Genesis 11 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 11:1-32

Nsanja ya Babeli

1Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi. 2Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.

3Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula. 4Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”

5Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga. 6Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita. 7Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”

8Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo. 9Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.

Mibado Kuyambira pa Semu Mpaka Abramu

10Nayi mibado yochokera kwa Semu.

Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi. 11Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

12Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela. 13Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

14Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi. 15Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

16Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi. 17Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

18Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu. 19Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

20Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi. 21Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

22Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori. 23Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

24Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera. 25Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

26Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.

Mibado Yochokera mwa Tera

27Nayi mibado yochokera mwa Tera.

Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti. 28Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira. 29Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani. 30Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.

31Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.

32Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.

Persian Contemporary Bible

پيدايش 11:1-32

برج بابل

1در آن روزگار همهٔ مردم جهان به يک زبان سخن می‌گفتند. 2جمعيت دنيا رفته‌رفته زياد می‌شد و مردم به طرف شرق كوچ می‌كردند. آنها سرانجام به دشتی وسيع و پهناور در بابل رسيدند و در آنجا سكنی گزيدند. 3‏-4مردمی كه در آنجا می‌زيستند با هم مشورت كرده، گفتند: «بياييد شهری بزرگ بنا كنيم و برجی بلند در آن بسازيم كه سرش به آسمان برسد تا نامی برای خود پيدا كنيم. بنای اين شهر و برج مانع پراكندگی ما خواهد شد.» برای بنای شهر و برج آن خشتهای پخته تهيه نمودند. از اين خشتها به جای سنگ و از قير به جای گچ استفاده كردند. 5‏-6اما هنگامی كه خداوند به شهر و برجی كه در حال بنا شدن بود نظر انداخت، گفت: «زبان همهٔ مردم يكی است و متحد شده، اين كار را شروع كرده‌اند. اگر اكنون از كار آنها جلوگيری نكنيم، در آينده هر كاری بخواهند انجام خواهند داد. 7پس زبان آنها را تغيير خواهيم داد تا سخن يكديگر را نفهمند.» 8اين اختلافِ زبان موجب شد كه آنها از بنای شهر دست بردارند؛ و به اين ترتيب خداوند ايشان را روی زمين پراكنده ساخت. 9از اين سبب آنجا را بابل (يعنی «اختلاف») ناميدند، چون در آنجا بود كه خداوند در زبان آنها اختلاف ايجاد كرد و ايشان را روی زمين پراكنده ساخت.

از سام تا ابرام

(اول تواريخ 1‏:24‏-27)

10‏-11اين است نسل سام: دو سال بعد از طوفان، وقتی سام ۱۰۰ ساله بود، پسرش11‏:10‏و11 «پسر» می‌تواند به معنی «نوه» يا «نبيره» نيز باشد؛ همچنين در آيات 12‏-25‏.‏ ارفكشاد به دنيا آمد. پس از آن سام ۵۰۰ سال ديگر زندگی كرد و صاحب پسران و دختران شد.

12‏-13وقتی ارفكشاد سی و پنج ساله بود، پسرش شالح متولد شد و پس از آن، ارفكشاد ۴۰۳ سال ديگر زندگی كرد و صاحب پسران و دختران شد.

14‏-15وقتی شالح سی ساله بود، پسرش عابر متولد شد. بعد از آن شالح ۴۰۳ سال ديگر زندگی كرد و صاحب پسران و دختران شد.

16‏-17وقتی عابرسی و چهار ساله بود، پسرش فالج متولد شد. پس از آن، عابر ۴۳۰ سال ديگر زندگی كرد و صاحب پسران و دختران شد.

18‏-19فالج سی ساله بود كه پسرش رعو متولد شد. پس از آن، او ۲۰۹ سال ديگر زندگی كرد و صاحب پسران و دختران شد.

20‏-21وقتی رعو سی و دو ساله بود، پسرش سروج متولد شد. پس از آن، رعو ۲۰۷ سال ديگر زندگی كرد و صاحب پسران و دختران شد.

22‏-23وقتی سروج سی ساله بود، پسرش ناحور به دنيا آمد. پس از آن سروج ۲۰۰ سال ديگر زندگی كرد و صاحب پسران و دختران شد.

24‏-25ناحور در موقع تولدِ پسرش تارح، بيست و نه سال داشت، و ۱۱۹ سال ديگر زندگی كرد و صاحب پسران و دختران شد.

26‏-27تارح پس از هفتاد سالگی صاحب سه پسر شد به نامهای ابرام، ناحور و هاران. هاران پسری داشت به نام لوط. 28هاران در همان جايی كه به دنيا آمده بود (يعنی اور كلدانيان) در برابر چشمان پدرش در سن جوانی درگذشت.

29ابرام با خواهر ناتنی خود سارای، و ناحور با برادرزادهٔ خويش مِلكه ازدواج كردند. (مِلكه دختر هاران بود و برادرش يسكا نام داشت.) 30سارای نازا بود و فرزندی نداشت.

31تارح پسرش ابرام، نوه‌اش لوط و عروسش سارای را با خود برداشت و اور كلدانيان را به قصد كنعان ترک گفت. اما وقتی آنها به شهر حران رسيدند در آنجا ماندند. 32تارح در سن ۲۰۵ سالگی در حران درگذشت.