Ezekieli 46 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 46:1-24

1“Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano. 2Mfumu izilowa podzera mʼkhonde la mʼkati la chipata pochokera kunja, nʼkudzayima pafupi ndi nsanamira yapakhomo. Ansembe apereke nsembe yake yopsereza ndi nsembe yake yachiyanjano. Mfumuyo ipembedze pa chiwundo cha pa chipatacho kenaka nʼkutuluka. Koma chipatacho asachitseke mpaka madzulo. 3Anthu a mʼdziko azipembedza pamaso pa Yehova pa khomo la chipata chimenechi pa masiku a sabata ndi pa tsiku la mwezi watsopano. 4Nsembe yopsereza imene mfumu iyenera kupereka kwa Yehova ikhale motere: pa tsiku la Sabata izipereka ana ankhosa aamuna asanu ndi mmodzi wopanda chilema, ndiponso nkhosa yayima yopanda chilema. 5Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, mfumu izipereka nsembe ya chakudya yokwanira efa imodzi. Pamodzi ndi ana ankhosa, mfumu izipereka monga ikufunira kutero. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse ya tirigu. 6Pa tsiku la mwezi watsopano mfumuyo ipereke mwana wangʼombe wamwamuna, ana ankhosa asanu ndi mmodzi ndiponso nkhosa yayimuna, zonsezi zopanda chilema. 7Ipereke efa imodzi ya tirigu pa ngʼombe yayimuna iliyonse ndiponso efa ina pa nkhosa yayimuna iliyonse. Pa ana ankhosa ipereke tirigu monga ikufunira kutero. Pamodzi ndi efa ya tirigu, ipereke hini imodzi ya mafuta. 8Pamene mfumu ikulowa, izidzera mʼkhonde lamʼkati la chipata chakummawa, izitulukiranso pomwepo.

9“Anthu a mʼdzikomo akabwera kudzapembedza Yehova pa masiku a chikondwerero, ngati munthu alowera pa chipata chakumpoto atulukire chipata chakummwera. Munthu wolowera chipata chakummwera, atulukire chipata chakumpoto. Munthu asatulukire pomwe walowera, koma atulukire pa chipata choyangʼanana nacho. 10Mfumu izidzakhala pakati pawo. Anthu akamadzalowa mfumu idzalowa nawo. Anthu akamadzatuluka mfumu idzatuluka nawo.

11“Pa masiku achikondwerero ndi pa masiku ena osankhidwa, zopereka za chakudya zikhale zokwanira efa imodzi pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, efa imodzinso ndi nkhosa yayimuna, koma pa mwana wankhosa apereke monga angathere. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse. 12Pamene mfumu ikufuna kupereka chopereka chaufulu kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena zopereka za chiyanjano, ayitsekulire chipata chakummawa. Iyo ipereke nsembe yopsereza kapena zopereka zake za chiyanjano monga imachitira pa tsiku la Sabata. Kenaka ituluke ndipo mfumuyo itatuluka, atseke chitsekocho.

13“Tsiku lililonse nthawi ya mmawa azipereka kwa Yehova mwana wankhosa wa chaka chimodzi. 14Pamodzi ndi nyamayo aziperekanso mmawa uliwonse chopereka cha chakudya chokwanira chimodzi mwa zigawo zisanu ndi chimodzi za efa. Aziperekanso chimodzi mwa zigawo zitatu za hini ya mafuta okandira ufa wosalala. Chopereka cha chakudya chimenechi chiziperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mwa lamulo. 15Motero azipereka mwana wankhosa ndi chopereka cha chakudya ndi mafuta mmawa uliwonse kuti zikhale nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku.

16“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ngati kalonga apereka mphatso chigawo cha cholowa chake kwa mmodzi mwa ana ake, mphatsoyo idzakhala ya ana akewo. Idzakhala yawo chifukwa ndi cholowa chawo. 17Koma ngati ipereka mphatso yotere kuchokera pa cholowa chake kwa mmodzi mwa antchito ake, mphatsoyo idzakhala ya wantchitoyo mpaka chaka chaufulu. Pambuyo pake idzabwereranso kwa kalongayo chifukwa cholowa chake ndi cha ana ake. 18Kalonga asalande cholowa chilichonse cha anthu, kuwachotsa mʼdera lawo la dziko. Iye apereke kwa ana ake cholowa chawo chochokera pa chuma chakechake, kuti pasapezeke ndi mmodzi yemwe mwa anthu anga wolandidwa chuma chake.’ ”

19Kenaka munthu uja anandidzeretsa pa khomo la pambali pa chipata nandilowetsa ku zipinda za ansembe zoyangʼana kumpoto. Ndipo ndinaona kumeneko malo chakumadzulo kwa zipindazo. 20Munthuyo anandiwuza kuti, “Awa ndi malo amene ansembe adzaphikirapo nsembe yopepesera kupalamula ndi nsembe yopepesera machimo. Kumenekonso azidzawotcherako chopereka cha chakudya. Sadzatuluka nazo zoyerazi mʼbwalo lakunja kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu ena.”

21Pambuyo pake anandilowetsa mʼbwalo lakunja napita nane ku ngodya zinayi za bwalolo. Ndipo ndinaona mʼkati mwa ngodya iliyonse bwalo lina. 22Motero pa ngodya zinayi za bwalo panalinso mabwalo ena angʼonoangʼono. Mabwalo amenewa anali ofanana. Mulitali mwake munali mamita makumi awiri ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi ndi asanu. 23Kuzungulira mabwalo anayi angʼonoangʼono aja panali mpanda wamiyala, ndi malo asonkhapo moto omangidwa mʼmunsi mwa mpandawo mozungulira. 24Munthuyo anandiwuza kuti, “Izi ndi zipinda zophikiramo. Mʼmenemu anthu otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzaphikiramo nyama za nsembe za anthu.”

O Livro

Ezequiel 46:1-24

1Diz o Senhor Deus: A entrada do lado da parede interior, a oriente, estará fechada durante os seis dias úteis e só se abrirá no sábado e nos dias das celebrações da lua nova. 2O príncipe entrará pela entrada exterior da passagem e permanecerá junto à ombreira da porta, enquanto o sacerdote oferece os seus holocaustos e ofertas de paz. Ele adorará no interior da passagem e depois regressará à entrada, a qual não será fechada antes do anoitecer. 3O povo adorará o Senhor em frente desta passagem, nos sábados e nos dias das celebrações da lua nova.

4Os holocaustos que o príncipe oferece ao Senhor nos dias de sábado consistirão em seis cordeiros e um carneiro, todos sem o mínimo defeito. 5Apresentará uma oferta de cereais de 22 litros de farinha, para acompanhar o carneiro, e também uma outra quantidade, desta vez conforme o que ele entender, para acompanhar cada cordeiro. Trará também 3,8 litros de azeite por cada 22 litros de farinha. 6Na celebração da lua nova trará um novilho perfeito, seis cordeiros e um carneiro sem qualquer imperfeição. 7Com o novilho trará 22 litros de farinha para uma oferta de cereais. Com o carneiro trará também 22 litros de farinha. Com o cordeiro trará aquilo que ele quiser dar. Por cada quantidade de 22 litros de farinha oferecerá 3,8 litros de azeite.

8O príncipe poderá entrar e sair pela passagem. 9Mas quando o povo entrar pela passagem do norte, para sacrificar durante as festas religiosas, deverá depois sair pelo lado sul. E os que entrarem pelo lado sul sairão pela passagem oposta, a do norte. Nunca sairão pelo sítio por onde entraram; deverão sempre utilizar a passagem oposta. 10O príncipe entrará e sairá juntamente com o povo nestas ocasiões.

11Para resumir: Nas celebrações especiais e nas festas sagradas, as ofertas de cereais serão constituídas por 22 litros de farinha a acompanhar o novilho; o mesmo para acompanhar o carneiro; tanto quanto ele quiser para acompanhar o cordeiro; 3,8 litros de azeite por cada quantidade de 22 litros de farinha. 12Sempre que o príncipe oferecer um holocausto ou uma oferta voluntária de paz, para serem sacrificados ao Senhor, o portão interior oriental será aberto para que possa entrar e oferecer os seus sacrifícios, como acontece aos sábados. Depois voltar-se-á e sairá, após o que a porta será fechada sobre ele.

13Todas as manhãs, um cordeiro de um ano será sacrificado como holocausto ao Senhor. 14Haverá também, todas as manhãs, uma oferta de cereais de 3,8 litros de farinha, com 1,3 litros de azeite misturados. Isto é um regulamento permanente. 15O cordeiro, a oferta de cereal e o azeite serão fornecidos em cada manhã para esse holocausto diário.

16Diz o Senhor Deus: Se o príncipe der uma oferta de terra a um dos seus filhos, pertencer-lhe-á sempre. 17Mas se der uma oferta de terra a um dos seus servos, este conservá-la-á até ao ano da liberdade, ano em que se tornará livre; nessa altura, a terra retornará ao seu primeiro possuidor, o príncipe. Apenas os dons concedidos aos seus filhos terão carácter permanente. 18Aliás, o príncipe nunca poderá subtrair a propriedade duma outra pessoa pela violência. Se der um presente de terra aos seus filhos, deverá ser das suas possessões privadas, pois não quero que o meu povo perca o que lhe pertence e que por isso tenha de abandonar a terra.”

19Depois disso, usando a porta através da parede do lado da passagem principal, conduziu-me pela entrada até ao bloco dos quartos sagrados, virados para o lado norte. Ali, no extremo oeste dessas câmaras, vi um lugar onde, 20pelo que me foi dito pelo homem que me guiava, os sacerdotes cozem o alimento do sacrifício de culpa e da oferta pelo pecado, e onde cozem o pão com a farinha das ofertas de cereais; fazem-no aqui para evitar ter de carregar os sacrifícios através do átrio exterior, para que o povo não toque naquilo que é sagrado.

21Tornou a trazer-me para o átrio exterior e levou-me a cada um dos quatro cantos do átrio. 22Vi que havia em cada canto uma câmara de 20 metros de comprimento por 15 metros de largura, rodeada por paredes. 23Debaixo das muralhas, em toda a volta, havia uma fila de fornos de tijolo. 24Explicou-me depois que esses fornos era onde os auxiliares do templo, os levitas, coziam os sacrifícios que o povo oferecia.