Genesis 11 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 11:1-32

Nsanja ya Babeli

1Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi. 2Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.

3Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula. 4Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”

5Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga. 6Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita. 7Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”

8Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo. 9Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.

Mibado Kuyambira pa Semu Mpaka Abramu

10Nayi mibado yochokera kwa Semu.

Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi. 11Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

12Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela. 13Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

14Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi. 15Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

16Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi. 17Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

18Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu. 19Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

20Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi. 21Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

22Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori. 23Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

24Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera. 25Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

26Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.

Mibado Yochokera mwa Tera

27Nayi mibado yochokera mwa Tera.

Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti. 28Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira. 29Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani. 30Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.

31Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.

32Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

创世记 11:1-32

巴别塔

1那时,天下人都用同一种语言,讲同一种话。 2人们向东迁移时,在示拿地区找到一处平原,定居下来。 3他们彼此商量说:“来呀,我们烧些砖吧。”他们用砖作石块,用柏油作水泥来造塔, 4说:“来吧,让我们造一座城和一座高耸入云的塔,这样我们可以扬名天下,不致分散在地上。” 5耶和华从天上下来,要察看人建造的城和塔。 6耶和华说:“看啊,他们同属一个民族,都用同一种语言,现在就做这样的事,如果继续下去,他们会为所欲为。 7让我们下去变乱他们的语言,使他们彼此言语不通。” 8于是,耶和华把他们从那里分散到世界各地,他们便不再建造那城了。 9因此,人称那城为巴别,因为耶和华在那里变乱了人类的语言,把他们分散到世界各地。

闪的后代

10以下是的后代。

洪水过后两年,一百岁生亚法撒11之后又活了五百年,生儿育女。

12亚法撒三十五岁生沙拉13之后又活了四百零三年,生儿育女。

14沙拉三十岁生希伯15之后又活了四百零三年,生儿育女。

16希伯三十四岁生法勒17之后又活了四百三十年,生儿育女。

18法勒三十岁生拉吴19之后又活了二百零九年,生儿育女。

20拉吴三十二岁生西鹿21之后又活了二百零七年,生儿育女。

22西鹿三十岁生拿鹤23之后又活了二百年,生儿育女。

24拿鹤二十九岁生他拉25之后又活了一百一十九年,生儿育女。

26他拉七十岁后,生了亚伯兰拿鹤哈兰

他拉的后代

27以下是他拉的后代。

他拉亚伯兰拿鹤哈兰哈兰罗得28哈兰比他父亲他拉先去世,他死在自己的家乡——迦勒底吾珥29亚伯兰拿鹤都娶了妻子,亚伯兰的妻子名叫撒莱拿鹤的妻子名叫密迦,是哈兰的女儿。哈兰密迦亦迦的父亲。 30撒莱不能生育,没有孩子。

31他拉带着儿子亚伯兰、孙子——哈兰的儿子罗得、儿媳妇——亚伯兰的妻子撒莱,离开迦勒底吾珥前往迦南,他们来到哈兰定居下来。 32他拉在那里去世,享年二百零五岁11:32 二百零五岁”有古卷作“一百四十五岁”。