Genesis 10 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 10:1-32

Mndandanda wa Mitundu ya Anthu

1Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.

Banja la Yafeti

2Ana aamuna a Yafeti anali:

Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.

3Ana aamuna a Gomeri anali:

Asikenazi, Rifati ndi Togarima.

4Ana aamuna a Yavani anali:

Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu. 5(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).

Banja la Hamu

6Ana aamuna a Hamu anali:

Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.

7Ana aamuna a Kusi anali:

Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka.

Ana aamuna a Raama anali:

Seba ndi Dedani.

8Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi. 9Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.” 10Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara. 11Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala, 12ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.

13Igupto ndiye kholo la

Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu, 14Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).

15Kanaani anabereka mwana wake wachisamba,

Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti; 16Ayebusi, Aamori, Agirigasi; 17Ahivi, Aariki, Asini, 18Aaravadi, Azemari ndi Ahamati.

Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse, 19mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.

20Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.

Banja la Semu

21Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.

22Ana aamuna a Semu anali:

Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.

23Ana aamuna a Aramu anali:

Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.

24Aripakisadi anabereka Sela,

ndipo Selayo anabereka Eberi.

25A Eberi anabereka ana aamuna awiri:

Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.

26Yokitani anabereka

Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera, 27Hadoramu, Uzali, Dikila, 28Obali, Abimaeli, Seba, 29Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.

30Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.

31Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.

32Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.

King James Version

Genesis 10:1-32

1Now these are the generations of the sons of Noah, Shem, Ham, and Japheth: and unto them were sons born after the flood. 2The sons of Japheth; Gomer, and Magog, and Madai, and Javan, and Tubal, and Meshech, and Tiras. 3And the sons of Gomer; Ashkenaz, and Riphath, and Togarmah. 4And the sons of Javan; Elishah, and Tarshish, Kittim, and Dodanim.10.4 Dodanim: or, as some read it, Rodanim 5By these were the isles of the Gentiles divided in their lands; every one after his tongue, after their families, in their nations.

6¶ And the sons of Ham; Cush, and Mizraim, and Phut, and Canaan. 7And the sons of Cush; Seba, and Havilah, and Sabtah, and Raamah, and Sabtecha: and the sons of Raamah; Sheba, and Dedan. 8And Cush begat Nimrod: he began to be a mighty one in the earth. 9He was a mighty hunter before the LORD: wherefore it is said, Even as Nimrod the mighty hunter before the LORD. 10And the beginning of his kingdom was Babel, and Erech, and Accad, and Calneh, in the land of Shinar.10.10 Babel: Gr. Babylon 11Out of that land went forth Asshur, and builded Nineveh, and the city Rehoboth, and Calah,10.11 went…: or, he went out into Assyria10.11 the city…: or, the streets of the city 12And Resen between Nineveh and Calah: the same is a great city. 13And Mizraim begat Ludim, and Anamim, and Lehabim, and Naphtuhim, 14And Pathrusim, and Casluhim, (out of whom came Philistim,) and Caphtorim.

15¶ And Canaan begat Sidon his firstborn, and Heth,10.15 Sidon: Heb. Tzidon 16And the Jebusite, and the Amorite, and the Girgasite, 17And the Hivite, and the Arkite, and the Sinite, 18And the Arvadite, and the Zemarite, and the Hamathite: and afterward were the families of the Canaanites spread abroad. 19And the border of the Canaanites was from Sidon, as thou comest to Gerar, unto Gaza; as thou goest, unto Sodom, and Gomorrah, and Admah, and Zeboim, even unto Lasha.10.19 Gaza: Heb. Azzah 20These are the sons of Ham, after their families, after their tongues, in their countries, and in their nations.

21¶ Unto Shem also, the father of all the children of Eber, the brother of Japheth the elder, even to him were children born. 22The children of Shem; Elam, and Asshur, and Arphaxad, and Lud, and Aram.10.22 Arphaxad: Heb. Arpachshad 23And the children of Aram; Uz, and Hul, and Gether, and Mash. 24And Arphaxad begat Salah; and Salah begat Eber.10.24 Salah: Heb. Shelah 25And unto Eber were born two sons: the name of one was Peleg; for in his days was the earth divided; and his brother’s name was Joktan.10.25 Peleg: that is Division 26And Joktan begat Almodad, and Sheleph, and Hazarmaveth, and Jerah, 27And Hadoram, and Uzal, and Diklah, 28And Obal, and Abimael, and Sheba, 29And Ophir, and Havilah, and Jobab: all these were the sons of Joktan. 30And their dwelling was from Mesha, as thou goest unto Sephar a mount of the east. 31These are the sons of Shem, after their families, after their tongues, in their lands, after their nations. 32These are the families of the sons of Noah, after their generations, in their nations: and by these were the nations divided in the earth after the flood.