Ezekieli 47 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 47:1-23

Mtsinje Wotuluka Mʼnyumba ya Mulungu

1Munthuyo anabwerera nane ku chipata cha Nyumba ya Mulungu. Ndinaona madzi akutuluka kunsi kwa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu chakummawa; poti Nyumba ya Mulungu inayangʼana kummawa. Madziwo ankachokera kunsi kwa mbali yakummwera ya Nyumba ya Mulungu; kummwera kwa guwa lansembe. 2Ananditulutsira pa chipata chakumpoto ndipo anazungulira nane panja mpaka ku chipata chakunja choyangʼana kummawa. Ndipo ndinaona madzi akutuluka chakummwera kwa chipatacho.

3Munthuyo anapita chakummawa ali ndi chingwe choyezera mʼdzanja lake. Iye anayeza mamita 500, ndipo pambuyo pake analowa nane mʼmadziwo amene ankalekeza mʼkakolo. 4Anayezanso mamita 500 ndipo analowa nane mʼmadzi amene amalekeza mʼmawondo. Iye anayezanso mamita 500 ndipo analowa nane mʼmadzi amene amalekeza mʼchiwuno. 5Munthuyo anayezanso mamita 500, ndipo madziwo anasanduka mtsinje woti sindikanatha kuwoloka, pakuti madziwo anakwera, ndipo anali ozama ofunika kusambira pofuna kuwoloka. 6Munthuyo anandifunsa kuti: “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi?”

Kenaka anabwerera nane ku gombe la mtsinjewo. 7Nditafika pa gombepo, ndinaona mitengo yambiri ku mbali iliyonse ya mtsinjewo. 8Tsono munthuyo anandiwuza kuti, “Madziwa akupita ku chigawo chakummawa ndi kutsikira ku chigwa cha Araba. Kenaka akathira mʼNyanja Yakufa, ndipo akakalowa mʼnyanjayo, madzi a nyanjayo adzasanduka okoma. 9Kulikonse kumene mtsinjewo ukuyenda cholengedwa chilichonse chidzakhala ndi moyo. Nsombanso zidzakhala zambiri. Paja madzi amenewa amapita kumeneko kuti akakometse madzi ena. Choncho kulikonse kumene madziwa akuyenda chilichonse chidzakhala ndi moyo. 10Asodzi adzayima mʼmbali mwa Nyanja Yakufa. Pakuti kuchokera ku Eni-Gedi mpaka ku Eni Egilaimu kudzakhala malo oponyako makoka. Kudzakhala nsomba zamitundumitundu, monga nsomba za ku Nyanja Yayikulu. 11Koma mathawale ake ndi maiwe ake sadzakhala ndi madzi abwino; adzakhala ndi madzi a mchere. 12Mʼmbali zonse za mtsinje mudzamera mitengo ya zipatso zakudya za mtundu uliwonse. Masamba ake sadzafota kapena kulephera kubereka zipatso. Izidzabereka mwezi uliwonse, chifukwa madzi ake adzakhala ochokera ku Nyumba ya Mulungu. Zipatso zake anthu azidzadya ndipo masamba ake azidzachitira mankhwala.”

Malire a Dziko

13Ambuye Yehova akuti, “Nawa malire amene mudzatsate powagawira dziko mafuko khumi ndi awiri a Israeli aja. Yosefe adzalandire zigawo ziwiri. 14Mudzawagawire dzikolo mofanana. Paja ndinalumbira kwa makolo anu kuti dzikoli lidzakhala lanulanu.

15“Malire a dzikolo adzakhala motere:

Mbali ya kumpoto adzachokera ku Nyanja Yayikulu kutsata msewu wa ku Hetiloni mpaka ku chipata cha Hamoti ndi kupitirira ku Zedadi, 16Berota ndi Sibraimu (mizinda imene ili pakati pa malire a Damasiko ndi Hamati mpaka kukafika ku Hazeri Hatikoni mzinda umene uli mʼmalire mwa Haurani. 17Motero malire akumpoto adzachokera ku nyanja mpaka ku mzinda wa Hazari-Enoni, mʼmalire akumpoto a Damasiko ndi chakumpoto kwa malire a Hamati. Awa adzakhala malire a kumpoto.

18Mbali ya kummawa malire adzayenda pakati pa Haurani ndi Damasiko, mbali ya ku Yorodani pakati pa Giliyadi ndi dziko la Israeli, ku nyanja ya kummawa mpaka ku mzinda wa Tamara. Awa adzakhala malire akummawa.

19Mbali yakummwera malire adzayenda kuchokera ku dziwe la mzinda wa Tamara mpaka ku madzi a ku Meriba Kadesi. Kenaka ndi kutsata chigwa cha ku Igupto mpaka ku Nyanja Yayikulu. Awa adzakhala malire akummwera.

20Mbali ya kumadzulo, malire adzakhala Nyanja Yayikulu mpaka pa malo oyangʼanana ndi Lebo Hamati. Awa adzakhala malire akumadzulo.”

21“Mugawane dziko limeneli pakati panu potsata mafuko a Israeli. 22Muligawe kuti likhale cholowa chanu ndiponso cholowa cha alendo amene akukhala pakati panu, nakhala ndi ana pakati panu. Inu muwatenge monga mbadwa za mu Israeli. Adzapatsidwe cholowa chawo pamodzi ndi inu pakati pa mafuko a Israeli. 23Mu fuko lililonse kumene mlendoyo akukhala mumupatse cholowa chake.” Ndikutero Ine Ambuye Yehova.

La Bible du Semeur

Ezéchiel 47:1-23

Le fleuve issu du Temple

1L’individu me ramena vers l’entrée du Temple. Et je vis que de l’eau jaillissait de dessous le seuil du Temple, du côté oriental, la façade du Temple étant à l’est, et l’eau s’écoulait du côté sud de l’édifice en passant au sud de l’autel. 2L’individu me fit sortir par la porte nord et m’en fit contourner l’extérieur jusqu’à la porte extérieure orientale. Je vis l’eau sourdre du côté droit de cette porte.

3L’individu s’éloigna vers l’est, un cordeau à la main. Il mesura mille coudées en aval et me fit traverser l’eau ; elle m’arrivait jusqu’aux chevilles. 4Il mesura encore mille coudées et me fit de nouveau traverser : l’eau me venait jusqu’aux genoux. Il mesura encore mille coudées et me fit traverser : l’eau me venait jusqu’à la taille. 5Il mesura encore mille coudées : maintenant c’était un torrent que je ne pouvais plus franchir, car l’eau était si profonde qu’il fallait nager. On ne pouvait plus le traverser autrement. 6Il me dit : Fils d’homme, as-tu vu ?

Puis il me ramena sur le bord du torrent. 7Lorsque j’y fus revenu, j’aperçus, sur les deux rives, des arbres en très grand nombre. 8Le personnage me dit : Ces eaux s’écoulent vers la région est du pays, elles descendent dans la plaine du Jourdain et se jetteront dans la mer Morte. Quand elles se déverseront dans la mer, celle-ci sera assainie. 9Partout où passera le double torrent, les animaux foisonneront et pourront vivre, et il y aura beaucoup de poissons, car ces eaux viendront assainir la mer, et la vie se développera sur tout le passage du torrent47.9 Dans l’état actuel, aucun poisson ne peut vivre dans la mer Morte.. 10Sur les rives de la mer s’établiront des pêcheurs depuis Eyn-Guédi jusqu’à Eyn-Eglaïm47.10 Eyn-Guédi: sur la rive occidentale de la mer Morte (Jos 15.62). Eyn-Eglaïm: sur la rive est ou nord., on étendra des filets et les poissons de toute espèce seront très abondants, tout comme dans la mer Méditerranée. 11Mais ses marais et ses lagunes ne seront pas assainis, ils seront laissés en salines. 12Le long du torrent, sur chacune de ses rives, croîtront toutes sortes d’arbres fruitiers dont le feuillage restera toujours vert et dont les fruits ne s’épuiseront jamais. Chaque mois ils porteront de nouveaux fruits grâce aux eaux provenant du sanctuaire. Leurs fruits seront bons à manger et leurs feuilles serviront de remèdes.

Le partage du pays

13Voici ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : Vous délimiterez les lots du pays pour le partager entre les douze tribus d’Israël de la façon suivante. Les descendants de Joseph auront deux parts. 14Vous recevrez le pays en possession, chacun ayant une part équivalente à celle de l’autre. Car j’ai juré de le donner à vos ancêtres, et il vous reviendra comme patrimoine.

15Voici les limites du pays : la frontière nord partira de la mer Méditerranée et passera par Hetlôn, puis par Tsedad, 16Hamath, Bérota47.16 Hamath: à environ 200 kilomètres au nord de Damas. C’était la capitale d’un royaume araméen sur les rives de l’Oronte (Nb 13.21). Hetlôn, puis… 16 Hamath, Bérota: selon le texte hébreu traditionnel. L’ancienne version grecque a : Hetlôn, Lebo-Hamath, Tsedad, 16 puis Bérota (voir 48.1)., Sibraïm qui se trouve entre la frontière de Damas et celle de Hamath, et Hatzer-Hattikôn qui est sur la frontière du Haurân47.16 District à l’est du lac de Galilée au sud de Damas et au nord-est du Basan.. 17La frontière s’étendra donc depuis la mer Méditerranée jusqu’à Hatsar-Enôn, sur la frontière de Damas, puis, vers le nord, jusqu’à Tsaphôn et la frontière de Hamath. Telle sera la limite du côté nord.

18Du côté est, vous ferez partir la frontière entre le Haurân et Damas, et vous la ferez passer entre Galaad et le pays d’Israël, le long du Jourdain depuis la frontière nord jusqu’à la mer Morte47.18 depuis la frontière nord jusqu’à la mer Morte: selon le texte hébreu traditionnel. L’ancienne version grecque a : jusqu’à Tamar, sur la mer… (voir v. 19).. Telle sera la limite du côté est47.18 Le territoire de la tribu de Galaad à l’est du Jourdain ne faisait pas partie du territoire alloué primitivement à Israël (Nb 34.12)..

19Du côté du Néguev, au sud, la frontière ira de Tamar jusqu’aux eaux de Meriba de Qadesh, puis longera le torrent d’Egypte47.19 Qadesh: voir Nb 34.4. Le torrent d’Egypte: sans doute le Wadi el-Arich qui se jette dans la Méditerranée à quelque 80 kilomètres au sud de Gaza. jusqu’à la mer Méditerranée. Telle sera la limite du côté sud vers le Néguev. 20Et du côté ouest, elle sera marquée par la mer Méditerranée, depuis la frontière sud jusqu’en face de Lebo-Hamath. Telle sera la limite occidentale.

Le partage entre les tribus

21Vous vous partagerez ce pays entre les tribus d’Israël. 22Vous le répartirez en tirant au sort les parts de patrimoine pour vous et pour les étrangers qui résident au milieu de vous et qui ont eu là des enfants. Vous les traiterez comme les Israélites de souche, ils tireront leurs parts au sort avec vous, au milieu des tribus d’Israël. 23C’est dans la tribu même où l’étranger est installé que vous lui donnerez son patrimoine, le Seigneur, l’Eternel, le déclare.