Ezekieli 47 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 47:1-23

Mtsinje Wotuluka Mʼnyumba ya Mulungu

1Munthuyo anabwerera nane ku chipata cha Nyumba ya Mulungu. Ndinaona madzi akutuluka kunsi kwa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu chakummawa; poti Nyumba ya Mulungu inayangʼana kummawa. Madziwo ankachokera kunsi kwa mbali yakummwera ya Nyumba ya Mulungu; kummwera kwa guwa lansembe. 2Ananditulutsira pa chipata chakumpoto ndipo anazungulira nane panja mpaka ku chipata chakunja choyangʼana kummawa. Ndipo ndinaona madzi akutuluka chakummwera kwa chipatacho.

3Munthuyo anapita chakummawa ali ndi chingwe choyezera mʼdzanja lake. Iye anayeza mamita 500, ndipo pambuyo pake analowa nane mʼmadziwo amene ankalekeza mʼkakolo. 4Anayezanso mamita 500 ndipo analowa nane mʼmadzi amene amalekeza mʼmawondo. Iye anayezanso mamita 500 ndipo analowa nane mʼmadzi amene amalekeza mʼchiwuno. 5Munthuyo anayezanso mamita 500, ndipo madziwo anasanduka mtsinje woti sindikanatha kuwoloka, pakuti madziwo anakwera, ndipo anali ozama ofunika kusambira pofuna kuwoloka. 6Munthuyo anandifunsa kuti: “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi?”

Kenaka anabwerera nane ku gombe la mtsinjewo. 7Nditafika pa gombepo, ndinaona mitengo yambiri ku mbali iliyonse ya mtsinjewo. 8Tsono munthuyo anandiwuza kuti, “Madziwa akupita ku chigawo chakummawa ndi kutsikira ku chigwa cha Araba. Kenaka akathira mʼNyanja Yakufa, ndipo akakalowa mʼnyanjayo, madzi a nyanjayo adzasanduka okoma. 9Kulikonse kumene mtsinjewo ukuyenda cholengedwa chilichonse chidzakhala ndi moyo. Nsombanso zidzakhala zambiri. Paja madzi amenewa amapita kumeneko kuti akakometse madzi ena. Choncho kulikonse kumene madziwa akuyenda chilichonse chidzakhala ndi moyo. 10Asodzi adzayima mʼmbali mwa Nyanja Yakufa. Pakuti kuchokera ku Eni-Gedi mpaka ku Eni Egilaimu kudzakhala malo oponyako makoka. Kudzakhala nsomba zamitundumitundu, monga nsomba za ku Nyanja Yayikulu. 11Koma mathawale ake ndi maiwe ake sadzakhala ndi madzi abwino; adzakhala ndi madzi a mchere. 12Mʼmbali zonse za mtsinje mudzamera mitengo ya zipatso zakudya za mtundu uliwonse. Masamba ake sadzafota kapena kulephera kubereka zipatso. Izidzabereka mwezi uliwonse, chifukwa madzi ake adzakhala ochokera ku Nyumba ya Mulungu. Zipatso zake anthu azidzadya ndipo masamba ake azidzachitira mankhwala.”

Malire a Dziko

13Ambuye Yehova akuti, “Nawa malire amene mudzatsate powagawira dziko mafuko khumi ndi awiri a Israeli aja. Yosefe adzalandire zigawo ziwiri. 14Mudzawagawire dzikolo mofanana. Paja ndinalumbira kwa makolo anu kuti dzikoli lidzakhala lanulanu.

15“Malire a dzikolo adzakhala motere:

Mbali ya kumpoto adzachokera ku Nyanja Yayikulu kutsata msewu wa ku Hetiloni mpaka ku chipata cha Hamoti ndi kupitirira ku Zedadi, 16Berota ndi Sibraimu (mizinda imene ili pakati pa malire a Damasiko ndi Hamati mpaka kukafika ku Hazeri Hatikoni mzinda umene uli mʼmalire mwa Haurani. 17Motero malire akumpoto adzachokera ku nyanja mpaka ku mzinda wa Hazari-Enoni, mʼmalire akumpoto a Damasiko ndi chakumpoto kwa malire a Hamati. Awa adzakhala malire a kumpoto.

18Mbali ya kummawa malire adzayenda pakati pa Haurani ndi Damasiko, mbali ya ku Yorodani pakati pa Giliyadi ndi dziko la Israeli, ku nyanja ya kummawa mpaka ku mzinda wa Tamara. Awa adzakhala malire akummawa.

19Mbali yakummwera malire adzayenda kuchokera ku dziwe la mzinda wa Tamara mpaka ku madzi a ku Meriba Kadesi. Kenaka ndi kutsata chigwa cha ku Igupto mpaka ku Nyanja Yayikulu. Awa adzakhala malire akummwera.

20Mbali ya kumadzulo, malire adzakhala Nyanja Yayikulu mpaka pa malo oyangʼanana ndi Lebo Hamati. Awa adzakhala malire akumadzulo.”

21“Mugawane dziko limeneli pakati panu potsata mafuko a Israeli. 22Muligawe kuti likhale cholowa chanu ndiponso cholowa cha alendo amene akukhala pakati panu, nakhala ndi ana pakati panu. Inu muwatenge monga mbadwa za mu Israeli. Adzapatsidwe cholowa chawo pamodzi ndi inu pakati pa mafuko a Israeli. 23Mu fuko lililonse kumene mlendoyo akukhala mumupatse cholowa chake.” Ndikutero Ine Ambuye Yehova.

New International Version – UK

Ezekiel 47:1-23

The river from the temple

1The man brought me back to the entrance to the temple, and I saw water coming out from under the threshold of the temple towards the east (for the temple faced east). The water was coming down from under the south side of the temple, south of the altar. 2He then brought me out through the north gate and led me round the outside to the outer gate facing east, and the water was trickling from the south side.

3As the man went eastward with a measuring line in his hand, he measured off a thousand cubits47:3 That is, about 530 metres and then led me through water that was ankle-deep. 4He measured off another thousand cubits and led me through water that was knee-deep. He measured off another thousand and led me through water that was up to the waist. 5He measured off another thousand, but now it was a river that I could not cross, because the water had risen and was deep enough to swim in – a river that no-one could cross. 6He asked me, ‘Son of man, do you see this?’

Then he led me back to the bank of the river. 7When I arrived there, I saw a great number of trees on each side of the river. 8He said to me, ‘This water flows towards the eastern region and goes down into the Arabah,47:8 Or the Jordan Valley where it enters the Dead Sea. When it empties into the sea, the salty water there becomes fresh. 9Swarms of living creatures will live wherever the river flows. There will be large numbers of fish, because this water flows there and makes the salt water fresh; so where the river flows everything will live. 10Fishermen will stand along the shore; from En Gedi to En Eglaim there will be places for spreading nets. The fish will be of many kinds – like the fish of the Mediterranean Sea. 11But the swamps and marshes will not become fresh; they will be left for salt. 12Fruit trees of all kinds will grow on both banks of the river. Their leaves will not wither, nor will their fruit fail. Every month they will bear fruit, because the water from the sanctuary flows to them. Their fruit will serve for food and their leaves for healing.’

The boundaries of the land

13This is what the Sovereign Lord says: ‘These are the boundaries of the land that you will divide among the twelve tribes of Israel as their inheritance, with two portions for Joseph. 14You are to divide it equally among them. Because I swore with uplifted hand to give it to your ancestors, this land will become your inheritance.

15‘This is to be the boundary of the land:

‘On the north side it will run from the Mediterranean Sea by the Hethlon road past Lebo Hamath to Zedad, 16Berothah47:15,16 See Septuagint and 48:1; Hebrew road to go into Zedad, 16 Hamath, Berothah. and Sibraim (which lies on the border between Damascus and Hamath), as far as Hazer Hattikon, which is on the border of Hauran. 17The boundary will extend from the sea to Hazar Enan,47:17 Hebrew Enon, a variant of Enan along the northern border of Damascus, with the border of Hamath to the north. This will be the northern boundary.

18On the east side the boundary will run between Hauran and Damascus, along the Jordan between Gilead and the land of Israel, to the Dead Sea and as far as Tamar.47:18 See Syriac; Hebrew Israel. You will measure to the Dead Sea. This will be the eastern boundary.

19On the south side it will run from Tamar as far as the waters of Meribah Kadesh, then along the Wadi of Egypt to the Mediterranean Sea. This will be the southern boundary.

20On the west side, the Mediterranean Sea will be the boundary to a point opposite Lebo Hamath. This will be the western boundary.

21‘You are to distribute this land among yourselves according to the tribes of Israel. 22You are to allot it as an inheritance for yourselves and for the foreigners residing among you and who have children. You are to consider them as native-born Israelites; along with you they are to be allotted an inheritance among the tribes of Israel. 23In whatever tribe a foreigner resides, there you are to give them their inheritance,’ declares the Sovereign Lord.