Ezekieli 5 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 5:1-17

Chizindikiro cha Chiweruzo

1Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu. 2Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga. 3Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako. 4Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”

5Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira. 6Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.

7“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.

8“Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona. 9Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo. 10Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi. 11Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni. 12Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.

13“Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.

14“Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo 15Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula. 16Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku. 17Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Езекиил 5:1-17

1Теперь, смертный, возьми острый меч и обрей им, как бритвой цирюльника, себе голову и бороду. Возьми весы и раздели волосы на части. 2Когда дни твоей осады закончатся, сожги треть волос посреди нарисованного города. Другую треть возьми и изруби вокруг города мечом. Оставшуюся треть развей по ветру, и Я обнажу Свой меч и буду преследовать их. 3Но несколько волосков возьми и завяжи в край одежды. 4А из них возьми ещё, брось в огонь и дай сгореть. Огонь полыхнёт оттуда на весь народ Исраила.

5Так говорит Владыка Вечный:

– Это Иерусалим; Я поставил его посреди народов, и вокруг него – страны. 6Но он восстал против Моих законов и установлений, сделавшись нечестивее народов и стран, которые вокруг него; он отверг Мои законы и не соблюдал Моих установлений.

7Поэтому так говорит Владыка Вечный:

– Вы были непокорнее народов, которые вокруг вас, не соблюдали Моих установлений и не исполняли Моих законов, и даже не поступали5:7 Или: «даже поступали». по обычаям народов, которые вокруг вас.

8Поэтому так говорит Владыка Вечный:

– Смотри, Я Сам стал твоим противником; Я исполню над тобой приговор на глазах у народов. 9Из-за твоих омерзительных идолов Я сделаю с тобой то, чего не делал прежде и не сделаю впредь. 10За это ваши отцы будут есть своих детей, а дети будут есть своих отцов. Я исполню над тобой приговор и развею уцелевших по всем ветрам.

11Верно, как и то, что Я живу, – возвещает Владыка Вечный, – за то, что ты осквернил Моё святилище своими гнусными истуканами и омерзительными обычаями, Я сражу тебя: не взгляну на тебя с жалостью и не пощажу. 12Треть твоего народа умрёт от мора или погибнет от голода; треть падёт от меча за твоими стенами; а треть Я развею по ветру, обнажу Свой меч и буду преследовать их.

13Тогда Мой гнев угаснет, ярость против них уляжется, и Я буду удовлетворён. Когда Я изолью на них ярость, они узнают, что это Я, Вечный, говорил, объятый ревностью.

14Я сделаю тебя пустырём и позорищем у народов, которые вокруг тебя, в глазах всех, кто будет проходить мимо. 15Ты станешь позорищем и насмешкой, уроком и ужасом для всех народов, которые вокруг тебя, когда Я исполню над тобой приговор в гневе и в ярости, в неистовых казнях. Я, Вечный, сказал это. 16Я буду пускать в тебя злые стрелы голода, чтобы погубить тебя. Я усилю у тебя голод и уничтожу запасы пищи. 17Я нашлю на тебя голод и диких зверей, и они лишат тебя детей. Мор и кровопролитие пройдут по тебе, и Я наведу на тебя меч. Я, Вечный, сказал это.