Ezekieli 4 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 4:1-17

Chionetsero cha Kuzingidwa kwa Yerusalemu

1Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu. 2Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo. 3Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.

4“Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo. 5Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.

6“Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi. 7Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu. 8Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.

9“Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi. 10Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha. 11Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku. 12Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.” 13Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”

14Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”

15Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”

16Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha. 17Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Езекиил 4:1-17

Пророчество об осаде Иерусалима

1– А ты, смертный, возьми кирпич, положи его перед собой и нарисуй на нём город Иерусалим. 2Устрой против него осаду: сооруди укрепления, насыпь осадный вал, расположи под ним стан и окружи его стенобитными орудиями. 3Возьми железный противень, поставь его железной стеной между собой и городом и повернись к нему лицом. Он будет осаждён, а ты осаждай его. Это будет знамением исроильтянам.

4Ты же ляг на левый бок и возложи на себя4:4 Или: «на него». беззаконие4:4 Или: «наказание»; также в ст. 5 и 6. Исроила. Неси их беззаконие столько дней, сколько будешь лежать на боку. 5Я определил тебе столько дней, сколько лет они грешили: триста девяносто дней ты будешь нести беззаконие Исроила. 6Когда исполнишь это, ляг снова, но теперь на правый бок, и неси беззаконие Иудеи. Я определил тебе сорок дней, по дню за каждый год4:6 Хотя сложно приурочить данные числа к каким-либо историческим периодам и вехам, общий смысл пророчества очевиден: продолжительность осады Иерусалима, как наказания за его грехи, каким-то образом будет соответствовать числу лет нечестия и беззаконий исроильского народа.. 7Обрати лицо и обнажённую руку к осаждённому Иерусалиму и пророчествуй против него. 8Смотри, Я налагаю на тебя путы, чтобы ты не мог перевернуться с одного бока на другой, пока не окончишь дней осады.

9Возьми пшеницу и ячмень, фасоль и чечевицу, просо и полбу, положи в один сосуд и сделай себе лепёшки. Ты будешь есть их те триста девяносто дней, что будешь лежать на боку. 10Отвесь по двести сорок граммов4:10 Букв.: «двадцать шекелей». лепёшек, чтобы съедать каждый день, и ешь их в установленное время. 11Также отмерь один литр4:11 Букв.: «шестую часть гина». воды и пей в установленное время. 12Ешь свои лепёшки, как если бы они были ячменными; пеки их на глазах у людей на человеческом кале, – 13сказал Вечный. – Вот так народ Исроила будет есть осквернённую пищу среди тех народов, к которым Я их изгоню.

14Тогда я сказал:

– О нет, Владыка Вечный! Я никогда не осквернялся4:14 Исроильтяне должны были закапывать человеческий кал за городом или лагерем, им было запрещено использовать его как топливо (см. Втор. 23:12-14).. С юности и до сегодняшнего дня я никогда не ел ни мертвечины, ни растерзанного диким зверем. Нечистое мясо не входило в мои уста.

15– Хорошо, – сказал Он, – Я позволяю тебе печь твои лепёшки на коровьем навозе вместо человеческого кала.

16Потом Он сказал мне:

– Смертный, Я уничтожу запасы пищи в Иерусалиме. Люди будут есть свою порцию хлеба в тревоге и пить свою порцию воды в ужасе, 17потому что пищи и воды не будет хватать. Они будут ужасаться при виде друг друга и угасать из-за своего греха4:17 Или: «в своём грехе»..