Ezekieli 41 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 41:1-26

1Ndipo munthuyo anapita nane mʼchipinda chopatulika cha Nyumba ya Mulungu ndipo anayeza khonde lake; mulifupi mwa khondelo munali mamita atatu mbali iliyonse kutalika kwake. 2Mulifupi mwa khomo munali motalika mamita asanu. Makoma a mbali zonse anali a mamita awiri ndi theka mulifupi mwake. Anayezanso kutalika kwa chipinda chopatulika chija ndipo mulitali mwake munali motalika mamita makumi awiri ndi mulifupi mwake munali mamita khumi.

3Kenaka munthuyo anakalowa mʼkati ndipo anayeza khonde la pa khomo; khondelo linali mita imodzi mulifupi mwake. Mulifupi mwa khondelo munali mamita atatu. 4Ndiponso anayeza kutalika kwa chipinda chopatulika chenichenicho. Mulitali mwake munali mamita khumi, ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi. Munthuyo anandiwuza kuti, “Ichi ndicho chipinda chopatulika kwambiri.”

5Tsono munthuyo anayeza khoma la Nyumba ya Mulungu; kuchindikira kwake kunali mamita atatu. Panalinso zipinda zina kuzungulira Nyumba ya Mulungu ndipo chilichonse chinali cha mamita awiri mulifupi wake. 6Zipindazo zinali zitatu zosanjikizana. Chigawo chilichonse chinali ndi zipinda makumi atatu. Pa makoma a Nyumba ya Mulungu panali zochirikiza zipindazo kuti zisatsamire khoma la Nyumba ya Mulungu. 7Zipinda za mʼmbalizo zinkapita zikulirakulira pomakwera chipinda ndi chipinda potsata kukulirakulira kwa zochirikiza za zipinda zija. Pambali pa Nyumba ya Mulungu panali makwerero okwerera pamwamba, kuchokera chigawo chapansi kudzera chapakati, mpaka kukafika pamwamba.

8Ndinaona chiwundo kuzungulira Nyumba ya Mulungu. Chinapanga maziko a zipindazo ndipo chinali cha mamita atatu. 9Khoma lakunja la zipindazo linali la mamita awiri ndi theka kuchindikira kwake. Pakati pa chiwundocho 10ndi zipinda za Nyumba ya Mulungu panali bwalo limeneli la mamita khumi kupingasa kwake kuzungulira Nyumba yonse ya Mulungu. 11Zitseko za zipinda zamʼmbalizo zinali zotsekulira ku chiwundo. Chitseko chimodzi chinkayangʼana kumpoto ndipo china chinkayangʼana kummwera. Chiwundo chosamangapo kanthu chinali mamita awiri ndi theka kukula kwake kuzungulira ponseponse.

12Nyumba imene inali chakummwera moyangʼanana ndi bwalo la Nyumba ya Mulungu inali mamita 35 mulifupi mwake. Khoma la nyumbayo linali mamita awiri ndi theka kuchindikira kwake kuzungulira ponseponse, ndipo mulitali mwake linali mamita 45.

13Ndipo munthuyo anayeza Nyumba ya Mulungu ndipo mulitali mwake inali mamita makumi asanu. Nyumbayo ndi makoma ake, zonse zinali za mamita makumi asanu. 14Kumaso kwa Nyumba ya Mulungu chakummawa kwa bwalolo mulifupi mwake munali mamita makumi asanu.

15Kenaka anayeza kutalika kwa nyumba yoyangʼanana ndi bwalo chakumadzulo kwa Nyumba ya Mulungu, kuphatikizapo njira zamʼkati ku mbali iliyonse. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.

Chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu, chimene chili chamʼkati, khonde lamʼkati loyangʼanana ndi bwalo, 16mazenera ndi maferemu ake, zonsezi zinali zokutidwa ndi matabwa. Pamwamba moyangʼanana ndi chiwundo, Nyumba ya Mulungu inakutidwa ndi matabwa kuyambira pansi mpaka ku mazenera, (mazenerawo anali okutidwa), 17pamwamba pa khomo lolowera ku malo opatulika amʼkati komanso kuzungulira makoma onse kunja ndi mʼkati, 18anajambulapo zithunzi za kerubi mmodzi atakhala pakati pa kanjedza muwiri. Kerubi aliyense anali ndi nkhope ziwiri: 19imodzi inali nkhope ya munthu yoyangʼana kanjedza mbali imodzi, ndi ina inali nkhope ya mkango yoyangʼana kanjedza mbali ina. Zinajambulidwa kuzungulira Nyumba ya Mulungu yonse. 20Motero kuyambira pansi mpaka pamwamba pa khomo komanso pa makoma onse a chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu, anajambula zithunzi za akerubi ndi kanjedza pa makoma onse a malo opatulika.

21Mphuthu za chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu kutalika kwake mbali zonse kunali kofanana. Ndipo kumaso kwa malo opatulika kunali chinthu china chooneka ngati 22guwa lansembe la matabwa. Msinkhu wake unali mita imodzi ndi theka, mulitali mwake munali mita imodzi, mulifupi mwake munalinso mita imodzi. Mphuthu zake, tsinde lake ndi mbali zonse zinali za matabwa. Munthuyo anandiwuza kuti, “Tebulo limeneli ndilo limakhala pamaso pa Yehova.” 23Chipinda chachikulu chija chinali ndi zitseko ziwiri. Malo opatulika aja analinso ndi zitseko ziwiri. 24Chitseko chilichonse chinali ndi zigawo ziwiri zopatukana. 25Ndipo pa zitsekopo anajambulipo zithunzi za akerubi ndi kanjedza monga zomwe anajambulapo pa makoma. Kunja kwake kunali ngati denga lamatabwa pamwamba pa khonde lamʼkati. 26Pa mbali zonse za khonde lamʼkatilo panali mazenera, ndipo pa makoma ake onse anajambulapo zithunzi za kanjedza.

Bibelen på hverdagsdansk

Ezekiels Bog 41:1-26

Det hellige og det allerhelligste

1Derefter førte han mig videre hen til selve tempelhallen, og han målte de to dørstolper, som døren sad fast i. De var hver 3 m brede. 2Døren var 5 m bred og væggene på begge sider af døren var 2,5 m brede. Tempelhallen var indvendig 20 m lang og 10 m bred.

3Så gik han hen til indgangen til det inderste rum. Dørstolperne ved den indgang var hver en meter brede. Døren var 3 m bred og væggene på begge sider af døren var hver 3,5 m brede. 4Det inderste rum var 10 m på hver led. „Rummet her er det allerhelligste,” forklarede han.

5Så gik han udenfor igen og målte tempelhallens mur: Den var 3 m tyk. Der var en tilbygning med rum hele vejen rundt om templets yderside mod syd, vest og nord. Hvert rum var 2 m bredt. 6-7Tilbygningen havde tre etager, og der var 30 rum på hver etage. Tempelhallens mur var bredest forneden og gik en tak indad to gange, så tilbygningens støttebjælker havde en hylde at hvile på. Bjælkerne var altså ikke bygget ind i tempelmuren, men lå på en afsats. Derfor var tilbygningens midterste etage bredere end den nederste, og den øverste var lige så meget bredere igen i forhold til den midterste. Der var trapper fra nederste etage gennem den midterste til den øverste etage.

8Rundt om hele templet var der bygget et fundament, som var 3 m højt, og tilbygningen med de mange rum var bygget oven på det fundament. 9Tilbygningens ydermur var 2,5 m tyk, og uden for muren var der et åbent stykke som en terrasse. 10Hele vejen rundt var der et åbent stykke på 10 m, indtil man kom til de andre værelser.41,10 Teksten er uklar. 11Der var to døre i tilbygningen, hvoraf en vendte mod nord og en mod syd. Dørene åbnede ud mod den åbne terrasse, som var 2,5 m bred.

12Vest for tempelhallen var der en baggård, hvori der lå en bygning, som var 35 m bred og 45 m lang, og dens mure var på alle sider 2,5 m tykke. 13Derpå målte manden længden fra øst til vest af tempelhallen plus tilbygningen. Den var 50 m. Og han målte længden af baggården med dens bygning og mur. Den var også 50 m. 14Derpå målte han bredden fra syd til nord af tempelhallen plus den indre forgård. Den var også 50 m. 15Han havde nu målt baggården og dens bygning med dens balkoner.

Både det ydre og indre rum i tempelhallen samt forhallen var indvendig beklædt med træpaneler. 16Træpanelerne gik fra gulvet op til vinduerne, som der var gitter for.41,16 Som flere andre steder i disse kapitler er originalteksten vanskelig at tyde. 17Væggen over døren ind til det allerhelligste var også beklædt med paneler. 18-20Alle væggene var udsmykket med udskårne billeder af keruber og palmer fra gulvet til op over dørene. Der var skiftevis en kerub og en palme hele vejen rundt på templets indervæg. Keruberne havde to ansigter. Deres menneskeansigt så i retning af palmen på den ene side, mens deres løveansigt så i retning af palmen på den anden side.

21Dørstolperne ved indgangen til det ydre rum i tempelhallen var firkantede, og det samme gjaldt dørstolperne ind til det indre rum. 22Foran indgangen til det indre rum stod røgelsesalteret. Det var 1,5 m højt, 1 m bredt og 1 m langt. Dets hjørner, fodstykke og sider var helt igennem af træ. „Dette alter viser, at Herren er nær,” forklarede manden.

23-24Både indgangen til det ydre og indre rum i templet havde dobbelte fløjdøre, 25der ligesom væggene var udsmykket med keruber og palmemotiver. Over indgangen til forhallen var der desuden et udhæng af træ. 26Der var også palmemotiver på forhallens vægge rundt omkring vinduerne.