Genesis 10 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 10:1-32

Mndandanda wa Mitundu ya Anthu

1Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.

Banja la Yafeti

2Ana aamuna a Yafeti anali:

Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.

3Ana aamuna a Gomeri anali:

Asikenazi, Rifati ndi Togarima.

4Ana aamuna a Yavani anali:

Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu. 5(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).

Banja la Hamu

6Ana aamuna a Hamu anali:

Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.

7Ana aamuna a Kusi anali:

Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka.

Ana aamuna a Raama anali:

Seba ndi Dedani.

8Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi. 9Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.” 10Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara. 11Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala, 12ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.

13Igupto ndiye kholo la

Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu, 14Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).

15Kanaani anabereka mwana wake wachisamba,

Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti; 16Ayebusi, Aamori, Agirigasi; 17Ahivi, Aariki, Asini, 18Aaravadi, Azemari ndi Ahamati.

Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse, 19mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.

20Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.

Banja la Semu

21Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.

22Ana aamuna a Semu anali:

Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.

23Ana aamuna a Aramu anali:

Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.

24Aripakisadi anabereka Sela,

ndipo Selayo anabereka Eberi.

25A Eberi anabereka ana aamuna awiri:

Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.

26Yokitani anabereka

Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera, 27Hadoramu, Uzali, Dikila, 28Obali, Abimaeli, Seba, 29Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.

30Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.

31Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.

32Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.

Persian Contemporary Bible

پيدايش 10:1-32

انشعاب قومهای جهان

(اول تواريخ 1‏:5‏-23)

1اينها هستند نسل سام و حام و يافث، پسران نوح، كه بعد از طوفان متولد شدند:

نسل يافث

2پسران10‏:2 «پسران» می‌تواند به معنی «نسل» يا «اعقاب» و يا «قومها» باشد. همچنين در آيات 3‏،4‏،6‏،7‏،22‏،23‏،26‏،30‏.‏ يافث عبارت بودند از: جومر، ماجوج، مادای، ياوان، توبال، ماشَک و تيراس.

3پسران جومر: اَشكناز، ريفات و توجَرمِه.

4پسران ياوان: اليشه، ترشيش، كتيم و رودانيم.

5فرزندان اين افراد به تدریج در سواحل و جزاير دنيا پخش شدند و اقوامی را با زبانهای گوناگون به وجود آوردند.

نسل حام

6پسران حام عبارت بودند از: كوش، مصرايم، فوط و كنعان.

7پسران كوش: سبا، حويله، سبته، رعمه و سبتكا. پسران رعمه: شبا و ددان.

8يكی از فرزندان كوش، شخصی بود به نام نمرود كه در دنيا، دلاوری بزرگ و معروف گشت. 9او با قدرتی كه خداوند به وی داده بود، تيرانداز ماهری شد؛ از اين جهت، وقتی می‌خواهند از مهارتِ تيراندازی كسی تعريف كنند، می‌گويند: «خداوند تو را در تيراندازی مانند نمرود گرداند.» 10قلمرو فرمانروايی او ابتدا شامل بابل، ارک، اكد و كلنه در سرزمين شنعار10‏:10 شنعار همان سرزمين بابل است.‏ بود. 11‏-12ولی بعد كشور آشور را نيز به قلمرو خود درآورد و نينوا، رحوبوت عير، كالح و ريسن را (واقع در بين نينوا و كالح) كه با هم شهر بزرگی را تشكيل می‌دادند، در آن كشور بنا كرد.

13‏-14مصرايم، جد اقوام زير بود: لودی‌ها، عنامی‌ها، لهابی‌ها، نفتوحی‌ها، فتروسی‌ها، كسلوحی‌ها (كه فلسطينی‌ها از اين قوم به وجود آمدند) و كفتوری‌ها.

15‏-19صيدون پسر ارشد كنعان بود و از كنعان اقوام زير به وجود آمدند: حيتّی‌ها، يبوسی‌ها، اموری‌ها، جرجاشی‌ها، حوّی‌ها، عرقی‌ها، سينی‌ها، اروادی‌ها، صماری‌ها و حماتی‌ها. فرزندان كنعان از سرزمين صيدون به سمت جرار تا غزه و به طرف سدوم و عموره و ادمه و صبوئيم تا به لاشع پراكنده شدند.

20اينها نسل حام بودند كه در قبايل و سرزمينهای خود زندگی می‌كردند و هر يک زبان خاص خود را داشتند.

نسل سام

21از نسل سام، كه برادر بزرگ يافث بود، عابر به وجود آمد (عابر جد عبرانيان است). 22اين است اسامی پسران سام: عيلام، آشور، ارفكشاد، لود و ارام.

23اينانند پسران ارام: عوص، حول، جاتر و ماشک.

24ارفكشاد پدر شالح، و شالح پدر عابر بود.

25عابر صاحب دو پسر شد به نامهای: فالح (يعنی «تفرقه» زيرا در زمان او بود كه مردم دنيا متفرق شدند) و يُقطان.

26‏-30الموداد، شالف، حضرموت، يارح، هدورام، اوزال، دقله، عوبال، ابيمائيل، شبا، اوفير، حويله و يوباب پسران يُقطان بودند. ايشان از نواحی ميشا تا كوهستانهای شرقی سفاره پراكنده بودند و در آنجا زندگی می‌كردند.

31اينها بودند فرزندان سام كه در قبايل و سرزمينهای خود زندگی می‌كردند و هر يک زبان خاص خود را داشتند.

32همهٔ افرادی كه در بالا نام برده شدند، از نسل نوح بودند كه بعد از طوفان، در دنيا پخش شدند و قومهای گوناگون را به وجود آوردند.