Ezekieli 38 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 38:1-23

Za Chilango cha Gogi

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu. 3Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala. 4Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola. 5Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo. 6Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.

7“ ‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo. 8Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere. 9Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.

10“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa. 11Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo. 12Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’ 13Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’ ”

14“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka. 15Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu. 16Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.

17“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli. 18Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse. 19Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli. 20Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi. 21Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga. 22Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye. 23Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’ ”

New Russian Translation

Иезекииль 38:1-23

Пророчество против Гога

1Было ко мне слово Господа:

2– Сын человеческий, обрати лицо к Гогу в земле Магог, верховному правителю38:2 Или: «Гогу … правителю Роша»; также в ст. 3. Мешеха и Тувала. Пророчествуй против него 3и скажи: Так говорит Владыка Господь: «Я – твой враг, о Гог, верховный правитель Мешеха и Тувала. 4Я поверну тебя обратно, продену в твои челюсти крюки и выведу тебя и твою рать: коней, всадников во всеоружии и огромное полчище с большими и малыми щитами – всех, владеющих мечом, 5а с ними Персию, Куш и Пут, всех со щитами и в шлемах, 6Гомера с его воинами, и Бет-Тогарму с окраин севера с ее воинами – многие народы с тобою.

7Готовься и снаряжайся, ты сам и все полчища, которые собрались к тебе. Встань во главе их. 8Спустя много дней тебя позовут действовать. В будущие годы ты вторгнешься в страну, которая оправилась после войны, чей народ был собран от многих народов к горам Израиля, и которая долго находилась в запустении. Ее обитатели были уведены от других народов и теперь живут в безопасности. 9Ты со своими воинами и многими народами поднимешься и придешь, словно смерч; ты будешь, как туча, что закрывает землю».

10Так говорит Владыка Господь: «В тот день к тебе придут плохие мысли, и ты задумаешь коварный план. 11Ты скажешь: „Пойду на край неогражденных селений. Нападу на мирный народ, который живет безопасно: они живут без стен, нет у них ни засовов, ни ворот. 12Буду грабить и расхищать; обращу руку против вновь заселенных развалин и против людей, собранных из чужих народов, что богаты скотом и добром и живут посреди земли“. 13Шева и Дедан, купцы и все торговцы38:13 Вероятный текст; евр.: «молодые львы». Таршиша скажут тебе: „Ты пришел грабить? Ты собрал полчища, чтобы расхищать, уносить золото и серебро, отнимать скот и добро, и взять богатую добычу?“»

14Поэтому, сын человеческий, пророчествуй и скажи Гогу: «Так говорит Владыка Господь: В день, когда Мой народ, Израиль, будет жить в безопасности, разве ты об этом не узнаешь?38:14 В одном из древних переводов: «ты двинешься в путь». 15Ты выйдешь из своих мест, что на окраине севера, ты сам и многие народы с тобой, все они ездят на конях – огромное полчище, могучая рать. 16Ты двинешься на Мой народ, Израиль, как туча, что закрывает землю. В будущие дни, Гог, Я пошлю тебя на Мою землю, чтобы народы познали Меня, когда Я явлю через тебя у них на глазах Мою святость».

17Так говорит Владыка Господь: «Разве не о тебе Я издревле говорил через Моих слуг, пророков Израиля? Они годами пророчествовали в те времена о том, что Я нашлю тебя на них. 18Вот что случится в этот день: когда Гог нападет на Израиль, Мой пылающий гнев вспыхнет, – возвещает Владыка Господь. – 19В ревности и пылающем гневе Своем Я возвещаю: в это время в земле Израиля произойдет страшное землетрясение. 20Рыбы в морях, птицы в небе, звери в лесу, всякое пресмыкающееся, что ползает по земле, и все люди на лице земли затрепещут предо Мной. Горы рухнут, скалы низвергнутся, и всякая стена повалится на землю. 21Я призову меч сражаться против Гога на всех Моих горах, – возвещает Владыка Господь. – Каждый его воин обнажит меч на соратника. 22Я покараю его мором и кровопролитием. Я обрушу на него, на его воинства и многие народы неистовый ливень, град и горящую серу. 23Я явлю Свое величие и святость и откроюсь многим народам. Тогда они узнают, что Я – Господь».