Ezekieli 46 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 46:1-24

1“Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano. 2Mfumu izilowa podzera mʼkhonde la mʼkati la chipata pochokera kunja, nʼkudzayima pafupi ndi nsanamira yapakhomo. Ansembe apereke nsembe yake yopsereza ndi nsembe yake yachiyanjano. Mfumuyo ipembedze pa chiwundo cha pa chipatacho kenaka nʼkutuluka. Koma chipatacho asachitseke mpaka madzulo. 3Anthu a mʼdziko azipembedza pamaso pa Yehova pa khomo la chipata chimenechi pa masiku a sabata ndi pa tsiku la mwezi watsopano. 4Nsembe yopsereza imene mfumu iyenera kupereka kwa Yehova ikhale motere: pa tsiku la Sabata izipereka ana ankhosa aamuna asanu ndi mmodzi wopanda chilema, ndiponso nkhosa yayima yopanda chilema. 5Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, mfumu izipereka nsembe ya chakudya yokwanira efa imodzi. Pamodzi ndi ana ankhosa, mfumu izipereka monga ikufunira kutero. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse ya tirigu. 6Pa tsiku la mwezi watsopano mfumuyo ipereke mwana wangʼombe wamwamuna, ana ankhosa asanu ndi mmodzi ndiponso nkhosa yayimuna, zonsezi zopanda chilema. 7Ipereke efa imodzi ya tirigu pa ngʼombe yayimuna iliyonse ndiponso efa ina pa nkhosa yayimuna iliyonse. Pa ana ankhosa ipereke tirigu monga ikufunira kutero. Pamodzi ndi efa ya tirigu, ipereke hini imodzi ya mafuta. 8Pamene mfumu ikulowa, izidzera mʼkhonde lamʼkati la chipata chakummawa, izitulukiranso pomwepo.

9“Anthu a mʼdzikomo akabwera kudzapembedza Yehova pa masiku a chikondwerero, ngati munthu alowera pa chipata chakumpoto atulukire chipata chakummwera. Munthu wolowera chipata chakummwera, atulukire chipata chakumpoto. Munthu asatulukire pomwe walowera, koma atulukire pa chipata choyangʼanana nacho. 10Mfumu izidzakhala pakati pawo. Anthu akamadzalowa mfumu idzalowa nawo. Anthu akamadzatuluka mfumu idzatuluka nawo.

11“Pa masiku achikondwerero ndi pa masiku ena osankhidwa, zopereka za chakudya zikhale zokwanira efa imodzi pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, efa imodzinso ndi nkhosa yayimuna, koma pa mwana wankhosa apereke monga angathere. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse. 12Pamene mfumu ikufuna kupereka chopereka chaufulu kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena zopereka za chiyanjano, ayitsekulire chipata chakummawa. Iyo ipereke nsembe yopsereza kapena zopereka zake za chiyanjano monga imachitira pa tsiku la Sabata. Kenaka ituluke ndipo mfumuyo itatuluka, atseke chitsekocho.

13“Tsiku lililonse nthawi ya mmawa azipereka kwa Yehova mwana wankhosa wa chaka chimodzi. 14Pamodzi ndi nyamayo aziperekanso mmawa uliwonse chopereka cha chakudya chokwanira chimodzi mwa zigawo zisanu ndi chimodzi za efa. Aziperekanso chimodzi mwa zigawo zitatu za hini ya mafuta okandira ufa wosalala. Chopereka cha chakudya chimenechi chiziperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mwa lamulo. 15Motero azipereka mwana wankhosa ndi chopereka cha chakudya ndi mafuta mmawa uliwonse kuti zikhale nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku.

16“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ngati kalonga apereka mphatso chigawo cha cholowa chake kwa mmodzi mwa ana ake, mphatsoyo idzakhala ya ana akewo. Idzakhala yawo chifukwa ndi cholowa chawo. 17Koma ngati ipereka mphatso yotere kuchokera pa cholowa chake kwa mmodzi mwa antchito ake, mphatsoyo idzakhala ya wantchitoyo mpaka chaka chaufulu. Pambuyo pake idzabwereranso kwa kalongayo chifukwa cholowa chake ndi cha ana ake. 18Kalonga asalande cholowa chilichonse cha anthu, kuwachotsa mʼdera lawo la dziko. Iye apereke kwa ana ake cholowa chawo chochokera pa chuma chakechake, kuti pasapezeke ndi mmodzi yemwe mwa anthu anga wolandidwa chuma chake.’ ”

19Kenaka munthu uja anandidzeretsa pa khomo la pambali pa chipata nandilowetsa ku zipinda za ansembe zoyangʼana kumpoto. Ndipo ndinaona kumeneko malo chakumadzulo kwa zipindazo. 20Munthuyo anandiwuza kuti, “Awa ndi malo amene ansembe adzaphikirapo nsembe yopepesera kupalamula ndi nsembe yopepesera machimo. Kumenekonso azidzawotcherako chopereka cha chakudya. Sadzatuluka nazo zoyerazi mʼbwalo lakunja kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu ena.”

21Pambuyo pake anandilowetsa mʼbwalo lakunja napita nane ku ngodya zinayi za bwalolo. Ndipo ndinaona mʼkati mwa ngodya iliyonse bwalo lina. 22Motero pa ngodya zinayi za bwalo panalinso mabwalo ena angʼonoangʼono. Mabwalo amenewa anali ofanana. Mulitali mwake munali mamita makumi awiri ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi ndi asanu. 23Kuzungulira mabwalo anayi angʼonoangʼono aja panali mpanda wamiyala, ndi malo asonkhapo moto omangidwa mʼmunsi mwa mpandawo mozungulira. 24Munthuyo anandiwuza kuti, “Izi ndi zipinda zophikiramo. Mʼmenemu anthu otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzaphikiramo nyama za nsembe za anthu.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Езекиил 46:1-24

1Так говорит Владыка Вечный:

– Ворота, ведущие во внутренний двор, обращённые к востоку, должны быть заперты шесть рабочих дней, а в субботу и в день новолуния46:1 Суббота – седьмой день недели у иудеев, день, посвящённый Вечному. В этот день, согласно повелению Вечного, исроильский народ должен был отдыхать и совершать ритуальные жертвоприношения (см. Исх. 31:12-17; Чис. 28:9-10). Новолуние – исроильтяне, пользовавшиеся лунным календарём, праздновали начало каждого месяца, которое совпадало с новолунием (см. Чис. 28:11-15). пусть их открывают. 2Вождь будет входить извне через притвор ворот и встанет у их столба. Священнослужители будут приносить его всесожжение и жертвы примирения. Он поклонится у порога ворот и выйдет обратно, но ворота будут открыты до вечера. 3По субботам и в дни новолуния народ страны будет поклоняться Вечному у входа в пассаж ворот. 4Всесожжение, которое вождь будет приносить в субботу, – это шесть ягнят и баран, животные без недостатков. 5Хлебное приношение при баране – четырнадцать килограммов муки, а при ягнятах – сколько он даст. На каждые четырнадцать килограммов муки полагается четыре литра46:5 Букв.: «одну ефу… один гин»; также в ст. 7 и 11. оливкового масла. 6В день новолуния пусть он приносит молодого быка, шестерых ягнят и барана, животных без недостатков. 7Пусть на быка и на барана он даёт в хлебное приношение четырнадцать килограммов муки, а на ягнят – сколько сможет. На каждые четырнадцать килограммов муки полагается четыре литра оливкового масла. 8Входя, вождь будет проходить через притвор ворот и там же выходить.

9Когда народ страны будет приходить на поклонение Вечному по установленным праздникам, пусть те, кто входит поклоняться через северные ворота, выходят через южные, а кто входит через южные, пусть выходят через северные. Пусть никто не возвращается через ворота, в которые он вошёл. Пусть все выходят через противоположные ворота. 10Вождь будет входить с ними, и с ними выходить.

11На торжествах и в установленные праздники хлебное приношение составляет четырнадцать килограммов муки на молодого быка и барана, а на ягнят – кто сколько даст. На каждые четырнадцать килограммов муки полагается четыре литра оливкового масла. 12Если вождь решит принести добровольное пожертвование Вечному, будь то всесожжение или жертва примирения, пусть для него откроют ворота, что смотрят на восток. Он принесёт всесожжение или жертву примирения, как в субботу. Он выйдет, и ворота за ним закроют.

13Каждый день приносите годовалого ягнёнка без недостатков для всесожжения Вечному. Приносите его каждое утро. 14Приносите вместе с ним каждое утро хлебное приношение, состоящее из двух с половиной килограммов лучшей муки и полутора литров46:14 Букв.: «шестой части ефы… третьей части гина». оливкового масла, чтобы смешать с мукой. Правила для этого приношения Вечному останутся в силе навеки. 15Ягнёнка с хлебным приношением и оливковым маслом следует приносить каждое утро для постоянного всесожжения.

О наследии надела вождя

16Так говорит Владыка Вечный:

– Если вождь подарит землю из своего надела одному из сыновей, то она будет принадлежать и его потомкам. Она станет клановым владением. 17Но если он подарит землю надела одному из слуг, то слуга будет владеть ею лишь до года освобождения. Потом земля вновь вернётся к вождю. Надел вождя принадлежит лишь его сыновьям; он принадлежит им. 18Вождь не может брать себе наделов народа, сгоняя их с земли. Пусть он даст сыновьям наследие из своего надела, чтобы никто из Моего народа не лишился владений.

Кухни храма

19Затем провожатый провёл меня через проход, находившийся сбоку от ворот, к северной галерее священных комнат, которые принадлежали священнослужителям, и указал мне на место в её западном конце.

20Он сказал мне:

– Здесь священнослужители будут готовить мясо жертвы повинности и жертвы за грех и печь хлебное приношение, чтобы не выносить их во внешний двор и не причинять вред народу46:20 Букв.: «для освящения народа»..

21Он привёл меня во внешний двор и провёл по четырём его углам. В каждом из углов я увидел ещё по двору. 22В четырёх углах внешнего двора были малые дворы – по двадцать метров в длину и пятнадцать метров46:22 Букв.: «сорок… тридцать локтей». в ширину. Каждый из дворов в четырёх углах был одного размера. 23Внутри каждый из них был обнесён каменной стеной со встроенными в неё очагами.

24Он сказал мне:

– Это кухни, где служители храма будут готовить мясо жертв, приносимых народом.