Genesis 11 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 11:1-32

Nsanja ya Babeli

1Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi. 2Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.

3Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula. 4Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”

5Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga. 6Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita. 7Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”

8Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo. 9Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.

Mibado Kuyambira pa Semu Mpaka Abramu

10Nayi mibado yochokera kwa Semu.

Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi. 11Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

12Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela. 13Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

14Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi. 15Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

16Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi. 17Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

18Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu. 19Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

20Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi. 21Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

22Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori. 23Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

24Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera. 25Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.

26Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.

Mibado Yochokera mwa Tera

27Nayi mibado yochokera mwa Tera.

Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti. 28Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira. 29Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani. 30Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.

31Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.

32Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Начало 11:1-32

Вавилонская башня

1Во всём мире был один язык и одно наречие. 2Двигаясь к востоку11:2 Или: «с востока»., люди вышли на равнину в Вавилонии и поселились там.

3Они сказали друг другу:

– Давайте сделаем кирпичи и обожжём их получше.

Кирпичи у них были вместо камня, а смола была вместо известкового раствора. 4Потом они сказали:

– Давайте построим себе город с башней до небес, чтобы прославить своё имя и не рассеяться по всей земле.

5Вечный сошёл посмотреть на город и башню, которые строили люди, 6и сказал:

– Все люди – один народ и у них один язык; вот они и затеяли такое; теперь не будет для них ничего невозможного. 7Сойдём же и смешаем им язык, чтобы они перестали понимать друг друга.

8И Вечный рассеял их оттуда по всему свету, и они перестали строить тот город. 9Вот почему он был назван Вавилоном («смешение»)11:9 На языке оригинала наблюдается игра слов: вавилонское баб-или («ворота бога») созвучно с еврейским глаголом «смешивать» (балал). – ведь Вечный смешал там язык всего мира. Оттуда Он рассеял их по всей земле.

Потомки от Сима до Иброма

(1 Лет. 1:24-27)

10Вот родословие Сима.

Симу было сто лет, когда у него родился Арфаксад, через два года после потопа. 11После рождения Арфаксада Сим жил пятьсот лет, и у него были ещё сыновья и дочери.

12Когда Арфаксад прожил тридцать пять лет, у него родился Шелах. 13После рождения Шелаха Арфаксад жил четыреста три года, и у него были ещё сыновья и дочери.

14Когда Шелах прожил тридцать лет, у него родился Евер. 15После рождения Евера Шелах жил четыреста три года, и у него были ещё сыновья и дочери.

16Когда Евер прожил тридцать четыре года, у него родился Фалек. 17После рождения Фалека Евер жил четыреста тридцать лет, и у него были ещё сыновья и дочери.

18Когда Фалек прожил тридцать лет, у него родился Реу. 19После рождения Реу Фалек жил двести девять лет, и у него были ещё сыновья и дочери.

20Когда Реу прожил тридцать два года, у него родился Серуг. 21После рождения Серуга Реу жил двести семь лет, и у него были ещё сыновья и дочери.

22Когда Серуг прожил тридцать лет, у него родился Нахор. 23После рождения Нахора Серуг жил двести лет, и у него были ещё сыновья и дочери.

24Когда Нахор прожил двадцать девять лет, у него родился Терах. 25После рождения Тераха Нахор жил сто девятнадцать лет, и у него были ещё сыновья и дочери.

26После того как Терах прожил семьдесят лет, у него родились Ибром, Нахор и Аран.

Родословие Тераха и его переселение с Халдейской земли в Харран

27Вот родословие Тераха.

У Тераха родились Ибром, Нахор и Аран. У Арана родился Лут. 28Когда его отец Терах был ещё жив, Аран умер в Уре Халдейском, в земле, где он родился. 29Ибром и Нахор взяли себе жён. Жену Иброма звали Сара, а жену Нахора – Милка, она была дочерью Арана, отца Милки и Иски. 30Сара была бесплодна, и у неё не было детей.

31Терах взял своего сына Иброма, своего внука Лута, сына Арана, и свою невестку Сару, жену Иброма, и вместе они отправились из Ура Халдейского в Ханон. Но дойдя до Харрана, они поселились там. 32Терах жил двести пять лет и умер в Харране.