Ezekieli 8 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 8:1-18

Kupembedza Mafano Mʼnyumba ya Mulungu

1Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira. 2Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira. 3Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu. 4Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.

5Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.

6Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”

7Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo. 8Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.

9Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.” 10Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza. 11Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.

12Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’ 13Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’ ”

14Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi. 15Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”

16Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.

17Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo! 18Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”

New Russian Translation

Иезекииль 8:1-18

Идолопоклонство в храме

1В шестом году, в пятый день шестого месяца8:1 17 сентября 592 г. до н. э., когда я сидел у себя дома, и старейшины Иудеи сидели передо мной, рука Владыки Господа, снизошла на меня там. 2Я посмотрел, и увидел Кого-то, похожего на человека8:2 Так в одном из древних переводов; в нормативном еврейском тексте: «облик, похожий на огонь».. Ниже пояса Он был похож на огонь, а выше пояса Он сверкал, как сияющий металл. 3Он простер подобие руки и взял меня за волосы. Дух поднял меня между землей и небом и в видениях Божьих принес меня в Иерусалим, ко входу в северные ворота внутреннего двора, где стоял идол, вызывающий Божью ревность. 4И вот, там предо мной явилась слава Бога Израиля, как в том видении, которое я видел на равнине. 5И Бог сказал мне:

– Сын человеческий, посмотри на север.

Я посмотрел, и с северной стороны у ворот жертвенника увидел идола ревности. 6Бог сказал мне:

– Сын человеческий, ты видишь, что они делают, – эти страшные мерзости, которые дом Израиля творит здесь, чтобы удалить Меня из Моего святилища? Но ты увидишь еще большие мерзости.

7Он привел меня ко входу во двор. Я посмотрел и увидел отверстие в стене. 8Он сказал мне:

– Сын человеческий, прокопай стену.

Я прокопал и увидел какую-то дверь.

9Он сказал мне:

– Войди и посмотри на гнусные мерзости, которые они здесь творят.

10Я вошел, посмотрел и увидел нарисованные на стенах кругом изображения всяких ползучих тварей, мерзких животных и всех идолов дома Израиля. 11Перед ними стояли семьдесят старейшин дома Израиля, и Иазания, сын Шафана, стоял среди них. Каждый держал в руке кадильницу, и поднималось благовонное облако дыма.

12Бог сказал мне:

– Сын человеческий, ты видел, что старейшины дома Израиля творят во мраке, каждый в святилище своего лжебога? Они говорят: «Господь не видит нас; Господь бросил страну».

13И опять Он сказал мне:

– Ты увидишь еще большие мерзости, которые они делают.

14Он привел меня ко входу в северные ворота Господнего дома, и я увидел сидящих там женщин, которые оплакивали Таммуза8:14 Вавилонский бог плодородия и дождя, который по повериям умирал в начале засухи и воскресал в начале сезона дождей..

15Он сказал мне:

– Видишь это, сын человеческий? Ты увидишь еще большие мерзости.

16Он ввел меня во внутренний двор Господнего дома; там, у входа в храм, между притвором и жертвенником, было около двадцати пяти мужчин. Обратившись спиной к Господнему храму, а лицами на восток, они поклонялись солнцу на востоке. 17Он сказал мне:

– Видел это, сын человеческий? Разве не достаточно скверно для дома Иуды совершать те мерзости, которые они здесь творят? Зачем они наполняют страну насилием и возбуждают Мой гнев еще сильнее? Гляди, как они подносят ветви к своим носам! 18За это Я изолью на них Свой гнев; Я не гляну на них с жалостью и не пощажу. Пусть кричат Мне в самые уши, Я не стану их слушать.