Ezekieli 9 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 9:1-11

Opembedza Mafano Aphedwa

1Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.” 2Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.

3Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake 4ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”

5Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo. 6Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.

7Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse. 8Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”

9Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’ 10Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”

11Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以西结书 9:1-11

拜偶像者遭诛灭

1我听见祂高声呼喊说:“惩罚这城的人啊,拿起你们的兵器上前来吧!” 2只见六个人从北门走来,手中都拿着可怕的兵器。其中有一人身穿细麻衣,腰间带着墨盒。他们进入殿里,站在铜祭坛旁边。

3以色列上帝的荣耀原本在基路伯天使上,现在升到了殿门口。上帝把那身穿细麻衣、腰带墨盒的人召来, 4对他说:“你去走遍耶路撒冷,在那些因城中可憎之事而叹息哀伤的人额上画个记号。” 5我听见祂对其余的人说:“你们要跟随他走遍全城,毫不留情地杀戮, 6将男女老幼全部杀尽,但你们不能伤害额上有记号的。你们要从圣所开始。”于是他们首先杀了殿前的众长老。 7祂又对他们说:“要玷污这殿,把你们所杀的堆满整个院子。去吧!”他们便出去,在城中杀戮。 8那时,只留下我一个人,我便俯伏在地上呼求:“唉,主耶和华啊!你向耶路撒冷倾倒你的烈怒,要灭绝以色列所有的余民吗?”

9祂回答说:“以色列犹大人罪大恶极,遍地是血腥,满城是冤屈,他们说,‘耶和华丢弃了这片土地,祂看不见我们。’ 10因此,我必不顾惜他们,也不怜悯他们,我必照他们的所作所为报应他们。”

11那个身穿细麻衣,腰带墨盒的人回来禀告说:“我已照你的吩咐做了。”