Ezekieli 8 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 8:1-18

Kupembedza Mafano Mʼnyumba ya Mulungu

1Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira. 2Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira. 3Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu. 4Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.

5Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.

6Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”

7Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo. 8Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.

9Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.” 10Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza. 11Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.

12Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’ 13Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’ ”

14Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi. 15Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”

16Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.

17Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo! 18Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”

Bibelen på hverdagsdansk

Ezekiels Bog 8:1-18

Folkets afgudsdyrkelse

1På den femte dag i den sjette måned i det sjette år af vores eksil i Babylonien opholdt jeg mig i mit hus sammen med en gruppe af Judas ledere. Da kom Guds kraft over mig, 2og jeg fik igen et syn. Jeg så en skikkelse, der så ud som et menneske. Fra hofterne og nedefter så han ud som flammende ild, og fra hofterne og opefter så han ud som glødende metal. 3Han rakte noget ligesom en hånd ud og greb mig i håret. Ånden løftede mig op i luften, så jeg svævede mellem himmel og jord, og jeg blev i synet ført til Jerusalem, til templets indre forgård, hvor der tæt ved den nordlige indgang var opstillet et stort afgudsbillede, som vakte Herrens vrede.

4Pludselig fyldte Guds stråleglans stedet på samme måde, som jeg tidligere havde set den i dalen, 5og han sagde til mig: „Du menneske, se mod nord!” Da jeg gjorde det, kunne jeg se det afskyelige afgudsbillede ved den nordlige indgang, tæt ved alteret. 6„Ser du, hvem de bringer deres ofre til?” fortsatte han. „Ser du, hvilke afskyelige handlinger Israels folk begår? På den måde jager de mig ud af mit eget tempel. Men du vil få endnu værre ting at se.”

7Så førte han mig hen til indgangen til den ydre forgård, og jeg kunne se et hul i muren.

8„Gør hullet større!” beordrede han, og da jeg gjorde det, opdagede jeg en dør til en stor sal.

9„Gå ind,” beordrede han, „så skal du se den ondskab, som går for sig derinde.” 10Så gik jeg ind gennem døren.

Indenfor så jeg, at væggene var fyldt med billeder af alle mulige urene dyr og afskyelige afguder. De var mejslet ind i væggen hele vejen rundt. 1170 af Israels ledere, deriblandt Ja’azanja, Shafans søn, stod hele vejen rundt foran billederne og tilbad dem hver med sit røgelseskar i hånden. En tyk sky af røgelse hang i luften. 12„Se hvordan de israelitiske ledere i hemmelighed tilbeder afguder i deres bedehuse,” sagde Herren. „De siger, at jeg ikke kan se dem, og at jeg har forladt landet og ladt dem i stikken. 13Men kom, så skal jeg vise dig noget, som er endnu værre.”

14Derefter førte han mig til den nordlige indgang til den ydre forgård, hvor der sad en flok kvinder og fejrede den årlige sørgehøjtid for afguden Tammuz.8,14 En frugtbarhedsgud, som mentes at dø hvert efterår og komme til live igen om foråret. 15„Er det ikke forfærdeligt at se på?” spurgte han. „Men kom, så skal jeg vise dig noget, som er endnu værre.”

16Så førte han mig ind i templets indre forgård. Og der, mellem alteret og forhallen ind til selve tempelbygningen, stod omkring 25 mænd8,16 De 25 repræsenterer de 24 præsteskifter plus ypperstepræsten, altså hele præstestanden. med ryggen til Herrens tempel. Med ansigtet vendt mod øst tilbad de solen!

17„Er det ikke forfærdeligt at se på?” spurgte han. „Ikke alene tilbeder Judas folk afguderne her lige foran mit tempel, men de fylder også hele landet med vold. Deres stinkende afgudsdyrkelse er ulidelig.8,17 Den sidste del af verset er uforståelig. 18Derfor får de min vrede at føle. Jeg vil ikke skåne dem eller vise nogen form for medlidenhed. Nej, om de så skriger om nåde, vender jeg det døve øre til.”