Chimaliziro Chafika
1Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti, 2“Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti:
“Chimaliziro! Chimaliziro chafika
ku ngodya zinayi za dziko.
3Chimaliziro chili pa iwe tsopano.
Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe.
Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako
ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
4Ine sindidzakumvera chisoni
kapena kukuleka.
Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa
komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako.
Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
5“Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi:
“Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo!
Taona chikubwera!
6Chimaliziro chafika!
Chimaliziro chafika!
Chiwonongeko chakugwera.
Taona chafika!
7Inu anthu okhala mʼdziko,
chiwonongeko chakugwerani.
Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
8Ine ndili pafupi kukukwiyirani,
ndipo ukali wanga udzathera pa iwe;
Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako
ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
9Ine sindidzakumvera chisoni
kapena kukuleka.
Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako
ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
‘Pamenepo udzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndimakantha.’
10“Taona, tsikulo!
Taona, lafika!
Chiwonongeko chako chabwera.
Ndodo yaphuka mphundu za maluwa.
Kudzitama kwaphuka.
11Chiwawa chasanduka ndodo
yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo.
Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale.
Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo.
Palibiretu ndipo sipadzapezeka
munthu wowalira maliro.
12Nthawi yafika!
Tsiku layandikira!
Munthu wogula asakondwere
ndipo wogulitsa asamve chisoni,
popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
13Wogulitsa sadzazipezanso zinthu
zimene anagulitsa kwa wina
chinkana onse awiri akanali ndi moyo,
pakuti chilango chidzagwera onsewo
ndipo sichingasinthike.
Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense
amene adzapulumutsa moyo wake.
14“Lipenga lalira,
ndipo zonse zakonzeka.
Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo,
pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
15Ku bwalo kuli kumenyana
ndipo mʼkati muli mliri ndi njala.
Anthu okhala ku midzi
adzafa ndi nkhondo.
Iwo okhala ku mizinda
adzafa ndi mliri ndi njala.
16Onse amene adzapulumuka
ndi kumakakhala ku mapiri,
azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa.
Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
17Dzanja lililonse lidzalefuka,
ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
18Iwo adzavala ziguduli
ndipo adzagwidwa ndi mantha.
Adzakhala ndi nkhope zamanyazi
ndipo mitu yawo adzameta mpala.
19“Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu
ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa.
Siliva ndi golide wawo
sizidzatha kuwapulumutsa
pa tsiku la ukali wa Yehova.
Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala,
kapena kukhala okhuta,
pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
20Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka
ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa
kukhala zowanyansa.
21Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe.
Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda
ndi kudziyipitsa.
22Ine ndidzawalekerera anthuwo
ndipo adzayipitsa malo anga apamtima.
Adzalowamo ngati mbala
ndi kuyipitsamo.
23“Konzani maunyolo,
chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo
ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
24Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa
kuti idzalande nyumba zawo.
Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu
pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
25Nkhawa ikadzawafikira
adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
26Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake,
ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake.
Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri.
Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo,
ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
27Mfumu idzalira,
kalonga adzagwidwa ndi mantha.
Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha.
Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo,
ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.
Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
จุดจบมาถึงแล้ว
1พระดำรัสขององค์พระผู้เป็นเจ้ามาถึงข้าพเจ้าความว่า 2“บุตรมนุษย์เอ๋ย พระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตตรัสแก่ดินแดนอิสราเอลดังนี้ว่า
“ ‘จุดจบ! จุดจบ
มาเหนือสี่มุมของแผ่นดินแล้ว
3วาระสุดท้ายมาถึงเจ้าแล้ว
เราจะระบายความโกรธลงเหนือเจ้า
เราจะพิพากษาเจ้าตามความประพฤติของเจ้าและจะตอบแทนการกระทำอันน่าชิงชังทั้งสิ้นของเจ้า
4เราจะไม่เหลียวแลเจ้าด้วยความเอ็นดูสงสาร
หรือไว้ชีวิตเจ้า
เราจะตอบแทนเจ้าให้สาสมกับความประพฤติ
และการกระทำอันน่าชิงชังในหมู่พวกเจ้าอย่างแน่นอน
แล้วเจ้าจะรู้ว่าเราคือพระยาห์เวห์’
5“พระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตตรัสดังนี้ว่า
“ ‘ภัยพิบัติ! ภัยพิบัติอย่างที่ไม่เคยได้ยินมาก่อน7:5 สำเนาต้นฉบับภาษาฮีบรูบางฉบับ และฉบับ Syr. ว่าภัยพิบัติซ้อนภัยพิบัติ!
มันจะมาถึง!
6จุดจบมาถึงแล้ว!
จุดจบมาถึงแล้ว!
มันก่อตัวขึ้นมาเล่นงานเจ้า
มันมาถึงแล้ว!
7ความพินาศมาเหนือเจ้า
เหนือเจ้าผู้อาศัยอยู่ในดินแดน
ถึงเวลาแล้ว! วันนั้นใกล้เข้ามาแล้ว!
บนภูเขาทั้งหลายจะมีแต่ความโกลาหลอลหม่าน ไม่ใช่ความชื่นชมยินดี
8เรากำลังจะระบายโทสะลงเหนือเจ้า
และระบายความโกรธต่อเจ้า
เราจะพิพากษาเจ้าตามความประพฤติของเจ้า
และจะตอบแทนเจ้าให้สาสมกับการกระทำอันน่าชิงชังทั้งสิ้นของเจ้า
9เราจะไม่เหลียวแลเจ้าด้วยความเอ็นดูสงสาร
หรือไว้ชีวิตเจ้า
เราจะตอบแทนเจ้าให้สาสมกับความประพฤติ
และการกระทำอันน่าชิงชังในหมู่พวกเจ้า
เมื่อนั้นเจ้าจะรู้ว่าเราผู้เป็นพระยาห์เวห์นี่แหละที่ลงโทษพวกเจ้า
10“ ‘วันนั้นมาถึงแล้ว!
มันมาถึงแล้ว!
หายนะปะทุขึ้นแล้ว
ไม้เรียวผลิดอกแล้ว
และความหยิ่งยโสก็เบ่งบาน!
11ความทารุณก็เติบโต
เป็น7:11 หรือผู้ทารุณได้กลายเป็นไม้เรียวเพื่อลงโทษความชั่วร้าย
ไม่มีใครในชนชาตินั้น
ไม่มีสักคนในฝูงชนนั้น
ไม่มีทรัพย์สมบัติ
หรือสิ่งมีค่าเหลืออยู่เลย
12เวลานั้นมาถึงแล้ว!
วันนั้นมาถึงแล้ว!
อย่าให้ผู้ซื้อลิงโลด
อย่าให้ผู้ขายเศร้าโศก
เพราะพระพิโรธอยู่เหนือกลุ่มชนทั้งหมด
13ผู้ขายจะไม่ได้รับที่ดิน
ซึ่งขายไปกลับคืนมาเป็นของตน
ตราบเท่าที่ทั้งสองฝ่ายยังมีชีวิตอยู่
เพราะนิมิตเกี่ยวกับกลุ่มชนทั้งหมด
จะไม่ผันแปร
เนื่องจากบาปทั้งหลายของพวกเขา
จึงไม่มีแม้สักคนจะรักษาชีวิตของตนไว้ได้
14“ ‘แม้พวกเขาเป่าแตร
และเตรียมทุกสิ่งไว้พร้อมสรรพ
แต่ก็จะไม่มีใครออกรบเลย
เพราะโทสะของเราตกอยู่แก่กลุ่มชนทั้งหมด
15นอกกรุงคือสงคราม
ในกรุงคือโรคระบาดและการกันดารอาหาร
ผู้ที่อยู่ในท้องทุ่ง
ก็ตายเพราะสงคราม
ส่วนผู้ที่อยู่ในกรุง
ก็ถูกกลืนกินเพราะการกันดารอาหารและโรคระบาด
16คนทั้งปวงที่หนีรอดชีวิตไปได้
จะหนีไปอยู่ตามภูเขา
เหมือนนกพิราบตามหุบเขา
พวกเขาจะร้องครวญคราง
เพราะบาปของตน
17มือทุกมือจะอ่อนเปลี้ย
และเข่าทุกเข่าจะอ่อนปวกเปียกเหมือนน้ำ
18พวกเขาจะสวมใส่ผ้ากระสอบ
และนุ่งห่มความอกสั่นขวัญแขวน
ทุกใบหน้าจะถูกปิดด้วยความอัปยศอดสู
และทุกศีรษะจะถูกโกน
19“ ‘พวกเขาจะโยนเงินทิ้งตามถนน
ทองของพวกเขาจะมีค่าเท่ากับสิ่งโสโครก
เงินและทองของพวกเขา
จะไม่สามารถช่วยเขาให้รอดได้
ในวันแห่งพระพิโรธขององค์พระผู้เป็นเจ้า
มันจะไม่ช่วยแก้หิว
หรือช่วยให้อิ่มท้อง
เพราะมันทำให้พวกเขาสะดุดล้มลงในความบาป
20พวกเขาภูมิใจในเพชรพลอยอันงดงามของตน
และใช้มันทำรูปเคารพอันน่าชิงชัง
พวกเขาใช้มันทำเทวรูปอันชั่วช้าสามานย์
ดังนั้นเราจะเปลี่ยนสิ่งเหล่านี้ให้กลายเป็นสิ่งที่เป็นมลทินกับพวกเขา
21เราจะยกความมั่งคั่งของพวกเขาให้เป็นของปล้นแก่คนต่างชาติ
ให้เป็นของเชลยแก่คนชั่วร้ายบนโลก
ผู้ที่จะทำให้มันเป็นมลทิน
22เราจะเบือนหน้าหนีจากประชากร
และโจรจะย่ำยีสถานที่ที่เรารัก
พวกมันจะเข้ามา
และจะทำให้ที่นั่นเป็นมลทิน
23“ ‘จงเตรียมโซ่ตรวน!
เพราะแผ่นดินนองเลือด
และกรุงนี้เต็มไปด้วยความโหดร้ายทารุณ
24เราจะนำประชาชาติที่ชั่วร้ายที่สุด
มาครอบครองบ้านเรือนของพวกเขา
เราจะยุติความหยิ่งยโสของผู้มีอำนาจ
และสถานนมัสการของพวกเขาจะถูกทำให้เป็นมลทิน
25เมื่อความหวาดหวั่นพรั่นพรึงมาถึง
พวกเขาจะแสวงหาสันติภาพแต่ก็ไร้ประโยชน์
26หายนะโหมกระหน่ำเข้ามาครั้งแล้วครั้งเล่า
และมีข่าวลือระลอกแล้วระลอกเล่า
พวกเขาจะพยายามหานิมิตจากผู้เผยพระวจนะ
คำสอนของปุโรหิตจากบทบัญญัติจะหมดไป
คำปรึกษาของบรรดาผู้อาวุโสจะสูญสิ้นไป
27กษัตริย์จะคร่ำครวญ
เจ้านายจะคลุมกายด้วยความสิ้นหวัง
และประชาชนจะมือไม้สั่น
เราจะจัดการกับพวกเขาตามความประพฤติของพวกเขา
และเราจะพิพากษาพวกเขาตามมาตรฐานของพวกเขา
เมื่อนั้นพวกเขาจะรู้ว่าเราคือพระยาห์เวห์’ ”