Genesis 12 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 12:1-20

Mulungu Ayitana Abramu

1Tsiku lina Yehova anamuwuza Abramu kuti, “Tuluka mʼdziko lako. Siya abale ako ndi banja la abambo ako ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.

2“Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu wa anthu

ndipo ndidzakudalitsa;

ndi kukusandutsa wotchuka kotero kuti

udzakhala dalitso kwa anthu ambiri.

3Ndidzadalitsa amene adzadalitsa iwe,

ndi kutemberera amene adzatemberera iwe;

ndipo mafuko onse a pa dziko lapansi

adzadalitsika kudzera mwa iwe.”

4Choncho Abramu ananyamuka monga momwe Yehova anamuwuzira, napita pamodzi ndi Loti. Pamene Abramu amachoka ku Harani nʼkuti ali ndi zaka 75. 5Abramu anatenga mkazi wake Sarai, Loti, mwana wamngʼono wake, pamodzi ndi chuma chawo chimene anapeza ndi antchito amene anali nawo ku Harani. Iwo ananyamuka ulendo mpaka kukafika ku dziko la Kanaani.

6Abramu anadutsa mʼdzikomo mpaka kukafika ku Sekemu pa mtengo wa thundu wa ku More. Nthawi imeneyo Akanaani analipobe mʼdzikomo. 7Yehova anadza kwa Abramu nati, “Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko limeneli.” Choncho Abramu anamangira Yehova amene anadza kwa iye, guwa lansembe.

8Atachoka pamenepo analowera cha ku mapiri a kummawa kwa Beteli namangako tenti yake pakati pa Beteli chakumadzulo ndi Ai chakummawa. Kumeneko anamangira Yehova guwa lansembe napemphera mʼdzina la Yehovayo. 9Kenaka Abramu ananyamuka kumalowera cha ku Negevi.

Abramu ku Igupto

10Kunagwa njala yayikulu mʼdzikomo, ndipo Abramu anapita ku Igupto kukakhala ngati mlendo kwa kanthawi kochepa popeza njalayo inakula kwambiri. 11Atatsala pangʼono kulowa mu Igupto, Abramu anamuwuza mkazi wake Sarai kuti, “Ndimadziwa kuti ndiwe mkazi wokongola kwambiri. 12Tsono Aigupto akakuona adzanena kuti ‘Ameneyu ndi mkazi wake.’ Tsono adzandipha ine nakusiya iwe ndi moyo. 13Tsono udzikawawuza kuti iwe ndiwe mlongo wanga. Ukatero zidzandiyendera bwino ndipo ndidzapulumuka chifukwa cha iwe.”

14Pamene Abramu anafika ku Igupto, Aigupto aja anaona kuti Sarai anali mkazi wokongoladi. 15Pamene akuluakulu a ku nyumba ya Farao anamuona, anakamuyamikira pamaso pa Farao ndipo ananka naye ku nyumba ya Farao. 16Abramu naye zinthu zinkamuyendera bwino chifukwa cha Sarai. Farao anamupatsa nkhosa, ngʼombe, abulu aamuna ndi abulu aakazi, antchito aakazi pamodzi ndi ngamira.

17Koma Yehova anabweretsa matenda owopsa pa Farao pamodzi ndi banja lake lonse chifukwa cha Sarai mkazi wa Abramu. 18Choncho Farao anayitanitsa Abramu namufunsa kuti, “Nʼchiyani wandichitirachi? Nʼchifukwa chiyani sunandiwuze kuti ameneyu ndi mkazi wako? 19Nʼchifukwa chiyani unati ndi mlongo wako, mpaka ine ndinamutenga kukhala mkazi wanga? Eko mkazi wako. Mutenge uzipita!” 20Farao analamula asilikali ake ndipo iwo anamutulutsa Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo.

La Bible du Semeur

Genèse 12:1-20

L’appel d’Abram

1L’Eternel dit à Abram : Va, quitte ton pays, ta famille et la maison de ton père pour te rendre dans le pays que je t’indiquerai12.1 Voir Ac 7.2-3 ; Hé 11.8.. 2Je ferai de toi l’ancêtre d’un grand peuple ; je te bénirai, je ferai de toi un personnage renommé et tu deviendras une source de bénédiction pour d’autres. 3Je bénirai ceux qui te béniront et je maudirai ceux qui t’outrageront12.3 Cité en Ac 3.25 ; Ga 3.8.. Toutes les familles de la terre seront bénies à travers toi12.3 Autre traduction : se béniront en citant ton exemple..

4Abram partit comme l’Eternel le lui avait demandé, et Loth s’en alla avec lui. Abram avait soixante-quinze ans quand il quitta Harân12.4 Voir Hé 11.8.. 5Il emmena Saraï, sa femme, son neveu Loth, tous les biens et les serviteurs qu’ils avaient acquis à Harân, et ils se mirent en route pour aller au pays de Canaan. Quand ils furent arrivés, 6Abram traversa le pays jusqu’à un lieu appelé Sichem, jusqu’au chêne de Moré. A cette époque-là, les Cananéens habitaient le pays.

7L’Eternel apparut à Abram et lui dit : Je donnerai ce pays à ta descendance12.7 Voir Ac 7.5 ; Ga 3.16..

Abram érigea là un autel à l’Eternel qui lui était apparu. 8Puis il leva le camp pour se rendre dans la région montagneuse à l’est de Béthel12.8 A environ 15 kilomètres au nord de Jérusalem. D’après 28.19, à l’époque, ce lieu s’appelait encore Louz. ; il établit son campement entre Béthel, à l’ouest, et Aï, à l’est. Il y érigea un autre autel à l’Eternel et lui adressa des prières. 9Ensuite Abram repartit vers le sud ; d’étape en étape, il gagna le Néguev12.9 Nom qui signifie « terre desséchée » et qui désigne le plateau stérile s’étendant au sud de Jérusalem et menant au désert..

Abram en Egypte

10Une famine survint dans le pays. Alors Abram se rendit en Egypte12.10 Moins touchée par les années sèches, grâce à l’irrigation par des canaux (voir 26.1-2 ; 41.57). pour y séjourner quelque temps, car la famine sévissait dans le pays. 11Lorsqu’il approchait de l’Egypte, il dit à Saraï sa femme : Ecoute, je sais que tu es très belle. 12Quand les Egyptiens te verront, ils se diront : « C’est sa femme. » Ils me tueront et te laisseront en vie. 13Dis-leur donc que tu es ma sœur, pour qu’on me traite bien à cause de toi. Ainsi, grâce à toi, ma vie sera épargnée.

14En effet, quand Abram arriva en Egypte, les Egyptiens remarquèrent la grande beauté de sa femme. 15Des gens de la cour du pharaon la remarquèrent et la vantèrent à leur maître, de sorte qu’elle fut enlevée et emmenée au palais royal. 16A cause d’elle, le pharaon traita Abram avec bonté. Il lui offrit des moutons, des chèvres, des bovins, des ânes, des serviteurs, des servantes, des ânesses et des chameaux. 17Mais l’Eternel infligea de grands maux au pharaon et aux gens de sa maison, à cause de Saraï, la femme d’Abram. 18Alors le pharaon convoqua Abram et lui dit : Qu’est-ce que tu m’as fait là ? Pourquoi ne m’as-tu pas dit qu’elle était ta femme ? 19Pourquoi l’as-tu présentée comme ta sœur ? A cause de cela, j’en ai fait ma femme. Maintenant, voilà ta femme ; reprends-la et va-t’en !

20Et le pharaon chargea ses gens de le reconduire avec sa femme et avec tout ce qu’il possédait.