Ezekieli 9 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 9:1-11

Opembedza Mafano Aphedwa

1Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.” 2Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.

3Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake 4ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”

5Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo. 6Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.

7Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse. 8Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”

9Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’ 10Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”

11Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”

La Bible du Semeur

Ezéchiel 9:1-11

Préfiguration du châtiment

1Puis je l’entendis crier d’une voix forte : Approchez, inspecteurs de la ville ! Que chacun prenne son instrument de destruction en main9.1 Pour les v. 1-6, voir Ap 7.1-8 ; 9.4. !

2Je vis six individus déboucher du chemin de la porte supérieure qui fait face au nord ; chacun tenait en main son instrument de destruction. Au milieu d’eux se tenait un individu vêtu de lin et portant une écritoire à la ceinture. Ils vinrent se placer à côté de l’autel de bronze. 3Alors la gloire du Dieu d’Israël s’éleva au-dessus du chérubin sur lequel elle reposait et se dirigea vers le seuil du Temple9.3 La gloire de l’Eternel va quitter le Temple (voir 8.4 et note).. L’Eternel appela l’individu vêtu de lin qui portait l’écritoire à sa ceinture 4et il lui dit : Passe au milieu de la ville de Jérusalem et marque d’une croix sur le front les hommes qui gémissent et se plaignent à cause de toutes les pratiques abominables qui se commettent dans cette ville.

5Puis je l’entendis dire aux autres : Passez dans la ville derrière lui et frappez sans un regard de pitié ! Soyez sans merci. 6Tuez les vieillards, les jeunes gens, les jeunes filles, les enfants, les femmes, jusqu’à ce que tous soient exterminés ! Mais ne touchez pas à ceux qui portent sur le front la marque d’une croix. Vous commencerez par mon sanctuaire.

Ils commencèrent donc par les responsables du peuple qui se tenaient devant le Temple9.6 C’est-à-dire les vingt-cinq hommes de 8.16.. 7Puis il leur ordonna : Rendez le Temple impur et remplissez ses parvis de morts ! Allez !

Et ils partirent et frappèrent dans la ville. 8Pendant qu’ils frappaient, comme je restais seul sur place, je tombai sur ma face, et je m’écriai : Ah ! Seigneur, Eternel, en déchaînant ainsi ta colère sur Jérusalem, vas-tu exterminer tout ce qui reste d’Israël ?

9Il me répondit : Le péché des royaumes d’Israël et de Juda est excessivement grave. Le pays est rempli de sang et la ville est pleine d’injustices. Les gens disent : « L’Eternel a quitté ce pays, l’Eternel ne voit rien ! » 10Eh bien, je n’aurai aucun regard de pitié et je serai sans merci. Je ferai retomber sur eux ce que mérite leur conduite.

11A ce moment, l’individu vêtu de lin blanc qui portait une écritoire à la ceinture vint faire son rapport. Il dit : J’ai fait ce que tu m’as commandé.