Ezekieli 43 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 43:1-27

Ulemerero Ubwerera Mʼnyumba ya Mulungu

1Pambuyo pake munthuyo anapita nane ku chipinda choyangʼana kummawa, 2ndipo ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ukubwera kuchokera kummawa. Liwu lake linali ngati mkokomo wamadzi, ndipo dziko linawala ndi ulemerero wake. 3Masomphenya amene ndinawaonawa anali ngati masomphenya amene ndinawaona pamene Yehova anabwera kudzawononga mzinda ndiponso ngati masomphenya amene ndinawaona ku mtsinje wa Kebara. Ndipo ndinadzigwetsa chafufumimba. 4Ulemerero wa Yehova unalowa mʼNyumba ya Mulungu kudzera pa chipata choyangʼana kummawa. 5Tsono Mzimu unandinyamula nundilowetsa mʼbwalo lamʼkati, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.

6Munthuyo ali chiyimire pambali panga, ndinamva wina akundiyankhula kuchokera mʼNyumba ya Mulungu. 7Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi malo a mpando wanga waufumu, ndi malo opondapo mapazi anga. Pano ndiye pamene ndidzakhala pakati pa Aisraeli mpaka muyaya. Aisraeliwa kapena mafumu awo sadzayipitsa dzina langa popembedza milungu ina kapena poyika mitembo ya mafumu awo ku zitunda zachipembedzo. 8Ankamanga chiwundo chawo pafupi ndi chiwundo changa, ndiponso mphuthu zawo pafupi ndi mphuthu zanga, nʼkungokhala khoma chabe pakati pa iwowo ndi Ine. Motero anayipitsa dzina langa loyera ndi machitidwe awo onyansa. Choncho Ine ndinawawononga ndili wokwiya. 9Tsopano alekeretu kupembedza milungu ina ndipo achotseretu mitembo ya mafumu awo, isakhale pafupi ndi Ine, ndipo Ine ndidzakhala pakati pawo mpaka muyaya.

10“Iwe mwana wa munthu, awuze Aisraeliwa za Nyumba ya Mulunguyi, mamangidwe ake ndipo achite manyazi ndi machimo awo, 11akachita manyazi ndi zoyipa zonse anachita, uwafotokozera za Nyumba ya Mulungu, mamangidwe ake, makomo ake otulukira ndi makomo olowera, ndiye kuti, mamangidwe ake onse. Uwafotokozerenso malangizo ndi malamulo ake. Uwalembe akuona kuti athe kuwasunga ndi kuwachita.

12“Limeneli ndi lamulo la Nyumba ya Mulungu imene idzamangidwe pamwamba pa phiri. Malo ake onse ozungulira adzakhala oyera kwambiri. Limeneli ndilo lamulo la Nyumba ya Mulungu.

Guwa la Nsembe

13“Miyeso ya guwa lansembe ndi iyi: Pa tsinde pake padzakhala ngalande ya masentimita makumi asanu kuzama kwake ndi mulifupi mwake. Mʼphepete mwa ngalandeyo kuzungulira guwa lonse, mudzakhala mkombero wa masentimita 25. 14Kuchokera mʼngalande ya pansi padzakhala mpaka pa phaka lapansi mita imodzi, mulifupi mwake theka la mita. Kuchokera pa phaka lalingʼono mpaka pa phaka lalikulu, msinkhu wake ndi mamita awiri, mulifupi mwake ndi masentimita makumi asanu. 15Malo osonkhapo moto pa guwa, msinkhu wake udzakhala mamita awiri. Pa ngodya iliyonse ya malo osonkhapo motowo panatuluka nyanga imodzi. 16Malo osankhalapo moto pa guwa lansembe miyeso yake ndi yofanana mbali zonse. Mulitali mwake mudzakhala mamita asanu ndi limodzi ndipo mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi limodzi. 17Phaka lapamwamba muyeso wake udzakhala wofanana mbali zonse. Mulitali mudzakhala mamita asanu ndi awiri ndiponso mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi awiri. Mkombero wake udzakhala wa masentimita 25 ndiponso ngalande yake yozungulira idzakhala ya masentimita 25. Makwerero a guwa lansembe adzayangʼana kummawa.”

18Kenaka munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, Ambuye Yehova akuti: Guwalo litamangidwa, tsono malamulo awa azidzatsatidwa popereka nsembe zopsereza ndiponso powaza magazi pa guwapo. 19Udzawapatse ansembe, omwe ndi Alevi, a banja la Zadoki, amene amabwera pafupi nane kudzanditumikira, mwana wangʼombe wamwamuna kuti aperekere nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 20Udzatengeko magazi ake ena ndi kuwapaka pa nyanga zinayi za pa guwa lansembe, pa ngodya zinayi za phaka ndiponso mozungulira mkombero wonse. Motero udzaliyeretsa ndi kulipatula. 21Udzatenge ngʼombe yayimuna yomwe yaperekedwa ngati nsembe yopepesera machimo, ndipo udzayiwotche pa malo ake enieni mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, kunja kwa malo opatulika.

22“Mmawa mwake udzatenge mbuzi yopanda chilema kuti nayonso iperekedwe ngati nsembe yopepesera machimo. Pambuyo pake idzayeretse guwa lansembe monga unachitira ndi ngʼombe yayimuna ija. 23Utatha kuyeretsa guwa lansembelo, udzatenge mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndiponso nkhosa yayimuna yopanda chilema. 24Udzapereke zonsezi pamaso pa Yehova, ndipo ansembe adzazithire mchere ndi kuzipereka kuti zikhale nsembe zopsereza kwa Yehova.

25“Kwa masiku asanu ndi awiri, uzidzapereka tsiku ndi tsiku mbuzi yayimuna, mwana wangʼombe, ndiponso nkhosa kuti zikhale nsembe zopepesera machimo. Zonsezi zidzakhale zopanda chilema. 26Kwa masiku asanu ndi awiriwo ansembe adzachite mwambo woyeretsa ndi kupatula guwa lansembelo. 27Masiku amenewa atatha, kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu, ansembe azipereka nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe. Apo ndidzakulandirani. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

La Bible du Semeur

Ezéchiel 43:1-27

Le Seigneur vient dans son temple

1Puis le personnage me conduisit vers la porte orientale. 2Alors la gloire du Dieu d’Israël arriva par le côté est. Sa voix était comme celle des grandes eaux et la terre était illuminée de sa gloire43.2 Pour les v. 2-3, voir 1.1-3 ; 10.19 ; 8.4 et note ; 11.23.. 3La vision que je contemplais était semblable à celle que j’avais eue lorsqu’il était venu pour détruire la ville, et à celle que j’avais eue sur les bords du fleuve Kebar. Je tombai sur ma face.

4La gloire de l’Eternel entra dans le Temple par la porte orientale.

5L’Esprit m’enleva et me transporta dans le parvis intérieur : la gloire de l’Eternel remplissait le Temple43.5 Comme lors de la consécration du temple de Salomon (1 R 8.11).. 6Tandis que le personnage se tenait toujours à mes côtés, j’entendis quelqu’un qui me parlait depuis l’intérieur de la maison. 7Il me dit : Fils d’homme, c’est ici le lieu de mon trône, le lieu où je poserai mes pieds et où j’habiterai pour toujours au milieu des Israélites. Et ni la communauté d’Israël, ni ses rois ne me profaneront plus, moi qui suis saint, par leurs prostitutions, par les cadavres de leurs rois sur leurs hauts lieux43.7 Au lieu de sur leurs hauts lieux, certains manuscrits ont, moyennant une vocalisation légèrement différente : au moment de la mort de ceux-ci., 8ou en accolant le seuil de leurs demeures contre mon seuil, et les montants de leurs portes contre les miens, de sorte qu’il n’y avait qu’un mur mitoyen entre eux et moi43.8 Le palais des rois où l’on adorait les idoles n’était séparé du Temple que par un mur.. Oui, ils m’ont ainsi profané, moi qui suis saint, par les abominations qu’ils ont commises. C’est pour cela que je les ai consumés dans ma colère. 9Désormais, ils éloigneront de moi leurs prostitutions ainsi que les cadavres de leurs rois, et j’habiterai pour toujours au milieu d’eux.

10Quant à toi, fils d’homme, décris ce temple à la communauté d’Israël pour qu’ils aient honte de leurs péchés, et qu’ils mesurent les plans de cet édifice. 11Et s’ils ont vraiment honte de tout ce qu’ils ont fait, fais-leur connaître la configuration de ce temple, sa structure, ses entrées et ses sorties, oui, toute sa configuration, et toutes les prescriptions et les lois qui lui sont relatives. Mets-les par écrit sous leurs yeux et qu’ils obéissent à cette configuration et à ces prescriptions pour les appliquer. 12C’est ici la loi du Temple qui se trouve au sommet de la montagne : son territoire tout autour est très saint. Oui, telle est la loi du Temple.

Le culte dans le nouveau temple

13Et voici les dimensions de l’autel, données en grandes coudées, c’est-à-dire une coudée étant augmentée d’une paume : tout autour de la base de l’autel court un fossé ayant une coudée de profondeur et autant de largeur ; il est entouré d’un rebord d’une paume. Pour la hauteur de l’autel, 14depuis la base de l’autel, enterrée dans le sol, jusqu’au socle inférieur, il y a deux coudées. La section suivante est d’une coudée en retrait et, depuis le petit socle jusqu’au grand, elle a quatre coudées de haut. Puis vient un nouveau rebord d’une coudée de large. 15Le sommet de l’autel, avec le foyer43.15 En hébreu : la montagne de Dieu, terme qui n’apparaît qu’ici dans l’Ancien Testament. C’est un mot technique babylonien qui désigne le sommet de l’autel., a quatre coudées de hauteur, il est surmonté de quatre cornes. 16Ce foyer forme un carré de douze coudées de côté. 17Le grand socle est également un carré ayant quatorze coudées de côté avec un rebord d’une demi-coudée tout autour et un fossé d’une coudée tout autour. Les marches pour monter à l’autel se trouvent du côté est.

18Le personnage me dit : Fils d’homme, voici ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : Les prescriptions concernant l’autel pour le jour où il sera construit afin d’y offrir l’holocauste et d’y faire l’aspersion du sang sont les suivantes : 19tu remettras un jeune taureau comme sacrifice pour le péché aux prêtres-lévites qui sont de la postérité de Tsadoq et qui s’approchent de moi pour officier pour mon culte ; le Seigneur, l’Eternel, le déclare. 20Tu prendras de son sang et tu l’appliqueras sur les quatre cornes de l’autel ainsi que sur les quatre angles du socle et sur le rebord qui l’entoure ; tu purifieras ainsi l’autel et tu accompliras le rite d’expiation pour lui. 21Tu prendras ensuite le taureau qui a été offert pour le péché et tu le brûleras dans le lieu du Temple réservé à cet usage, en dehors du sanctuaire.

22Le second jour, tu offriras pour le péché un jeune bouc sans défaut et l’on purifiera l’autel comme on l’a fait avec le taureau. 23Quand tu auras terminé ce rite de purification, tu offriras un jeune taureau sans défaut et un bélier sans défaut pris dans le troupeau. 24Tu les présenteras devant l’Eternel ; les prêtres jetteront du sel43.24 Voir Lv 2.13. sur eux et les offriront en holocaustes à l’Eternel. 25Pendant sept jours consécutifs, tu offriras chaque jour un bouc en sacrifice pour le péché, puis un jeune taureau et un bélier sans défaut pris dans le troupeau. 26Pendant sept jours, on accomplira le rite d’expiation pour l’autel, on le purifiera et on le consacrera. 27Une fois ces jours passés, les prêtres offriront sur l’autel, le huitième jour et les jours suivants, vos holocaustes et vos sacrifices de communion, et je vous agréerai, le Seigneur, l’Eternel, le déclare.