Mndandanda wa Mitundu ya Anthu
1Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
Banja la Yafeti
2Ana aamuna a Yafeti anali:
Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
3Ana aamuna a Gomeri anali:
Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
4Ana aamuna a Yavani anali:
Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu. 5(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
Banja la Hamu
6Ana aamuna a Hamu anali:
Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
7Ana aamuna a Kusi anali:
Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka.
Ana aamuna a Raama anali:
Seba ndi Dedani.
8Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi. 9Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.” 10Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara. 11Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala, 12ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
13Igupto ndiye kholo la
Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu, 14Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
15Kanaani anabereka mwana wake wachisamba,
Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti; 16Ayebusi, Aamori, Agirigasi; 17Ahivi, Aariki, Asini, 18Aaravadi, Azemari ndi Ahamati.
Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse, 19mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
20Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
Banja la Semu
21Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
22Ana aamuna a Semu anali:
Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
23Ana aamuna a Aramu anali:
Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
24Aripakisadi anabereka Sela,
ndipo Selayo anabereka Eberi.
25A Eberi anabereka ana aamuna awiri:
Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
26Yokitani anabereka
Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera, 27Hadoramu, Uzali, Dikila, 28Obali, Abimaeli, Seba, 29Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
30Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
31Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
32Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.
挪亞三個兒子的後代
1洪水以後,挪亞的兒子閃、含和雅弗都生養了兒女,以下是他們的後代。
2雅弗的兒子是歌篾、瑪各、瑪代、雅完、土巴、米設、提拉。 3歌篾的兒子是亞實基拿、利法、陀迦瑪。 4雅完的兒子是以利沙、他施、基提、多單。 5雅弗的這些後裔按宗族、語言和民族分散在各海島。
6含的兒子是古實、麥西10·6 「麥西」希伯來文是Mizraim,就是「埃及」,13節亦同。、弗、迦南。 7古實的兒子是西巴、哈腓拉、撒弗他、拉瑪、撒弗提迦。拉瑪的兒子是示巴和底但。
8古實也是寧錄之父,寧錄是世上第一位勇士, 9在耶和華眼中是個孔武有力的獵人,因此有俗話說:「要像寧錄那樣在耶和華眼中是個孔武有力的獵人。」 10他首先在示拿地區的巴別、以力、亞甲、甲尼各地建國, 11後來擴展到亞述,在那裡建立了尼尼微、利河伯、迦拉各城, 12又在尼尼微與迦拉之間建立了利鮮大城。
13麥西的後代有路低人、亞拿米人、利哈比人、拿弗土希人、 14帕斯魯細人、迦斯路希人和迦斐托人。非利士人是迦斐托人的後代。
15迦南生長子西頓和次子赫, 16他的後代還有耶布斯人、亞摩利人、革迦撒人、 17希未人、亞基人、西尼人、 18亞瓦底人、洗瑪利人和哈馬人。後來迦南各宗族散居在各地。 19迦南的疆域從西頓向基拉耳延伸,遠至迦薩,再向所多瑪、蛾摩拉、押瑪、洗扁延伸,遠至拉沙。 20以上記載的都是含的子孫,他們根據自己的宗族、語言、地域和民族散居各處。
21雅弗的哥哥閃是希伯子孫的祖先。 22閃的兒子是以攔、亞述、亞法撒、路德、亞蘭。 23亞蘭的兒子是烏斯、戶勒、基帖、瑪施。 24亞法撒生沙拉,沙拉生希伯, 25希伯有兩個兒子,一個名叫法勒,意思是分開,因為那時人們分地而居。法勒的兄弟叫約坍。 26約坍生亞摩答、沙列、哈薩瑪非、耶拉、 27哈多蘭、烏薩、德拉、 28俄巴路、亞比瑪利、示巴、 29阿斐、哈腓拉、約巴。這些都是約坍的兒子。 30他們居住的地方,從米沙直到東邊的西發山區。 31以上記載的都是閃的子孫,他們按著自己的宗族、語言、地域和民族散居各處。
32這些人都是洪水以後挪亞三個兒子所生的子孫,他們按著自己的族系散居在各地,後來成為地上不同的民族。