Ezekieli 39 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 39:1-29

1“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala. 2Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli. 3Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja. 4Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo. 5Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 6Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’

7“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli. 8Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.

9“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri. 10Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.

11“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.

12“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko. 13Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.

14“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo. 15Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi. 16(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.

17“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi. 18Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani. 19Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera. 20Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.

21“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo. 22Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo. 23Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo. 24Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.

25“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera. 26Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine. 27Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera. 28Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo. 29Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Езекиил 39:1-29

1– Смертный, пророчествуй против Гога и скажи: Так говорит Владыка Вечный: «Я твой враг, Гог, верховный правитель Мешеха и Тувала. 2Я поверну тебя обратно и поволоку. Я выведу тебя с окраин севера и пошлю против гор Исроила. 3Я выбью у тебя лук из левой руки и рассыплю стрелы из правой. 4Ты падёшь в горах Исроила со своими воинами и народами. Я отдам тебя в пищу разным хищным птицам и диким зверям. 5Ты падёшь в открытом поле, потому что Я так сказал, – возвещает Владыка Вечный. – 6Я пошлю огонь на Магог и на тех, кто живёт в безопасности на побережье. Тогда они узнают, что Я – Вечный.

7Я возвещу Моё святое имя Моему народу Исроилу. Я не позволю впредь бесславить Моё святое имя, и народы узнают, что Я, Вечный, Святой в Исроиле. 8Он близится! Он непременно настанет, – возвещает Владыка Вечный, – день, о котором Я говорил.

9Жители исроильских городов выйдут собирать брошенное оружие, чтобы отправить его на топливо. Они будут разводить огонь из малых и больших щитов, луков и стрел, палиц и копий. Топлива им хватит на семь лет. 10Им не придётся собирать дрова в поле или рубить их в лесу: топливом у них будет оружие. Они оберут тех, кто их обирал, и ограбят тех, кто их грабил, – возвещает Владыка Вечный.

11В тот день Я дам Гогу место для погребения в Исроиле, в долине Аварим39:11 Или: «в долине Путешественников»., к востоку от моря39:11 То есть Мёртвого или Средиземного моря.. Оно преградит дорогу путешественникам, потому что там будут похоронены Гог и его полчища. Поэтому это место будет названо долиной Гамон-Гог («полчище Гога»).

12Семь месяцев исроильтяне будут хоронить их, чтобы очистить землю. 13Весь народ страны будет хоронить их и прославится этим в тот день, когда Я одержу победу, – возвещает Владыка Вечный.

14Будут назначены люди, чтобы всё время обходить землю, хоронить оставшихся на поверхности земли и очищать её. Они начнут поиски через семь месяцев. 15Люди будут обходить землю, и когда кто-нибудь из них увидит человеческую кость, он будет ставить рядом с ней знак, чтобы могильщики пришли и похоронили её в долине Гамон-Гог. 16(Там будет и город Гамона.) Так они очистят землю».

17А тебе, смертный, так говорит Владыка Вечный: Скажи разным птицам и диким зверям: «Собирайтесь отовсюду и отправляйтесь на жертвенный пир, который Я готовлю для вас, на великий жертвенный пир в горах Исроила. Вы будете есть мясо и пить кровь. 18Вы будете есть мясо могучих ратников и пить кровь правителей земли, словно бы они были баранами и ягнятами, козлами и молодыми быками – упитанной скотиной с плодородной Бошонской земли. 19На жертвенном пире, который Я готовлю для вас, вы досыта наедитесь жира и напьётесь крови. 20За Моим столом вы насытитесь мясом коней и колесничих, могучих ратников и разных военных людей», – возвещает Владыка Вечный.

21Я явлю народам Мою славу. Все народы увидят суд, который Я произвёл, и руку, которую Я на них опустил. 22С этого дня и впредь исроильтяне будут знать, что Я – Вечный, их Бог. 23Народы узнают, что исроильтяне отправились в плен за грехи, за то, что они были Мне неверны. За это Я скрыл от них лицо, отдал их во власть врагов, и все они пали от меча. 24Я поступил с ними по их нечистоте и преступлениям; Я скрыл от них Своё лицо.

25Поэтому так говорит Владыка Вечный:

– Теперь Я восстановлю потомков Якуба и помилую весь народ Исроила. Я возревную о Моём святом имени. 26Они смогут забыть о своём позоре и о неверности39:26 Или: «понесут бремя позора и неверности». Мне, когда будут снова жить в безопасности на своей земле, и никто не будет им угрожать. 27Вернув их из других народов и возвратив из вражеских стран, Я явлю через них Мою святость на глазах у многих народов. 28Они узнают, что Я – Вечный, их Бог, потому что, хотя Я и отправил их в плен к чужим народам, Я соберу их в их собственной стране, никого не забыв. 29Я больше не стану скрывать от них Своё лицо, когда изолью Моего Духа на народ Исроила, – возвещает Владыка Вечный.