndipo ndidzakudalitsa;

ndi kukusandutsa wotchuka kotero kuti

udzakhala dalitso kwa anthu ambiri.

3Ndidzadalitsa amene adzadalitsa iwe,

ndi kutemberera amene adzatemberera iwe;

ndipo mafuko onse a pa dziko lapansi

adzadalitsika kudzera mwa iwe.”

4Choncho Abramu ananyamuka monga momwe Yehova anamuwuzira, napita pamodzi ndi Loti. Pamene Abramu amachoka ku Harani nʼkuti ali ndi zaka 75. 5Abramu anatenga mkazi wake Sarai, Loti, mwana wamngʼono wake, pamodzi ndi chuma chawo chimene anapeza ndi antchito amene anali nawo ku Harani. Iwo ananyamuka ulendo mpaka kukafika ku dziko la Kanaani.

6Abramu anadutsa mʼdzikomo mpaka kukafika ku Sekemu pa mtengo wa thundu wa ku More. Nthawi imeneyo Akanaani analipobe mʼdzikomo. 7Yehova anadza kwa Abramu nati, “Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko limeneli.” Choncho Abramu anamangira Yehova amene anadza kwa iye, guwa lansembe.

8Atachoka pamenepo analowera cha ku mapiri a kummawa kwa Beteli namangako tenti yake pakati pa Beteli chakumadzulo ndi Ai chakummawa. Kumeneko anamangira Yehova guwa lansembe napemphera mʼdzina la Yehovayo. 9Kenaka Abramu ananyamuka kumalowera cha ku Negevi.

Abramu ku Igupto

10Kunagwa njala yayikulu mʼdzikomo, ndipo Abramu anapita ku Igupto kukakhala ngati mlendo kwa kanthawi kochepa popeza njalayo inakula kwambiri. 11Atatsala pangʼono kulowa mu Igupto, Abramu anamuwuza mkazi wake Sarai kuti, “Ndimadziwa kuti ndiwe mkazi wokongola kwambiri. 12Tsono Aigupto akakuona adzanena kuti ‘Ameneyu ndi mkazi wake.’ Tsono adzandipha ine nakusiya iwe ndi moyo. 13Tsono udzikawawuza kuti iwe ndiwe mlongo wanga. Ukatero zidzandiyendera bwino ndipo ndidzapulumuka chifukwa cha iwe.”

14Pamene Abramu anafika ku Igupto, Aigupto aja anaona kuti Sarai anali mkazi wokongoladi. 15Pamene akuluakulu a ku nyumba ya Farao anamuona, anakamuyamikira pamaso pa Farao ndipo ananka naye ku nyumba ya Farao. 16Abramu naye zinthu zinkamuyendera bwino chifukwa cha Sarai. Farao anamupatsa nkhosa, ngʼombe, abulu aamuna ndi abulu aakazi, antchito aakazi pamodzi ndi ngamira.

17Koma Yehova anabweretsa matenda owopsa pa Farao pamodzi ndi banja lake lonse chifukwa cha Sarai mkazi wa Abramu. 18Choncho Farao anayitanitsa Abramu namufunsa kuti, “Nʼchiyani wandichitirachi? Nʼchifukwa chiyani sunandiwuze kuti ameneyu ndi mkazi wako? 19Nʼchifukwa chiyani unati ndi mlongo wako, mpaka ine ndinamutenga kukhala mkazi wanga? Eko mkazi wako. Mutenge uzipita!” 20Farao analamula asilikali ake ndipo iwo anamutulutsa Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

创世记 12:1-20

上帝呼召亚伯兰

1耶和华对亚伯兰说:“你要离开家乡、亲族和父亲的家,到我要指示你的地方去。 2我必使你成为大国,我必赐福给你,使你声名远播。你必成为别人的祝福。 3我必赐福给那些祝福你的人,咒诅那些咒诅你的人。世上万族必因你而蒙福。”

4亚伯兰就照耶和华的吩咐离开哈兰,侄儿罗得与他同行。那时亚伯兰七十五岁。 5亚伯兰带着妻子撒莱、侄儿罗得以及在哈兰积攒的财物和所得的奴仆启程来到迦南。到了迦南以后, 6亚伯兰继续前行,来到示剑摩利橡树12:6 橡树”希伯来文是“大树”,也可能指灵树或圣树,下同13:1814:1318:135:435:8那里。当时迦南人住在那地方。 7耶和华向亚伯兰显现,对他说:“我要把这片土地赐给你的后裔。”亚伯兰就在那里为向他显现的耶和华筑了一座坛。 8然后,他们又启程前往伯特利东面的山区,在那里搭起帐篷。他们的西面是伯特利,东面是亚伯兰又在那里筑了一座坛,求告耶和华。 9之后,亚伯兰继续前往南地。

亚伯兰逃荒到埃及

10当时,那地方闹饥荒,灾情非常严重,亚伯兰便下到埃及暂住。 11快要到埃及的时候,他对妻子撒莱说:“我知道你是个美貌的女子, 12埃及人看见你,一定会因为你是我的妻子而杀了我,让你活着。 13所以,请你说你是我的妹妹,这样他们会因为你而善待我,留我一命。” 14亚伯兰一行到了埃及撒莱的美貌引起了埃及人的注意。 15法老的官员见了撒莱,就在法老面前称赞她的美貌,她便被带进法老的王宫。 16因为撒莱的缘故,法老厚待亚伯兰,赏给他许多牛、羊、驴、骆驼和仆婢。

17耶和华因亚伯兰妻子撒莱的缘故使法老和他全家患重病。 18法老便召见亚伯兰,说:“你做的是什么事?为什么不告诉我她是你妻子? 19为什么说她是你妹妹,以致我娶她为妻呢?现在你妻子在这里,带她走吧!” 20法老就吩咐人把亚伯兰、他妻子以及他所有的一切都送走了。